< 2 Mafumu 9 >

1 Mneneri Elisa anayitanitsa mmodzi mwa ana a aneneri, namuwuza kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga botolo la mafuta mʼdzanja lako ndipo upite ku Ramoti Giliyadi.
A prorok Elizeusz zawołał jednego z synów proroków i powiedział mu: Przepasz swoje biodra, weź do ręki ten dzban z oliwą i idź do Ramot-Gilead.
2 Ukakafika kumeneko, ukafunefune Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi. Ukapite kwa iye, ukamuchotse pakati pa anzake ndi kukamulowetsa mʼchipinda chamʼkati.
A gdy tam przybędziesz, zobaczysz tam Jehu, syna Jehoszafata, syna Nimsziego. Wejdź [tam], spraw, by powstał spośród swych braci i wprowadź go do najskrytszej komnaty.
3 Ndipo ukatenge botololi ndi kuthira mafuta pa mutu wake ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’ Kenaka ukatsekule chitseko ndi kuthawa ndipo usakachedwe!”
Następnie weź dzban oliwy, wylej na jego głowę i powiedz: Tak mówi PAN: Namaściłem cię na króla nad Izraelem. Potem otwórz drzwi i uciekaj, nie zwlekaj.
4 Choncho mneneri wachinyamatayo anapita ku Ramoti Giliyadi.
Poszedł więc ten młodzieniec – młody prorok – do Ramot-Gilead.
5 Atafika ku Giliyadiko anapeza atsogoleri a ankhondo ali pa msonkhano. Iye anati, “Mtsogoleri, ine ndili ndi uthenga wanu.” Ndipo Yehu anafunsa kuti, “Uthengawo ndi wa yani pakati pathu?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndi wa inuyo, mtsogoleri.”
A gdy przybył, oto dowódcy wojska siedzieli. A on powiedział: Wodzu! Mam do ciebie słowo. Jehu zapytał: Do którego z nas wszystkich? I odpowiedział: Do ciebie, wodzu!
6 Yehu anayimirira nakalowa mʼnyumba. Pamenepo mneneriyo anakhuthulira mafuta pamutu pa Yehu ndipo ananena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndikukudzoza kukhala mfumu ya Israeli, anthu a Yehova.
Wtedy wstał i wszedł do domu, a tamten wylał oliwę na jego głowę i powiedział mu: Tak mówi PAN, Bóg Izraela: Namaściłem cię na króla nad ludem PANA, nad Izraelem.
7 Uyenera kuwononga nyumba ya mbuye wako Ahabu ndipo ndidzabwezera imfa ya atumiki anga, aneneri ndiponso imfa ya atumiki ena onse a Yehova amene anaphedwa ndi Yezebeli.
Wytracisz dom Achaba, swego pana, ja bowiem pomszczę krew swoich sług, proroków i krew wszystkich sług PANA z ręki Jezabel.
8 Banja lonse la Ahabu lidzatheratu. Ndidzachotsa munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu kaya ndi kapolo kapena mfulu.
I tak zginie cały dom Achaba. Wytępię [z domu] Achaba każdego, aż do najmniejszego szczenięcia, każdego więźnia i opuszczonego w Izraelu.
9 Ndidzachititsa kuti banja la Ahabu lifanane ndi banja la Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati banja la Baasa mwana wa Ahiya.
I uczynię z domem Achaba jak z domem Jeroboama, syna Nebata, i jak z domem Baszy, syna Achiasza.
10 Kunena za Yezebeli, agalu adzamudya ku dera la Yezireeli ndipo palibe amene adzamuyike mʼmanda.’” Kenaka mneneriyo anatsekula chitseko nʼkuthawa.
Psy zjedzą Jezabel na polu Jizreel i nie będzie nikogo, kto ją pogrzebie. Potem otworzył drzwi i uciekł.
11 Yehu atatuluka kupita kumene kunali atsogoleri anzake, mmodzi mwa iwo anamufunsa kuti, “Kodi zonse zili bwino? Kodi munthu wamisala uja anabwera kudzatani kwa iwe?” Yehu anayankha kuti, “Iwe ukumudziwa munthu uja ndiponso ukudziwa zomwe amayankhula.”
A gdy Jehu wyszedł do sług swego pana, jeden z nich zapytał go: Czy wszystko dobrze? Po co ten szaleniec przyszedł do ciebie? Odpowiedział im: Wy znacie tego człowieka i jego słowa.
12 Atsogoleri aja anati, “Ukunama! Tiwuze.” Yehu anati, “Zimene wandiwuza ndi izi: ‘Yehova akuti: Ine ndakudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’”
Oni powiedzieli: To nieprawda. Powiedz, proszę. A on powiedział: Tak a tak przemówił do mnie: Tak mówi PAN: Namaściłem cię na króla nad Izraelem.
13 Atsogoleri aja mofulumira anatenga zofunda zawo naziyala pansi pa makwerero kuti Yehu akhalepo. Kenaka analiza lipenga, nafuwula kuti, “Yehu ndiye mfumu!”
Wtedy wszyscy pospiesznie wzięli swoje szaty, podłożyli je pod niego na najwyższym stopniu, zadęli w trąbę i zawołali: Jehu jest królem!
14 Choncho Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi, anachitira chiwembu Yoramu. (Nthawi imeneyi nʼkuti Yoramu ndi Aisraeli onse akuteteza Ramoti Giliyadi kwa Hazaeli mfumu ya ku Aramu,
Wtedy Jehu, syn Jehoszafata, syna Nimsziego, uknuł spisek przeciw Joramowi. (A w tym czasie Joram wraz z całym Izraelem strzegł Ramot-Gilead przed Chazaelem, królem Syrii.
15 koma nʼkuti Yoramu atabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene Aaramu anamuvulaza pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya ku Aramu.) Yehu anati, “Ngati mukugwirizana nazo zimenezi, wina aliyense asatuluke mu mzinda muno kupita kukafotokoza nkhaniyi ku Yezireeli.”
Lecz król Joram wrócił, by leczyć się w Jizreel z ran, które mu zadali Syryjczycy, gdy walczył z Chazaelem, królem Syrii). Jehu powiedział: Jeśli się na to zgadzacie, niech nikt nie wychodzi z miasta, aby pójść i oznajmić to w Jizreel.
16 Pamenepo Yehu anakwera galeta lake, napita ku Yezireeli, chifukwa Yoramu anali akupumula kumeneko ndipo Ahaziya, mfumu ya ku Yuda, nʼkuti ali komweko kudzamuona.
Następnie Jehu wsiadł na rydwan i pojechał do Jizreel, bo tam leżał Joram. Także Achazjasz, król Judy, przyjechał, aby odwiedzić Jorama.
17 Mlonda amene ankayimirira pa nsanja yolondera mzinda wa Yezireeli ataona gulu lankhondo la Yehu likuyandikira, anafuwula kuti, “Ndikuona gulu lankhondo likubwera.” Yoramu analamula kuti, “Peza munthu wokwera kavalo, mutume kuti akakumane nawo ndi kuwafunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’”
A gdy strażnik, który stał na wieży w Jizreel, zobaczył nadjeżdżający oddział Jehu, powiedział: Widzę oddział. Joram rzekł: Weź jeźdźca i wyślij [go] naprzeciw [nich], niech zapyta: Czy jest pokój?
18 Choncho munthu wokwera kavalo anapita kukakumana ndi Yehu ndipo anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.” Mlonda uja anakafotokoza kwa mfumu kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwerera.”
Jeździec więc wyruszył mu naprzeciw i zapytał: Tak mówi król: Czy jest pokój? Jehu odpowiedział: Co tobie do pokoju? Zawróć i [jedź] za mną. Strażnik oznajmił: Posłaniec dotarł do nich, ale nie wraca.
19 Choncho mfumu inatumanso munthu wina wachiwiri wokwera kavalo. Atafika kwa anthuwo iye anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.”
Wysłał więc drugiego jeźdźca, który przybył do nich i powiedział: Tak mówi król: Czy jest pokój? Jehu odpowiedział: Co tobie do pokoju? Zawróć i jedź za mną.
20 Mlonda uja anakanenanso kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwereranso. Kuyendako kukukhala ngati kwa Yehu mwana wa Nimisi, iye amayenda ngati munthu wamisala.”
Strażnik znowu oznajmił: Dotarł do nich, ale nie wraca. A jego jazda jest jak jazda Jehu, syna Nimsziego, bo jedzie jak szalony.
21 Yoramu analamula kuti, “Konzani galeta langa.” Ndipo atakonza galeta lake, Yoramu mfumu ya Israeli ndi Ahaziya mfumu ya ku Yuda anakwera nʼkutuluka mu mzindamo, aliyense atakwera galeta lake, kukakumana ndi Yehu. Iwo anakumana ndi Yehu pa munda umene unali wa Naboti, wa ku Yezireeli.
Wtedy Joram powiedział: Zaprzęgaj. Zaprzężono więc jego rydwan. I Joram, król Izraela, i Achazjasz, król Judy, wyjechali, każdy na swoim rydwanie. Wyjechali naprzeciw Jehu i spotkali go na polu Nabota Jizreelity.
22 Yoramu ataona Yehu anafunsa kuti, “Yehu, kodi wabwera mwamtendere?” Yehu anayankha kuti, “Pangakhale bwanji mtendere pamene zopembedza mafano zonse zilipo ndiponso ufiti wa amayi ako Yezebeli uli ponseponse?”
A gdy Joram zobaczył Jehu, zapytał: Czy jest pokój, Jehu? Odpowiedział: Co to za pokój, dopóki [trwają] cudzołóstwa Jezabel, twojej matki, i jej liczne czary.
23 Yoramu anatembenuka, nathawa akufuwula kwa Ahaziya kuti, “Ahaziya, anthuwa atiwukira!”
Wtedy Joram zawrócił i uciekł, mówiąc do Achazjasza: Zdrada, Achazjaszu!
24 Pamenepo Yehu anakoka uta wake ndipo analasa Yoramu kumsana pakati pa mapewa. Muviwo unakalasa mtima wake ndipo anagwa pansi mʼgaleta lakelo.
A Jehu wziął do rąk łuk i trafił Jorama między ramiona tak, że strzała przeszyła jego serce, a on padł na swój rydwan.
25 Yehu anawuza Bidikara, mtsogoleri wa galeta lake kuti, “Munyamule ndipo ukamuponye mʼmunda umene unali wa Naboti wa ku Yezireeli, chifukwa kumbukira mmene iwe ndi ine tinkayenda pambuyo pa Ahabu abambo ake, kuti Yehova ananeneratu za iye kuti,
Potem [Jehu] odezwał się do Bidkara, swego dowódcy: Weź go i porzuć na polu Nabota Jizreelity. Pamiętasz bowiem: gdy ja i ty jechaliśmy razem za Achabem, jego ojcem, PAN wydał przeciwko niemu ten wyrok:
26 ‘Zoonadi dzulo ndinaona magazi a Naboti ndi magazi a ana ake, akutero Yehova, ndipo Ine ndidzakubwezera ndithu choyipa chimenechi pa munda womwe uno, akutero Yehova.’ Tsono munyamule ndipo ukamuponye mʼmundamo, potsatira zimene Yehova ananena.”
Z pewnością widziałem wczoraj krew Nabota i krew jego synów – mówi PAN. I zemszczę się na tobie na tym polu – mówi PAN. Teraz więc weź go i porzuć na polu według słowa PANA.
27 Ahaziya mfumu ya ku Yuda ataona zimene zinachitika, anathawira ku Beti Hagani. Yehu anamuthamangitsa, uku akufuwula kuti, “Mupheninso!” Iwo anamuvulaza ali mʼgaleta lakelo pa njira yopita ku Guri pafupi ndi Ibuleamu, koma iye anathawira ku Megido ndipo anakafera kumeneko.
Gdy zobaczył to Achazjasz, król Judy, zaczął uciekać drogą do domu ogrodowego. Lecz Jehu ścigał go i polecił: Tego także zabijcie na jego rydwanie. I [zranili go] na wzniesieniu Gur, które jest przy Jibleam. Uciekł do Megiddo i tam umarł.
28 Antchito ake anamunyamulira mʼgaleta kupita naye ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide.
Jego słudzy przewieźli go do Jerozolimy i pogrzebali w jego grobie z jego ojcami w mieście Dawida.
29 (Mʼchaka cha khumi ndi chimodzi cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu, Ahaziya anakhala mfumu ya ku Yuda).
W jedenastym roku Jorama, syna Achaba, Achazjasz zaczął królować nad Judą.
30 Kenaka Yehu anapita ku Yezireeli. Yezebeli atamva zimene zinachitika, anapaka zodzikometsera mʼmaso, naluka tsitsi lake, namasuzumira pa zenera.
Potem Jehu przybył do Jizreel. Gdy Jezabel usłyszała o tym, pomalowała swoją twarz, upiększyła włosy i wyglądała przez okno.
31 Pamene Yehu ankalowa pa chipata iye anafunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere, iwe Zimuri, munthu wopha mbuye wako?”
A gdy Jehu wjeżdżał przez bramę, zapytała: Czy miał pokój Zimri, który zabił swego pana?
32 Yehu anakweza maso nayangʼana pa zenera, ndipo anafuwula kuti, “Kodi ndani ali mbali yanga? Ndani?” Anthu ofulidwa awiri kapena atatu anayangʼana Yehu pansipo.
On zaś podniósł twarz ku oknu i zawołał: Kto [jest] ze mną? Kto? Wtedy wyjrzeli ku niemu dwaj [albo] trzej eunuchowie.
33 Yehu anawawuza kuti, “Muponyeni pansi!” Motero anamuponya pansi ndipo magazi ake ena anafalikira pa khoma ndi pa akavalo pamene ankamupondaponda.
Powiedział im: Zrzućcie ją. Wtedy zrzucili ją. Jej krew obryzgała mur i konie, a on podeptał ją.
34 Yehu analowa mʼnyumba yaufumu ndipo anadya ndi kumwa. Kenaka iye anati, “Kamutoleni mkazi wotembereredwayo, ndipo kamuyikeni mʼmanda, popeza ndi mwana wa mfumu.”
A gdy [tam] wszedł, najadł się i napił, potem powiedział: Zajmijcie się teraz tą przeklętą i pogrzebcie ją. Jest bowiem córką króla.
35 Koma atapita kuti akamuyike mʼmanda, sanapeze kanthu kupatula chibade cha mutu wokha, mapazi ake ndi manja ake.
Poszli, aby ją pogrzebać, lecz nie znaleźli z niej nic poza czaszką, stopami i dłońmi.
36 Choncho iwo anabwerera kwa Yehu ndi kukamufotokozera kuti, “Mawu amene Yehova anayankhula kudzera mwa mtumiki wake Eliya wa ku Tisibe ndi awa: Pa munda wa ku Yezireeli agalu adzadya mtembo wa Yezebeli.
Wrócili więc i oznajmili mu to. On zaś powiedział: [Wypełniło się] słowo PANA, które wypowiedział przez swego sługę Eliasza Tiszbitę: Na polu Jizreel psy zjedzą ciało Jezabel.
37 Mtembo wa Yezebeli udzakhala ngati zinyalala pa munda wa ku Yezireeli, kotero kuti palibe amene adzathe kunena kuti, ‘Uyu ndi Yezebeli.’”
A trup Jezabel będzie jak gnój leżący na powierzchni roli, na polu Jizreel, tak że nikt nie powie: To jest Jezabel.

< 2 Mafumu 9 >