< 2 Mafumu 9 >

1 Mneneri Elisa anayitanitsa mmodzi mwa ana a aneneri, namuwuza kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga botolo la mafuta mʼdzanja lako ndipo upite ku Ramoti Giliyadi.
A Jelisije prorok dozva jednoga izmeðu sinova proroèkih, i reèe mu: opaši se i uzmi ovu uljanicu, pa idi u Ramot Galadski.
2 Ukakafika kumeneko, ukafunefune Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi. Ukapite kwa iye, ukamuchotse pakati pa anzake ndi kukamulowetsa mʼchipinda chamʼkati.
I kad doðeš onamo, vidjeæeš ondje Juja sina Josafata sina Nimsijina, i ušavši izvedi ga izmeðu braæe njegove i odvedi ga u najtajniju klijet.
3 Ndipo ukatenge botololi ndi kuthira mafuta pa mutu wake ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’ Kenaka ukatsekule chitseko ndi kuthawa ndipo usakachedwe!”
I uzmi uljanicu i izlij mu na glavu, i reci: ovako veli Gospod: pomazah te za cara nad Izrailjem. Zatijem otvori vrata i bježi, i ne zabavljaj se.
4 Choncho mneneri wachinyamatayo anapita ku Ramoti Giliyadi.
I otide mladiæ, momak prorokov, u Ramot Galadski.
5 Atafika ku Giliyadiko anapeza atsogoleri a ankhondo ali pa msonkhano. Iye anati, “Mtsogoleri, ine ndili ndi uthenga wanu.” Ndipo Yehu anafunsa kuti, “Uthengawo ndi wa yani pakati pathu?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndi wa inuyo, mtsogoleri.”
I kad uðe, gle, sjeðahu vojvode; a on reèe: vojvodo, imam nešto da ti kažem. A Juj mu reèe: kome izmeðu svijeh nas? A on reèe: tebi, vojvodo.
6 Yehu anayimirira nakalowa mʼnyumba. Pamenepo mneneriyo anakhuthulira mafuta pamutu pa Yehu ndipo ananena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndikukudzoza kukhala mfumu ya Israeli, anthu a Yehova.
Tada usta, i uðe u kuæu, a on mu izli na glavu ulje, i reèe mu: ovako veli Gospod Bog Izrailjev: pomazah te za cara nad narodom Gospodnjim, Izrailjem.
7 Uyenera kuwononga nyumba ya mbuye wako Ahabu ndipo ndidzabwezera imfa ya atumiki anga, aneneri ndiponso imfa ya atumiki ena onse a Yehova amene anaphedwa ndi Yezebeli.
I pobij dom Ahava gospodara svojega, jer hoæu da pokajem krv sluga svojih proroka, i krv svijeh sluga Gospodnjijeh od ruke Jezaveljine.
8 Banja lonse la Ahabu lidzatheratu. Ndidzachotsa munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu kaya ndi kapolo kapena mfulu.
I tako æe izginuti sav dom Ahavov, i istrijebiæu Ahavu i ono što uza zid mokri, i uhvaæenoga i ostavljenoga u Izrailju.
9 Ndidzachititsa kuti banja la Ahabu lifanane ndi banja la Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati banja la Baasa mwana wa Ahiya.
I uèiniæu s domom Ahavovijem kao s domom Jerovoama sina Navatova i kao s domom Vase sina Ahijina.
10 Kunena za Yezebeli, agalu adzamudya ku dera la Yezireeli ndipo palibe amene adzamuyike mʼmanda.’” Kenaka mneneriyo anatsekula chitseko nʼkuthawa.
I Jezavelju æe izjesti psi u polju Jezraelskom i neæe biti nikoga da je pogrebe. Potom otvori vrata i pobježe.
11 Yehu atatuluka kupita kumene kunali atsogoleri anzake, mmodzi mwa iwo anamufunsa kuti, “Kodi zonse zili bwino? Kodi munthu wamisala uja anabwera kudzatani kwa iwe?” Yehu anayankha kuti, “Iwe ukumudziwa munthu uja ndiponso ukudziwa zomwe amayankhula.”
A Juj izide k slugama gospodara svojega, i zapitaše ga: je li dobro? što je došao taj bezumnik k tebi? A on im reèe: znate èovjeka i besjedu njegovu.
12 Atsogoleri aja anati, “Ukunama! Tiwuze.” Yehu anati, “Zimene wandiwuza ndi izi: ‘Yehova akuti: Ine ndakudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’”
A oni rekoše: nije istina; kaži nam. A on im reèe: tako i tako reèe mi govoreæi: ovako veli Gospod: pomazah te za cara nad Izrailjem.
13 Atsogoleri aja mofulumira anatenga zofunda zawo naziyala pansi pa makwerero kuti Yehu akhalepo. Kenaka analiza lipenga, nafuwula kuti, “Yehu ndiye mfumu!”
Tada brže uzeše svak svoju haljinu, i metnuše poda nj na najvišem basamaku, i zatrubiše u trubu i rekoše: Juj posta car.
14 Choncho Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi, anachitira chiwembu Yoramu. (Nthawi imeneyi nʼkuti Yoramu ndi Aisraeli onse akuteteza Ramoti Giliyadi kwa Hazaeli mfumu ya ku Aramu,
Tako se pobuni Juj sin Josafata sina Nimsijina na Jorama; a Joram èuvaše Ramot Galadski sa svijem Izrailjem od Azaila cara Sirskoga.
15 koma nʼkuti Yoramu atabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene Aaramu anamuvulaza pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya ku Aramu.) Yehu anati, “Ngati mukugwirizana nazo zimenezi, wina aliyense asatuluke mu mzinda muno kupita kukafotokoza nkhaniyi ku Yezireeli.”
A bješe se vratio car Joram da se lijeèi u Jezraelu od rana koje mu zadaše Sirci, kad se bijaše s Azailom carem Sirskim. I reèe Juj: ako vam je volja, neka niko ne izlazi iz grada da otide i javi u Jezrael.
16 Pamenepo Yehu anakwera galeta lake, napita ku Yezireeli, chifukwa Yoramu anali akupumula kumeneko ndipo Ahaziya, mfumu ya ku Yuda, nʼkuti ali komweko kudzamuona.
I Juj sjede na kola i otide u Jezrael, jer Joram ležaše ondje; i Ohozija car Judin bješe došao da vidi Jorama.
17 Mlonda amene ankayimirira pa nsanja yolondera mzinda wa Yezireeli ataona gulu lankhondo la Yehu likuyandikira, anafuwula kuti, “Ndikuona gulu lankhondo likubwera.” Yoramu analamula kuti, “Peza munthu wokwera kavalo, mutume kuti akakumane nawo ndi kuwafunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’”
A stražar koji stajaše na kuli u Jezraelu, kad ugleda ljudstvo Jujevo gdje ide, reèe: neko ljudstvo vidim. Tada reèe Joram: uzmi konjika i pošlji ga pred njih, i neka zapita: je li mir?
18 Choncho munthu wokwera kavalo anapita kukakumana ndi Yehu ndipo anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.” Mlonda uja anakafotokoza kwa mfumu kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwerera.”
I otide konjik preda nj, i reèe: ovako veli car: je li mir? A Juj reèe: šta je tebi do mira? hajde za mnom. A stražar javi govoreæi: glasnik doðe do njih, ali se ne vraæa.
19 Choncho mfumu inatumanso munthu wina wachiwiri wokwera kavalo. Atafika kwa anthuwo iye anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.”
I posla drugoga konjika, koji kad doðe k njima reèe: ovako veli car: je li mir? A Juj reèe: šta je tebi do mira? hajde za mnom.
20 Mlonda uja anakanenanso kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwereranso. Kuyendako kukukhala ngati kwa Yehu mwana wa Nimisi, iye amayenda ngati munthu wamisala.”
Opet javi stražar govoreæi: doðe do njih, ali se ne vraæa; a hod kao da je hod Jujev, jer ide pomamno.
21 Yoramu analamula kuti, “Konzani galeta langa.” Ndipo atakonza galeta lake, Yoramu mfumu ya Israeli ndi Ahaziya mfumu ya ku Yuda anakwera nʼkutuluka mu mzindamo, aliyense atakwera galeta lake, kukakumana ndi Yehu. Iwo anakumana ndi Yehu pa munda umene unali wa Naboti, wa ku Yezireeli.
Tada reèe Joram: preži. I upregoše u kola njegova. Tako izide Joram car Izrailjev i Ohozija car Judin, svaki na svojim kolima, i otidoše na susret Juju, i sretoše ga na njivi Navuteja Jezraeljanina.
22 Yoramu ataona Yehu anafunsa kuti, “Yehu, kodi wabwera mwamtendere?” Yehu anayankha kuti, “Pangakhale bwanji mtendere pamene zopembedza mafano zonse zilipo ndiponso ufiti wa amayi ako Yezebeli uli ponseponse?”
I kad Joram ugleda Juja, reèe mu: je li mir, Juju? A on odgovori: kakav mir? dok je tolikoga kurvanja Jezavelje matere tvoje i èaranja njezinijeh.
23 Yoramu anatembenuka, nathawa akufuwula kwa Ahaziya kuti, “Ahaziya, anthuwa atiwukira!”
Tada Joram okrete se i pobježe govoreæi Ohoziji: izdaja, Ohozija!
24 Pamenepo Yehu anakoka uta wake ndipo analasa Yoramu kumsana pakati pa mapewa. Muviwo unakalasa mtima wake ndipo anagwa pansi mʼgaleta lakelo.
Ali Juj zgrabi luk svoj i ustrijeli Jorama meðu pleæi da mu strijela proðe kroz srce, te pade u kolima svojim.
25 Yehu anawuza Bidikara, mtsogoleri wa galeta lake kuti, “Munyamule ndipo ukamuponye mʼmunda umene unali wa Naboti wa ku Yezireeli, chifukwa kumbukira mmene iwe ndi ine tinkayenda pambuyo pa Ahabu abambo ake, kuti Yehova ananeneratu za iye kuti,
Tada reèe Juj Vadekaru vojvodi svom: uzmi ga, i baci ga na njivu Navuteja Jezraeljanina; jer opomeni se kad ja i ti zajedno jahasmo za Ahavom ocem njegovijem, kako Gospod izreèe za nj ovo zlo:
26 ‘Zoonadi dzulo ndinaona magazi a Naboti ndi magazi a ana ake, akutero Yehova, ndipo Ine ndidzakubwezera ndithu choyipa chimenechi pa munda womwe uno, akutero Yehova.’ Tsono munyamule ndipo ukamuponye mʼmundamo, potsatira zimene Yehova ananena.”
Zaista, krv Navutejevu i krv sinova njegovijeh vidjeh sinoæ, reèe Gospod, i platiæu ti na ovoj njivi, reèe Gospod. Zato uzmi ga sad i baci na tu njivu po rijeèi Gospodnjoj.
27 Ahaziya mfumu ya ku Yuda ataona zimene zinachitika, anathawira ku Beti Hagani. Yehu anamuthamangitsa, uku akufuwula kuti, “Mupheninso!” Iwo anamuvulaza ali mʼgaleta lakelo pa njira yopita ku Guri pafupi ndi Ibuleamu, koma iye anathawira ku Megido ndipo anakafera kumeneko.
A Ohozija car Judin vidjevši to pobježe k domu u vrtu; ali ga potjera Juj, i reèe: ubijte i toga na njegovijem kolima. I raniše ga na brdu Guru, koje je kod Ivleama. I uteèe u Megidon, i ondje umrije.
28 Antchito ake anamunyamulira mʼgaleta kupita naye ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide.
I sluge ga njegove metnuše na kola i odvezoše u Jerusalim, i pogreboše ga u grobu njegovu kod otaca njegovijeh u gradu Davidovu.
29 (Mʼchaka cha khumi ndi chimodzi cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu, Ahaziya anakhala mfumu ya ku Yuda).
A jedanaeste godine carovanja Jorama sina Ahavova poèe carovati Ohozija nad Judom.
30 Kenaka Yehu anapita ku Yezireeli. Yezebeli atamva zimene zinachitika, anapaka zodzikometsera mʼmaso, naluka tsitsi lake, namasuzumira pa zenera.
Iza toga Juj doðe u Jezrael. A Jezavelja kad èu, namaza lice svoje i nakiti glavu svoju, pa gledaše s prozora.
31 Pamene Yehu ankalowa pa chipata iye anafunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere, iwe Zimuri, munthu wopha mbuye wako?”
I kad Juj ulažaše na vrata, reèe ona: je li mir, Zimrije, krvnièe gospodara svojega?
32 Yehu anakweza maso nayangʼana pa zenera, ndipo anafuwula kuti, “Kodi ndani ali mbali yanga? Ndani?” Anthu ofulidwa awiri kapena atatu anayangʼana Yehu pansipo.
A on pogleda na prozor i reèe: ko je sa mnom? ko? Tada pogledaše u nj dva tri dvoranina.
33 Yehu anawawuza kuti, “Muponyeni pansi!” Motero anamuponya pansi ndipo magazi ake ena anafalikira pa khoma ndi pa akavalo pamene ankamupondaponda.
A on im reèe: bacite je dolje. I baciše je, i pršte krv njezina po zidu i po konjma, i pogazi je.
34 Yehu analowa mʼnyumba yaufumu ndipo anadya ndi kumwa. Kenaka iye anati, “Kamutoleni mkazi wotembereredwayo, ndipo kamuyikeni mʼmanda, popeza ndi mwana wa mfumu.”
Potom ušavši jede i pi, pa reèe: vidite onu prokletnicu, i pogrebite je, jer je carska kæi.
35 Koma atapita kuti akamuyike mʼmanda, sanapeze kanthu kupatula chibade cha mutu wokha, mapazi ake ndi manja ake.
I otidoše da je pogrebu, i ne naðoše od nje ništa do lubanju i stopala i šake.
36 Choncho iwo anabwerera kwa Yehu ndi kukamufotokozera kuti, “Mawu amene Yehova anayankhula kudzera mwa mtumiki wake Eliya wa ku Tisibe ndi awa: Pa munda wa ku Yezireeli agalu adzadya mtembo wa Yezebeli.
I doðoše natrag i javiše, a on reèe: to je rijeè Gospodnja, koju je rekao preko sluge svojega Ilije Tesviæanina govoreæi: u polju Jezraelskom izješæe psi tijelo Jezaveljino.
37 Mtembo wa Yezebeli udzakhala ngati zinyalala pa munda wa ku Yezireeli, kotero kuti palibe amene adzathe kunena kuti, ‘Uyu ndi Yezebeli.’”
Neka bude tijelo Jezaveljino kao gnoj na njivi u polju Jezraelskom da se ne može kazati: ovo je Jezavelja.

< 2 Mafumu 9 >