< 2 Mafumu 23 >

1 Pamenepo mfumu inayitanitsa akuluakulu onse a ku Yuda ndi Yerusalemu.
Wtedy król posłał, aby zebrali się wokół niego wszyscy starsi Judy i Jerozolimy.
2 Mfumuyo inapita ku Nyumba ya Yehova pamodzi ndi anthu onse a ku Yuda, ndi onse okhala mu Yerusalemu, ansembe ndi aneneri, ndiponso anthu ena onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu. Mfumuyo inawerenga mawu onse a mʼBuku la Chipangano limene linapezeka mʼNyumba ya Yehova, anthu onse akumva.
Następnie król udał się do domu PANA, a wraz z nim wszyscy mężczyźni Judy, wszyscy mieszkańcy Jerozolimy, kapłani, prorocy oraz cały lud – od najmniejszych do największych. I czytał do ich uszu wszystkie słowa księgi przymierza, którą znaleziono w domu PANA.
3 Mfumu inayimirira pambali pa chipilala ndi kuchita pangano pamaso pa Yehova kuti idzatsatira Yehova ndi kusunga malamulo, mawu ndi malangizo ake ndi mtima wonse ndi moyo wonse, kukwaniritsa mawu a mʼpanganoli, olembedwa mʼbukuli. Pamenepo anthu onse anadzipereka kutsatira panganoli.
Potem król stanął przy kolumnie i zawarł przymierze przed PANEM, że będą szli za PANEM i będą przestrzegać jego przykazań, świadectw i nakazów z całego serca i całą duszą i wypełniać słowa przymierza, które zostały napisane w tej księdze. I cały lud przystąpił do przymierza.
4 Mfumu inalamula wansembe wamkulu Hilikiya, ansembe othandizana naye ndi alonda a pa khomo kuti achotse mʼNyumba ya Yehova ziwiya zonse zopembedzera Baala ndi Asera ndiponso mafano a zinthu zamlengalenga. Yosiya anazitentha kunja kwa Yerusalemu, ku minda ya ku Chigwa cha Kidroni ndipo phulusa lake anapita nalo ku Beteli.
Wtedy król nakazał najwyższemu kapłanowi Chilkiaszowi, kapłanom drugiego rzędu i stróżom progu wynieść ze świątyni PANA wszystkie przedmioty wykonane dla Baala, do gaju i dla całego zastępu niebieskiego. I spalił je poza Jerozolimą na polu Cedronu, i zaniósł ich popiół do Betel.
5 Iye anachotsa ansembe a mafano amene anayikidwa ndi mafumu a Yuda kuti azifukiza lubani ku malo opembedzera mafano a ku mizinda ya ku Yuda ndi kumalo ozungulira Yerusalemu, amene ankafukiza lubani kwa Baala, dzuwa, mwezi, nyenyezi ndi zinthu zonse zamlengalenga.
Zwolnił też [z urzędu] bałwochwalczych kapłanów, których ustanowili królowie Judy, aby palili kadzidło na wyżynach w miastach Judy i w okolicach Jerozolimy, oraz tych, którzy palili kadzidło Baalowi, słońcu, księżycowi, planetom i całemu zastępowi niebieskiemu.
6 Anachotsa fano la Asera mʼNyumba ya Yehova napita nalo kunja kwa Yerusalemu, ku Chigwa cha Kidroni, nalitentha kumeneko. Anapera fanolo ndi kukataya phulusa lake pa manda a anthu wamba.
Wyniósł gaj z domu PANA poza Jerozolimę, do potoku Cedron, i spalił go przy potoku Cedron, starł go na proch i rozrzucił na grobach synów ludu.
7 Iye anagwetsanso tinyumba ta ochita zachiwerewere, timene tinali mʼNyumba ya Yehova, kumene akazi ankalukirako mikanjo yovala popembedza Asera.
Zburzył też domy Sodomitów, które znajdowały się przy domu PANA, gdzie kobiety tkały zasłony do gaju.
8 Yosiya anabweretsanso ansembe onse kuchokera mʼmizinda ya Yuda, nawononga malo opembedzera mafano, kuyambira ku Geba mpaka ku Beeriseba, kumene ansembe ankafukizako lubani. Anagwetsa nyumba za milungu zimene zinali pa chipata cha Yoswa, bwanamkubwa wa mzindawo, kumanzere kwa chipata cha mzinda.
I zwołał wszystkich kapłanów z miast Judy, i splugawił wyżyny, na których kapłani palili kadzidło, od Geba aż do Beer-Szeby, i zburzył wyżyny przy bramach [znajdujących się] u wejścia bramy Jozuego, namiestnika miasta, po lewej stronie, gdy się wchodzi przez bramę miejską.
9 Ngakhale kuti ansembe a ku malo opembedzera mafanowo sanawalole kuti atumikire pa guwa lansembe la Yehova mu Yerusalemu, koma ankadya buledi wopanda yisiti pamodzi ndi ansembe anzawo.
Jednakże kapłani wyżyn nie przystąpili do ołtarza PANA w Jerozolimie, ale mogli jeść przaśne chleby wśród swoich braci.
10 Mfumu Yosiya anawononganso Tofeti, amene anali ku Chigwa cha Hinomu, kuti wina aliyense asagwiritse ntchito malowo popereka mwana wake wamwamuna kapena wamkazi pa moto kwa Moleki.
Splugawił również Tofet, które było w dolinie syna Hinnom, aby nikt więcej nie przeprowadził swego syna ani córki przez ogień [ku czci] Molocha.
11 Anachotsa pa chipata cholowera ku Nyumba ya Yehova akavalo amene mafumu a Yuda anawapereka ngati nsembe kwa dzuwa. Akavalo anali pafupi ndi bwalo la chipinda cha mkulu wina wotchedwa Natani-Meleki. Ndipo Yosiya anatentha magaleta opembedzera dzuwa.
Usunął też konie, które królowie Judy poświęcili słońcu u wejścia do domu PANA, obok komnaty dworzanina Natanmeleka, która była na przedmieściu, a rydwany słońca spalił ogniem.
12 Anagwetsa maguwa amene mafumu a Yuda anawamanga pa denga pafupi ndi chipinda chapamwamba cha Ahazi, ndiponso maguwa amene Manase anamanga mʼmabwalo awiri a Nyumba ya Yehova. Yosiya anawachotsa kumeneko nawaphwanya ndi kutaya zidutswa zake mʼChigwa cha Kidroni.
Król zburzył także ołtarze, które znajdowały się na dachu górnej komnaty Achaza, zbudowane przez królów Judy, oraz ołtarze, które uczynił Manasses w obu dziedzińcach domu PANA. Usunął je stamtąd i wrzucił ich proch do potoku Cedron.
13 Mfumuyo inawononga malo opembedzera mafano amene ali kummawa kwa Yerusalemu cha kumpoto kwa Phiri la Chiwonongeko. Maguwawa Solomoni mfumu ya Israeli inamangira Asitoreti, fano lalikazi lonyansa la Asidoni, Kemosi, fano lonyansa la Amowabu, ndi Moleki, fano lonyansa la anthu a ku Amoni.
Król splugawił wyżyny, które stały przed Jerozolimą po prawej stronie Góry Zatracenia i które zbudował Salomon, król Izraela, dla Asztarty, obrzydliwości Sydończyków, dla Kemosza, obrzydliwości Moabitów, i dla Milkoma, obrzydliwości synów Ammona.
14 Yosiya anaphwanya miyala ya chipembedzo ndiponso anadula mitengo ya fano la Asera ndipo anakwirira malowo ndi mafupa a anthu.
I pokruszył posągi, powycinał gaje, a ich miejsca napełnił kośćmi ludzkimi.
15 Ngakhalenso guwa lansembe la ku Beteli, malo opembedzera mafano amene anapanga Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli, Yosiya anawononga guwalo ndi malo opembedzera mafanowo. Iye anatentha malo opembedzera mafanowo ndi kuwapera ndipo anatenthanso fano la Asera.
Ponadto ołtarz, który był w Betel, [i] wyżynę uczynioną przez Jeroboama, syna Nebata, który przywiódł Izraela do grzechu – także ten ołtarz i wyżynę zburzył. Spalił wyżynę, starł na proch i spalił gaj.
16 Kenaka Yosiya anayangʼanayangʼana ndipo ataona manda amene anali pomwepo, mʼmbali mwa phiri, analamula kuti afukule mandawo ndi kutulutsa mafupa kuti awatenthe paguwapo kuti alidetse, potsatira mawu a Yehova amene munthu wa Mulungu analoseratu za zimenezi.
A gdy Jozjasz odwrócił się, zobaczył groby, które były tam na górze. Posłał i zabrał kości z tych grobów, i spalił je na ołtarzu, plugawiąc go zgodnie ze słowem PANA wygłoszonym przez męża Bożego, który wypowiedział te rzeczy.
17 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi chizindikiro cha manda chimene ndikuwaonawo ndi chayani?” Anthu a mu mzindamo anayankha kuti, “Ndi chizindikiro cha manda a munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda amene ananeneratu zimene inu mwalichita guwa lansembe la Beteli.”
I zapytał: Co to za napis, który widzę? Ludzie z tego miasta odpowiedzieli: To grób męża Bożego, który przyszedł z Judy i zapowiedział rzeczy, które wykonałeś nad ołtarzem w Betel.
18 Mfumuyo inati, “Alekeni manda amenewo, munthu asachotse mafupa ake.” Choncho anawasiya mafupa akewo pamodzi ndi mafupa a mneneri wa ku Samariya uja.
Wtedy powiedział: Zostawcie go, niech nikt nie rusza jego kości. Pozostawiono więc jego kości wraz z kośćmi proroka, który przybył z Samarii.
19 Monga momwe Yosiya anachitira ku Beteli, anachotsa ndi kuwononga nyumba za milungu zonse ndi malo opembedzera mafano amene mafumu anamanga mʼmizinda ya ku Samariya omwe anakwiyitsa Yehova.
Jozjasz usunął też wszystkie świątynie na wyżynach, które były w miastach Samarii zbudowanych przez królów Izraela, aby drażnić [PANA]. Postąpił z nimi tak samo, jak uczynił w Betel.
20 Yosiya anapha ansembe onse amene ankatumikira ku malo opembedzera mafano, anawaphera pa maguwa awo ndi kutentha mafupa awo. Kenaka iye anapita ku Yerusalemu.
Pozabijał także wszystkich kapłanów wyżyn, którzy tam [byli] przy ołtarzach, i spalił na nich ludzkie kości. Potem wrócił do Jerozolimy.
21 Mfumu inalamula anthu onse kuti, “Chitani Chikondwerero cha Paska kulemekeza Yehova Mulungu wanu, motsatira zomwe zalembedwa mʼBuku la Chipangano.”
I król nakazał całemu ludowi: Obchodźcie święto Paschy dla PANA, waszego Boga, tak jak jest napisane w księdze tego przymierza.
22 Paska yotere inali isanachitikepo kuyambira nthawi ya oweruza amene anatsogolera Israeli, kapenanso nthawi yonse ya mafumu a Yuda sipanachitikenso Paska ngati imeneyo.
Takiej Paschy nie obchodzono od czasów sędziów, którzy sądzili Izraela, i przez wszystkie dni królów Izraela i królów Judy.
23 Koma mʼchaka cha 18 cha Mfumu Yosiya, Paska imeneyi anachitira Yehova mu Yerusalemu.
Dopiero w osiemnastym roku króla Jozjasza obchodzono taką Paschę dla PANA w Jerozolimie.
24 Kuwonjezera apa, Yosiya anachotsa anthu a mawula, woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, milungu ya mʼnyumba, mafano ndiponso zinthu zonse zonyansa zopezeka mu Yuda ndi Yerusalemu. Iye anachita izi pokwaniritsa lamulo lolembedwa mʼbuku limene Hilikiya analipeza mʼNyumba ya Yehova.
Jozjasz usunął również czarowników, wróżbiarzy, posągi, bożki i wszystkie obrzydliwości, które widziano w ziemi Judy i w Jerozolimie, aby wypełnić słowa prawa napisane w księdze, którą znalazł kapłan Chilkiasz w domu PANA.
25 Yosiyayo asanalowe ufumu, ngakhale atamwalira, panalibenso mfumu ina yofanana naye imene inatembenukira kwa Yehova monga anachitira, ndi mtima wake wonse, ndi moyo wake wonse, ndi mphamvu zake zonse, motsatira Malamulo onse a Mose.
I nie było przed nim króla podobnego do niego, który by wrócił do PANA z całego swego serca, całą swoją duszą i z całej swojej siły, według całego Prawa Mojżesza, i po nim nie powstał nikt jemu podobny.
26 Komabe Yehova sanachotse mkwiyo wake woopsa, umene anali nawo pa Yuda chifukwa cha zonse zimene anachita Manase poputa mkwiyo wa Mulungu.
PAN jednak nie odwrócił się od zapalczywości swego wielkiego gniewu, którym zapłonął przeciwko Judzie z powodu wszelkich zniewag, którymi rozdrażnił go Manasses.
27 Choncho Yehova anati, “Ndidzawachotsanso anthu a ku Yuda pamaso panga monga ndinachotsera anthu a ku Israeli ndipo ndidzawukana mzinda wa Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha, pamodzi ndi Nyumba ino imene ndinati, ‘Dzina langa lidzakhala mʼmenemo.’”
PAN więc powiedział: Również Judę odrzucę sprzed swojego oblicza, jak odrzuciłem Izraela, i wzgardzę tym miastem, które wybrałem, Jerozolimą, i domem tym, o którym powiedziałem: Tam będzie moje imię.
28 Ntchito zina za Yosiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
A pozostałe dzieje Jozjasza i wszystko, co czynił, czy nie są zapisane w księdze kronik królów Judy?
29 Yosiya akanali mfumu, Farao wotchedwa Neko, mfumu ya Igupto, anapita ku Mtsinje wa Yufurate kukathandiza mfumu ya ku Asiriya. Mfumu Yosiya anapita kukachita naye nkhondo, koma Neko anakumana naye ndi kumupha ku Megido.
Za jego dni faraon Necho, król Egiptu, wyruszył przeciwko królowi Asyrii nad rzekę Eufrat. Król Jozjasz wyruszył przeciwko niemu, a gdy ten go zobaczył, zabił go w Megiddo.
30 Atumiki a Yosiyayo ananyamula mtembo wake mu galeta kuchokera ku Megido mpaka ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda akeake. Ndipo anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namudzoza, ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
I jego słudzy przewieźli go zmarłego z Megiddo, sprowadzili go do Jerozolimy i pogrzebali w jego grobie. Potem lud tej ziemi wziął Jehoachaza, syna Jozjasza, namaścił go i ustanowił go królem w miejsce jego ojca.
31 Yehowahazi anakhala mfumu ali ndi 23 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Hamutali, mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Jehoachaz miał dwadzieścia trzy lata, kiedy zaczął królować, i królował trzy miesiące w Jerozolimie. Jego matka miała na imię Chamutal [i była] córką Jeremiasza z Libny.
32 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
Czynił on to, co złe w oczach PANA, zupełnie tak, jak czynili jego ojcowie.
33 Farao Neko anamuyika mʼndende ku Ribula mʼdziko la Hamati kuti asalamulirenso mu Yerusalemu. Farao analamula Yuda kuti azikhoma msonkho wa siliva wolemera makilogalamu 3,400, ndiponso golide wolemera makilogalamu 34.
Faraon Necho uwięził go w Ribla w ziemi Chamat, aby nie królował w Jerozolimie, i nałożył na ziemię daninę w wysokości stu talentów srebra i jednego talentu złota.
34 Farao Neko anayika Eliyakimu mwana wa Yosiya kuti akhale mfumu mʼmalo mwa abambo ake Yosiya, ndipo anasintha dzina lake kukhala Yehoyakimu. Koma iye anatenga Yehowahazi kupita naye ku Igupto ndipo anakafera kumeneko.
Faraon Necho ustanowił królem Eliakima, syna Jozjasza, w miejsce jego ojca Jozjasza, i zmienił jego imię na Joakim, a Jehoachaza zabrał. Ten przyszedł do Egiptu i tam umarł.
35 Yehoyakimu anapereka kwa Farao Neko siliva ndi golide amene anamufuna uja. Koma kuti iye apereke zimenezi, amankhometsa msonkho mʼdziko mwakemo ndipo amalandira siliva ndi golide kuchokera kwa anthu a mʼdzikomo molingana ndi chuma cha munthu aliyense.
A Joakim dał faraonowi srebro i złoto, ale opodatkował ziemię, aby mógł oddać pieniądze według rozkazu faraona. Pobierał srebro i złoto od ludu ziemi, od każdego według oszacowania, aby je oddać faraonowi Necho.
36 Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Zebuda, mwana wa Pedaya wa ku Ruma.
Joakim miał dwadzieścia pięć lat, kiedy zaczął królować, i królował jedenaście lat w Jerozolimie. Jego matka miała na imię Zebidda [i była] córką Pedajasza z Rumy.
37 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
Czynił on to, co złe w oczach PANA, zupełnie tak, jak czynili jego ojcowie.

< 2 Mafumu 23 >