< 2 Mafumu 20 >

1 Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”
In tho daies Ezechie was sijk `til to the deeth; and Isaie, the prophete, sone of Amos, cam to hym, and seide to hym, The Lord God seith these thingis, Comaunde to thin hows, for thou schalt die, and thou schalt not lyue.
2 Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti,
Which Ezechie turnyde his face to the wal, and worschipide the Lord,
3 “Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.
and seide, Y biseche, Lord, haue mynde, hou Y yede bifor thee in treuthe, and in a parfit herte, and Y dide that, that was plesaunt bifor thee. Therfor Ezechie wepte bi greet wepyng.
4 Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti,
And bifor that Ysaie yede out half the part of the court, the word of the Lord was maad to Isaie, and seide,
5 “Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova.
Turne thou ayen, and seie to Ezechie, duyk of my puple, The Lord God of Dauid, thi fadir, seith thes thingis, Y herde thi preiere, and Y siy thi teer, and, lo! Y heelide thee. In the thridde dai thou schalt stie in to the temple of the Lord,
6 Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
and Y schal adde fiftene yeer to thi daies; but also Y schal delyuere thee and this citee fro the hond of the kyng of Assiriens, and Y schal defende this citee for me, and for Dauid, my seruaunt.
7 Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.
And Ysaie seide, Brynge ye to me a gobet of figis. And whanne thei hadden brouyte it, and hadde putte on `his botche, he was heelid.
8 Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”
Forsothe Ezechie seide to Isaie, What schal be the signe, that the Lord schal heele me, and that in the thridde dai Y schal stie in to the temple of the Lord?
9 Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”
To whom Ysaie seide, This schal be `a signe of the Lord, that the Lord schal do the word which he spak; wolt thou, that the schadewe stie by ten lynes, ethir turne ayen bi so many degrees?
10 Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”
And Ezechie seide, It is esy that the schadewe encreesse bi ten lynes, nethir Y wole that this be doon, but that it turne ayen bacward bi ten degrees.
11 Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.
Therfor Ysaie, the prophete, clepide inwardli the Lord, and brouyte ayen bacward bi ten degrees the schadewe bi lynes, bi whiche it hadde go doun thanne in the orologie of Achaz.
12 Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo.
In that tyme Beradacbaladan, sone of Baladam, the kyng of Babiloyne, sente lettris and yiftis to Ezechie; for he hadde herd that Ezechie was sijk, and hadde couerid.
13 Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.
Forsothe Ezechie was glad in the comyng of hem, and he schewide to hem the hows of spyceries, and gold, and siluer, and dyuerse pymentis, also oynementis, and the hows of hise vessels, and alle thingis whiche he myyte haue in hise tresouris; `no word was, `which Ezechie schewide not to hem in his hows, and in al his power.
14 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
Sotheli Ysaie, the prophete, cam to the kyng Ezechie, and seide to hym, What seiden these men, ether fro whennus camen thei to the? To whom Ezechie seide, Thei camen to me fro a fer lond, fro Babiloyne.
15 Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?” Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”
And he answeride, What `sien thei in thin hows? Ezechie seide, Thei sien alle thingis, what euer thingis ben in myn hows; no thing is in my tresouris, which Y schewide not to hem.
16 Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena:
Therfor Isaie seide to Ezechie, Here thou the word of the Lord.
17 Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova.
Lo! dayes comen, and alle thingis that ben in thin hows, and `whiche thingis thi fadris maden til in to this dai, schulen be takun awey into Babiloyne; `not ony thing schal dwelle, seith the Lord.
18 Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”
But also of thi sones, that schulen go out of thee, whiche thou schalt gendere, schulen be takun, and thei schulen be geldyngis in the paleis of the king of Babiloyne.
19 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’”
Ezechie seide to Isaie, The word of the Lord, `which he spak, is good; ooneli pees and treuthe be in my daies.
20 Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Forsothe the residue of wordis of Ezechie, and al his strengthe, and hou he made a cisterne, and a watir cundijt, and brouyte watris, `in to the citee, whether these ben not writun in the book of wordis of daies of the kyngis of Juda?
21 Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Ezechie slepte with hise fadris, and Manasses, his sone, regnyde for hym.

< 2 Mafumu 20 >