< 2 Mafumu 6 >

1 Ana a aneneri anati kwa Elisa, “Taonani malo amene timakhala ndi inu atichepera kwambiri.
Forsothe the sones of prophetis seiden to Elisee, Lo! the place in which we dwellen bifor thee, is streiyt to vs;
2 Tiloleni tipite ku Yorodani kumene aliyense wa ife akadule mtengo umodzi, kuti timange malo woti tizikhalamo.” Ndipo Elisa anati, “Pitani.”
go we `til to Jordan, and ech man take of the wode `a mater for hym silf, that we bild to vs here a place to dwelle.
3 Mmodzi wa iwo anati, “Chonde mulole kutsagana nawo atumiki anu.” Elisa anayankha kuti, “Ndipita nanu.”
Which Elisee seide, Go ye. And oon of hem seide, Therfor `and thou come with thi seruauntis. He answeride, Y schal come. And he yede with hem.
4 Ndipo anapita nawo. Anapita ku Yorodani nayamba kudula mitengo.
And whanne thei `hadden come to Jordan, thei hewiden trees.
5 Pamene wina ankadula mtengo, nkhwangwa yake inaguluka nigwera mʼmadzi. Iye anafuwula kuti, “Mayo! Mbuye wanga! Popeza ndi yobwereka!”
Sotheli it bifelde, that whanne `o man hadde kit doun mater, the yrun of the axe felde in to the watir; and he criede, and seide, Alas! alas! alas! my lord, and Y hadde take this same thing bi borewing.
6 Ndipo munthu wa Mulungu uja anafunsa, “Yagwera pati?” Pamene anamuonetsa malowo, Elisa anadula kamtengo nakaponya pamenepo, ndipo nkhwangwayo inayandama.
Sotheli the man of God seide, Where felde it? And he schewide to hym the place. Therfor he kittide doun a tree, and sente thidur; and the yrun fletide.
7 Elisa anati, “Itenge.” Ndipo munthuyo anatambalitsa dzanja lake nayitenga.
And he seide, Take thou. Which helde forth the hond, and took it.
8 Tsono mfumu ya ku Aramu inali pa nkhondo ndi Israeli. Itakambirana ndi atsogoleri ake ankhondo inati, “Ndidzamanga misasa yanga pamalo akutiakuti.”
Forsothe the kyng of Syrie fauyte ayens Israel; and he took counseil with hise seruauntis, and seide, Sette we buschementis in this place and that.
9 Munthu wa Mulungu anatumiza mawu kwa mfumu ya ku Israeli kuti “Musamale podutsa malo akuti, chifukwa Aaramu akupita kumeneko.”
Therfor the man of God sente to the kyng of Israel, and seide, Be war, lest thou passe to that place, for men of Sirie ben there in buschementis.
10 Choncho mfumu ya ku Israeli inatuma anthu kumalo kumene munthu wa Mulunguyo ananena. Nthawi ndi nthawi Elisa ankachenjeza mfumu, kotero kuti ankakhala tcheru ku malo amenewo.
Therfor the kyng of Israel sente to the place, which the man of God hadde seid to him, and bifor ocupiede it, and kepte hym silf there not onys, nether twies.
11 Zimenezi zinakwiyitsa kwambiri mfumu ya ku Aramu. Mfumuyo inayitanitsa atsogoleri ake ankhondo ndipo inawafunsa kuti, “Kodi simungandiwuze munthu amene pakati pathu pano ali mbali ya mfumu ya ku Israeli?”
And the herte of the kyng of Sirie was disturblid for this thing; and whanne hise seruauntis weren clepide togidere, he seide, Whi schewen ye not to me, who is my tretour anentis the kyng of Israel?
12 Mmodzi mwa atsogoleri a ankhondowo anati, “Palibe ndi mmodzi yemwe pakati pathu, inu mbuye wanga, koma Elisa mneneri amene ali ku Israeli amawuza mfumu ya ku Israeli mawu enieni amene inu mumayankhula ku chipinda kwanu.”
And oon of hise seruauntis seide, Nay, my lord the kyng, but Elisee, the prophete, which is in Israel, schewith to the kyng of Israel alle thingis, what euer thingis thou spekist in thi closet.
13 Choncho mfumu inalamula kuti, “Pitani, kafufuzeni kumene akukhala kuti ine nditume anthu kukamugwira.” Anthuwo anabweretsa mawu oti, “Taonani, Elisa ali ku Dotani.”
And the kyng seide to hem, `Go ye, and se, where he is, that Y sende, and take hym. And thei telden to him, and seiden, Lo! he dwellith in Dothaym.
14 Ndipo mfumu inatumizako magaleta ndi akavalo ndiponso gulu lankhondo lamphamvu. Anapita usiku nakawuzungulira mzindawo.
And the kyng sente thidur horsis, and charis, and the strengthe of the oost; whiche, whanne thei hadden come bi nyyt, cumpassiden the citee.
15 Mtumiki wa munthu wa Mulungu atadzuka mmamawa ndi kutuluka panja, gulu la ankhondo pamodzi ndi akavalo ndi magaleta anali atazungulira mzindawo. Mtumikiyo anafunsa kuti, “Kalanga mbuye wanga, tidzachita chiyani?”
Sotheli the mynystre of the man of God roos eerli, and yede out, and he siy an oost in the cumpas of the citee, and horsis, and charis. And he telde to the man of God, and seide, Alas! alas! alas! my lord, what schulen we do?
16 Mneneri anamuyankha kuti, “Usachite mantha. Amene ali mbali yathu ndi ambiri kupambana amene ali mbali yawo.”
And he answeride, Nile thou drede; for mo ben with vs than with hem.
17 Ndipo Elisa anapemphera kuti, “Inu Yehova tsekulani maso ake kuti aone.” Pamenepo Yehova anatsekula maso a mtumikiyo, ndipo anayangʼana naona kuti phiri lonse linali lodzaza ndi akavalo ndi magaleta a moto atazungulira Elisa.
And whanne Elisee hadde preied, he seide, Lord, opene thou the iyen of this child, that he se. And the Lord openyde the iyen of the child, and he siy. And, lo! the hil ful of horsis, and of charis of fier, in the cumpas of Elisee.
18 Pamene adaniwo ankabwera kudzalimbana naye, Elisa anapemphera kwa Yehova kuti, “Achititseni khungu anthu awa.” Kotero Yehova anawachititsa khungu monga anapemphera Elisa.
Sotheli the enemyes camen doun to hym; forsothe Elisee preiede to the Lord, and seide, Y biseche, smyte thou this folc with blyndenesse. And the Lord smoot hem, that thei sien not, bi the word of Elisee.
19 Elisa anawawuza ankhondowo kuti, “Njira si imeneyi ndipo mzinda sumenewunso. Tsateni, ndipo ndidzakutengerani kwa munthu amene mukumufunayo.” Ndipo anawatengera ku Samariya.
Forsothe Elisee seide to hem, This is not the weie, nether this is the citee; sue ye me, and Y schal schewe to you the man, whom ye seken. And he ledde hem into Samarie.
20 Atalowa mu mzinda wa Samariya, Elisa anati, “Yehova tsekulani maso a anthu awa kuti aone.” Choncho Yehova anatsekula maso awo ndipo anangoona kuti ali mʼkati mwenimweni mwa Samariya.
And whanne thei hadden entrid into Samarie, Elisee seide, Lord, opene thou the iyen of these men, that thei see. And the Lord openyde her iyen, and thei siyen, that thei weren in the myddis of Samarie.
21 Mfumu ya ku Israeli itawaona, inafunsa Elisa kuti, “Abambo anga, kodi ndiwaphe? Kodi ndiwaphe?”
And the kyng of Israel, whanne he hadde seyn hem, seide to Elisee, My fadir, whether Y schal smyte hem?
22 Elisa anayankha kuti, “Musawaphe. Kodi mungaphe anthu amene munawagwira pogwiritsa ntchito lupanga ndi uta? Apatseni chakudya ndi madzi kuti adye ndi kumwa kenaka apite kwa mbuye wawo.”
And he seide, Thou schalt not smyte hem, for thou hast not take hem bi thi swerd and bouwe, that thou smyte hem; but sette thou breed and watir bifor hem, that thei ete and drynke, and go to her lord.
23 Choncho anawakonzera mphwando lalikulu, ndipo atatsiriza kudya ndi kumwa, anawatumiza kwawo ndipo anabwerera kwa mbuye wawo. Kotero magulu a ankhondo a ku Aramu analeka kuthira nkhondo dziko la Israeli.
And `greet makyng redi of metis was set forth to hem; and thei eten, and drunken. And the kyng lefte hem, and thei yeden to her lord; and theues of Sirie camen no more in to the lond of Israel.
24 Patapita nthawi, Beni-Hadadi mfumu ya Aramu anasonkhanitsa gulu lake lonse la ankhondo, napita kukazungulira mzinda wa Samariya.
Forsothe it was don after these thingis, Benadab, king of Sirie, gaderide alle his oost, and stiede, and bisegide Samarie.
25 Mu mzinda wa Samariya munali njala yoopsa. Ndipo taonani, Aaramu anazungulira mzindawu kwa nthawi yayitali kotero kuti mutu wa bulu ankawugulitsa ndalama za siliva 80, ndipo magalamu 200 a zitosi za nkhunda ankawagulitsa pa mtengo wa masekeli asanu.
And greet hungur was maad in Samarie; and so long it was bisegid, til the heed of an asse were seeld for fourescore platis of siluer, and the fourthe part of a mesure clepid cabus of the crawe of culueris was seeld for fyue platis of siluer.
26 Pamene mfumu inkayenda pa khoma la mzindawo, mayi wina anafuwulira mfumuyo kuti, “Thandizeni mbuye wanga mfumu!”
And whanne the kyng of Israel passide bi the wal, sum womman criede to hym, and seide, My lord the kyng, saue thou me.
27 Mfumu inayankha kuti, “Ngati Yehova sakuthandiza iwe, ine thandizo lako ndingalipeze kuti? Kuchokera ku malo opunthira tirigu kodi? Kuchokera kumalo opsinyira mphesa kodi?”
Which seide, Nai, the Lord saue thee; wherof may Y saue thee? of cornfloor, ethir of pressour? And the kyng seide to hir, What wolt thou to thee?
28 Pamenepo mfumuyo inafunsa mayiyo kuti, “Kodi chakuvuta nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Mayi uyu anandiwuza kuti, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye lero, ndipo mawa tidzadya mwana wangayu.’
And sche answeride, This womman seide to me, Yyue thi sone, that we ete hym to dai, and we schulen ete my sone to morewe.
29 Choncho tinaphika mwana wanga ndi kumudya. Tsiku lotsatira lakelo ine ndinati, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye,’ koma iye anabisa mwana wakeyo.”
Therfor we setheden my sone, and eten him. And Y seide to hir in the tother day, Yyue thi sone, that we ete hym; and she hidde hir sone.
30 Mfumu itamva mawu a mayiyo, inangʼamba mkanjo wake. Pamene inkayenda pa khoma, anthu anayangʼana, ndipo anaona zovala zamʼkati, pakuti anavala chiguduli.
And whanne the kyng hadde herd this, he to-rente hise clothis, and passide bi the wal; and al the puple siy the heire, `with which the kyng was clothid at the fleisch with ynne.
31 Mfumuyo inati, “Mulungu andilange, andilange kwambiri ndikapanda kudula mutu wa Elisa mwana wa Safati lero!”
And the kyng seide, God do to me these thingis, and adde these thingis, if the heed of Elise, sone of Saphat, schal stonde on hym to dai.
32 Tsono Elisa nʼkuti atakhala mʼnyumba mwake, ndipo akuluakulu anali naye limodzi. Mfumu inatuma munthu wina kuti imutsogolere, koma asanafike, Elisa anawuza akuluakuluwo kuti, “Kodi simukuona momwe wopha munthu uja watumizira munthu wina kuti adzadule mutu wanga? Taonani mthengayo akafika, mutseke chitseko ndipo muchigwiritsitse kuti asalowe. Kodi ndikumvawo pambuyo pake si mgugu wa mbuye wake?”
Sotheli Elisee sat in his hows, and elde men saten with hym; `therfor he biforsente a man, and bifor that thilke messanger cam, Elisee seide to the elde men, Whether ye witen, that the sone of manquellere sente hidur, that myn heed be gird of? Therfor se ye, whanne the messanger cometh, close ye the dore, and `suffre ye not hym to entre; for, lo! the sown of the feet of his lord is bihynde hym.
33 Elisa akuyankhulabe ndi anthuwo, taonani, wamthengayo anafika kwa iye. Ndipo mfumu inati, “Mavuto amenewa ndi ochokera kwa Yehova. Kodi nʼchifukwa chiyani ine ndiyenera kudikira thandizo lochokera kwa Yehova?”
And yit `while he spak to hem, the messanger that cam to hym apperide; and the kyng seide, Lo! so greet yuel is of the Lord; sotheli what more schal Y abide of the Lord?

< 2 Mafumu 6 >