< 2 Mafumu 3 >

1 Yoramu mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya mʼchaka cha 18 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda ndipo analamulira zaka khumi ndi ziwiri.
A Joram sin Ahavov zacari se nad Izrailjem u Samariji osamnaeste godine carovanja Josafatova nad Judom, i carova dvanaest godina.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova koma sizinafanane ndi zimene anachita abambo ndi amayi ake. Iye anachotsa fano la mwala la Baala limene abambo ake anapanga.
I èinjaše što je zlo pred Gospodom, ali ne kao otac njegov i kao mati njegova, jer obori lik Valov koji bješe naèinio otac njegov.
3 Komabe anawumirira kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo sanafune kuwaleka.
Ali osta u grijesima Jerovoama sina Navatova, kojima navede na grijeh Izrailja, i ne otstupi od njih.
4 Tsono Mesa, mfumu ya ku Mowabu ankaweta nkhosa, ndipo iye ankayenera kumapereka kwa mfumu ya ku Israeli chaka ndi chaka ana ankhosa onenepa okwanira 100,000 pamodzi ndi ubweya wankhosa 100,000 zazimuna.
A Misa car Moavski imaše mnogo stoke, i davaše caru Izrailjevu sto tisuæa jaganjaca i sto tisuæa ovnova pod runom.
5 Koma atamwalira Ahabu, mfumu ya ku Mowabu inawukira mfumu ya ku Israeli.
Ali kad umrije Ahav, odmetnu se car Moavski od cara Izrailjeva.
6 Choncho nthawi imeneyi mfumu Yoramu inatuluka mu Samariya ndi kukasonkhanitsa Aisraeli onse.
A car Joram izide u to vrijeme iz Samarije i prebroji svega Izrailja.
7 Yoramu anatumizanso uthenga uwu kwa Yehosafati mfumu ya ku Yuda: “Mfumu ya ku Mowabu yandiwukira. Kodi ungapite nane kukamenyana ndi Mowabu?” Iye anayankha kuti, “Ine ndidzapita nawe. Iwe ndi ine ndife anthu amodzi, anthu anga ali ngati anthu ako, akavalo anga ali ngati akavalo ako.”
I otide, te posla k Josafatu caru Judinu i poruèi mu: car Moavski odmetnu se od mene; hoæeš li iæi sa mnom na vojsku na Moavce? A on reèe: hoæu, ja kao ti, moj narod kao tvoj narod, moji konji kao tvoji konji.
8 Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi tidzera njira iti popita ku nkhondoko?” Yoramu anayankha kuti, “Tidzera ku Chipululu cha Edomu.”
Iza toga reèe: a kojim æemo putem iæi? A on reèe: preko pustinje Edomske.
9 Choncho mfumu ya ku Israeli inanyamuka pamodzi ndi mfumu ya ku Yuda ndi ya ku Edomu. Ndipo atayenda mozungulira mʼchipululu kwa masiku asanu ndi awiri, asilikali analibe madzi woti amwe kapena kumwetsa nyama zawo zosenza katundu.
I tako izide car Izrailjev i car Judin i car Edomski, i idoše putem sedam dana, i ne bijaše vode vojsci ni stoci, koja iðaše za njima.
10 Mfumu inafuwula kuti, “Nʼchiyani chomwe chikutichitikira! Kodi Yehova wasonkhanitsa mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu?”
I reèe car Izrailjev: jaoh! dozva Gospod ova tri cara da ih preda u ruke Moavcima.
11 Koma mfumu Yehosafati inafunsa kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wa Yehova woti tingakafunse kwa Yehova kudzera mwa iyeyo?” Mtsogoleri wa ankhondo wa mfumu ya ku Israeli anayankha kuti, “Alipo, Elisa mwana wa Safati. Iye anali mtumiki wa Eliya.”
A Josafat reèe: ima li tu koji prorok Gospodnji da upitamo Gospoda preko njega? A jedan izmeðu sluga cara Izrailjeva odgovori i reèe: ovdje je Jelisije sin Safatov, koji je Iliji poljevao vodom ruke.
12 Yehosafati anati, “Yehova amayankhula kudzera mwa iye.” Choncho mfumu ya ku Israeli pamodzi ndi Yehosafati ndiponso mfumu ya ku Edomu anapita kwa Elisa.
Tada reèe Josafat: u njega je rijeè Gospodnja. I otidoše k njemu car Izrailjev i Josafat i car Edomski.
13 Elisa ananena kwa mfumu ya ku Israeli kuti, “Pali ubale wanji pakati pa inu ndi ine? Pitani kwa aneneri a abambo ndi amayi anu.” Mfumu ya ku Israeli inayankha kuti, “Ayi, pakuti ndi Yehova amene anatisonkhanitsa ife mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu.”
A Jelisije reèe caru Izrailjevu: šta je meni do tebe? idi ka prorocima oca svojega i ka prorocima matere svoje. A car Izrailjev reèe mu: ne, jer Gospod dozva ova tri cara da ih preda u ruke Moavcima.
14 Elisa anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse amene ndimamutumikira, pakanapanda kuti ndimamuchitira ulemu Yehosafati mfumu ya ku Yuda, sindikanakulabadirani kapena kukuyangʼanani nʼkomwe.
A Jelisije reèe: tako da je živ Gospod nad vojskama, pred kojim stojim, da ne gledam na Josafata cara Judina, ne bih mario za te niti bih te pogledao.
15 Koma tsopano ndiyitanireni munthu wodziwa kuyimba bwino zeze.” Munthuyo akuyimba zeze, mphamvu ya Yehova inafika pa Elisa,
Nego sada dovedite mi gudaèa. I kad gudaè guðaše, doðe ruka Gospodnja nada nj;
16 ndipo anati, “Yehova akuti, ‘Kumbani ngalande mʼchigwa chonse.’
I reèe: ovako veli Gospod: naèinite po ovoj dolini mnogo jama.
17 Pakuti Yehova akunena kuti, ‘Simudzaona mphepo kapena mvula, komabe chigwa ichi chopanda madzi chidzadzaza ndi madzi, ndipo inu mudzamwa pamodzi ndi ngʼombe zanu ndiponso nyama zanu zonse.’
Jer ovako veli Gospod: neæete osjetiti vjetra niti æete vidjeti dažda, ali æe se dolina ova napuniti vode, te æete piti i vi i ljudi vaši i stoka vaša.
18 Izi ndi zosavuta pamaso pa Yehova. Ndipo adzaperekanso Amowabu mʼmanja mwanu.
Pa i to je malo Gospodu, nego i Moavce æe vam predati u ruke.
19 Mudzagonjetsa mizinda yawo yonse yotetezedwa ndiponso mizinda yawo ikuluikulu. Mudzagwetsa mtengo wabwino uliwonse, mudzatseka akasupe onse amadzi, ndiponso mudzawononga minda yawo yonse yachonde poponyamo miyala.”
I raskopaæete sve tvrde gradove, i sve izabrane gradove, i posjeæi æete sva dobra drveta i zaroniti sve izvore vodene, i svaku njivu dobru potræete kamenjem.
20 Mmawa mwake, nthawi yopereka nsembe ili pafupi, anangoona madzi akutuluka kuchokera ku Edomu, ndipo malo onse anadzaza ndi madzi.
A ujutru kad se prinosi dar, gle, doðe voda od Edomske, i napuni se zemlja vode.
21 Tsono nʼkuti Amowabu onse atamva kuti mafumu abwera kudzachita nawo nkhondo. Kotero, anayitana munthu aliyense, wamkulu ndi wamngʼono amene ankatha kugwira chida chankhondo ndipo anakayima ku malire a dziko lawo.
A svi Moavci èuvši da su izišli carevi da udare na njih, sazvaše sve koji se poèinjahu pasati i starije i stadoše na meði.
22 Amowabu atadzuka mmamawa, dzuwa likuwala pa madziwo, anaona madziwo akuoneka wofiira ngati magazi patsogolo pawo.
A ujutru kad ustaše i sunce ogranu nad onom vodom, ugledaše Moavci prema sebi vodu gdje se crveni kao krv.
23 Ndipo iwo anati, “Taonani magazi! Mafumu aja amenyana okhaokha ndipo aphana. Amowabu, tsopano ndi nthawi yofunkha!”
I rekoše: krv je; pobili su se carevi, i jedan drugoga pogubili; sada dakle na plijen, Moavci!
24 Koma Amowabu atafika ku misasa ya Israeli, Aisraeli ananyamuka ndi kumenyana nawo mpaka anathawa. Ndipo Aisraeli analowa mʼdzikolo ndi kupha Amowabu.
A kad doðoše do okola Izrailjeva, podigoše se Izrailjci i razbiše Moavce, te pobjegoše ispred njih, a oni uðoše u zemlju Moavsku bijuæi ih.
25 Aisraeli anagumula mizinda yawo ndipo munthu aliyense anaponya mwala pa munda uliwonse wachonde mpaka utadzaza ndi miyala. Iwo anatseka akasupe onse amadzi ndiponso anadula mtengo wabwino uliwonse. Mzinda wa Kiri Hareseti wokha ndiye unatsala wotetezedwa koma anthu oponya miyala anawuzungulira nawuthiranso nkhondo.
I gradove njihove raskopaše, i na svaku dobru njivu bacajuæi svaki po kamen zasuše je, i sve izvore vodene zaroniše, i sva dobra drveta posjekoše tako da samo ostaviše kamenje u Kirarasetu. I opkolivši ga praæari stadoše ga biti.
26 Mfumu ya ku Mowabu itaona kuti nkhondo ikumulaka, inatenga anthu 700 a malupanga kuti athawe modutsa mfumu ya ku Edomu, koma inalephera.
A car Moavski kad vidje da æe ga nadvladati vojska, uze sa sobom sedam stotina ljudi, koji mahahu maèem, da prodru kroz vojsku cara Edomskoga, ali ne mogoše.
27 Choncho inatenga mwana wake wamwamuna woyamba kubadwa, amene akanalowa ufumu mʼmalo mwake, ndi kumupereka nsembe pa khoma la mzinda. Zimenezi zinachititsa kuti mkwiyo ndi ukali wa Amowabu ukule kwambiri pa Aisraeli ndipo Aisraeliwo anathawa nabwerera ku dziko la kwawo.
Tada uze sina svojega prvenca koji šæaše biti car na njegovo mjesto, i prinese ga na žrtvu paljenicu na zidu. Tada se podiže veliki gnjev na Izrailja, te otidoše odande i vratiše se u svoju zemlju.

< 2 Mafumu 3 >