< 2 Mafumu 17 >

1 Mʼchaka cha 12 cha Ahazi mfumu ya Yuda, Hoseya mwana wa Ela anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka zisanu ndi zinayi.
Dvanaeste godine carovanja Ahazova nad Judom zacari se u Samariji nad Izrailjem Osija sin Ilin, i carova devet godina.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi mafumu a Israeli amene ankalamulira iye asanalowe ufumuwo.
I èinjaše što je zlo pred Gospodom, ali ne kao carevi Izrailjevi koji biše prije njega.
3 Salimenezeri mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo Hoseya amene anali pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iyeyo.
Na njega doðe Salmanasar car Asirski, i Osija mu posta sluga, te mu plaæaše danak.
4 Koma mfumu ya ku Asiriya inazindikira kuti Hoseya akuwukira, pakuti Hoseyayo anali atatumiza nthumwi kwa So mfumu ya Igupto ndiponso analeka kukhoma msonkho kwa mfumu ya ku Asiriya, monga ankachitira chaka ndi chaka. Choncho Salimenezeri anagwira Hoseya ndi kumuyika mʼndende.
Ali car Asirski opazi da Osija hoæe da se odmetne, jer Osija posla poslanike k Soju caru Misirskom i ne posla danka godišnjega caru Asirskom; zato ga opkoli car Asirski i svezavši baci ga u tamnicu.
5 Mfumu ya ku Asiriya inapita kukathira nkhondo dziko lonse la Israeli ndipo inapita mpaka ku Samariya ndipo inazinga mzindawo kwa zaka zitatu.
I car Asirski proðe svu zemlju i doðe na Samariju, i bi je tri godine.
6 Mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya, mfumu ya ku Asiriya inalanda Samariya ndipo inatenga Aisraeli ndi kupita nawo ku Asiriya. Anakawakhazika ku Hala ndi Habori mʼmbali mwa mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
Devete godine Osijine uze car Asirski Samariju i odvede Izrailja u Asiriju i naseli u Alaju i u Avoru na vodi Gozanu i u gradovima Midskim.
7 Zonsezi zinachitika chifukwa Aisraeli anachimwira Yehova Mulungu wawo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto pansi pa ulamuliro wa Farao mfumu ya Igupto. Iwo ankapembedza milungu ina,
A to bi što sinovi Izrailjevi griješiše Gospodu Bogu svojemu, koji ih je izveo iz zemlje Misirske ispod ruke Faraona cara Misirskoga, i bojaše se drugih bogova,
8 ndiponso ankatsatira miyambo ya anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika mʼdzikomo pamodzinso ndi miyambo yonse imene mafumu a Israeli anayambitsa.
I hodiše po uredbama naroda koje odagna Gospod ispred sinova Izrailjevijeh, i kako èiniše carevi Izrailjevi;
9 Ndipo Aisraeli ankachita zoyipa mwamseri kutsutsana ndi Yehova Mulungu wawo. Kuchokera ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa, mʼmizinda yawo yonse anamangamo malo opembedzeramo mafano.
I tajno èiniše sinovi Izrailjevi što nije pravo pred Gospodom Bogom njihovijem, i pogradiše visine po svijem gradovima svojim, od kule stražarske do gradova ozidanijeh.
10 Anayimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya mafano a Asera pa phiri lililonse lalitali ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
I podigoše likove i lugove na svakom visokom humu i pod svakim zelenijem drvetom.
11 Pa malo aliwonse opembedzera mafano, anthuwa ankafukiza lubani monga momwe ankachitira anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika. Iwo anachita zinthu zoyipa zomwe zinaputa mkwiyo wa Yehova.
I kaðahu onuda po svijem visinama kao narodi koje odagna Gospod ispred njih, i èinjahu zle stvari gnjeveæi Gospoda.
12 Ndipo iwowo ankapembedza mafano ngakhale Yehova ananena kuti, “Musadzachite zimenezi.”
I služahu gadnijem bogovima, za koje im bješe Gospod rekao: ne èinite to.
13 Yehova anachenjeza Israeli ndi Yuda kudzera mwa aneneri ake onse ndi alosi kuti, “Lekani mchitidwe wanu woyipawo. Mverani malamulo anga ndi malangizo anga potsatira zonse zolembedwa mʼmalamulo a Mose, zimene ndinalamulira makolo anu kuti azimvere, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”
I Gospod opominjaše Izrailja i Judu preko svijeh proroka i svijeh vidjelaca govoreæi: vratite se sa zlijeh putova svojih i držite zapovijesti moje i uredbe moje po svemu zakonu koji sam zapovjedio ocima vašim i koji sam vam poslao po slugama svojim prorocima.
14 Koma anthuwa sanamvere ndipo anawumitsa khosi ngati momwe analili makolo awo, amene sanadalire Yehova Mulungu wawo.
Ali ne poslušaše; nego bjehu tvrdovrati kao i oci njihovi, koji ne vjerovaše Gospodu Bogu svojemu.
15 Anakana malangizo ake ndi pangano anachita ndi makolo awo ndipo ananyoza zochenjeza za Yehova. Iwo anatsatira mafano achabechabe nasanduka achabechabe. Anthuwa anatsanzira mitundu ya anthu owazungulira ngakhale kuti Yehova anawalamula kuti, “Musamachite zomwe iwo amachita,” koma iwo anachita zomwe Yehova anawaletsa.
I odbaciše uredbe njegove i zavjet njegov, koji uèini s ocima njihovijem, i svjedoèanstva njegova, kojima im svjedoèaše, i hodiše za ništavilom i postaše ništavi, i za narodima koji bijahu oko njih, za koje im bješe zapovjedio Gospod da ne èine kao oni.
16 Iwowo anasiya malamulo onse a Yehova Mulungu wawo, nadzipangira mafano awiri osungunula a ana angʼombe ndiponso fano la Asera, napembedza zonse zamlengalenga ndi kutumikira Baala.
I ostaviše sve zapovijesti Gospoda Boga svojega, i naèiniše sebi livene likove, dva teleta, i lugove, i klanjaše se svoj vojsci nebeskoj, i služiše Valu.
17 Ndipo anadutsitsa mʼmoto ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo ankawombeza mawula, namachitanso zanyanga ndipo anadzipereka kuchita zoyipa pamaso pa Yehova namukwiyitsa.
I provodiše sinove svoje i kæeri svoje kroz oganj, i davaše se na vraèanje i gatanje, i prodaše se da èine zlo pred Gospodom gnjeveæi ga.
18 Choncho Yehova anakwiya nawo kwambiri Aisraeli ndipo anawachotsa pamaso pake. Palibe amene anatsala kupatula fuko la Yuda lokha.
Zato se Gospod razgnjevi vrlo na Izrailja, i odbaci ih od sebe, te ne osta nego samo pleme Judino.
19 Yuda nayenso sanasunge malamulo a Yehova Mulungu wawo. Iwo ankatsatira machitidwe amene Israeli anayambitsa.
Pa ni Juda ne držaše zapovijesti Gospoda Boga svojega, nego hoðaše po uredbama koje naèiniše Izrailjci.
20 Motero Yehova anakana Aisraeli onse. Iye anawazunza nawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha mpaka Iye atawachotseratu pamaso pake.
Zato Gospod povrže sve sjeme Izrailjevo, i muèi ih, i predade ih u ruke onima koji ih plijene, dokle ih i odbaci od sebe.
21 Yehova atangʼamba Israeli kumuchotsa ku nyumba ya Davide, Aisraeliwo anasankha Yeroboamu mwana wa Nebati kukhala mfumu yawo. Yeroboamu ananyengerera Aisraeli kuti asatsatire Yehova ndipo anawachimwitsa tchimo lalikulu.
Jer se ocijepiše Izrailjci od doma Davidova, i postaviše carem Jerovoama sina Navatova, a Jerovoam odbi Izrailjce od Gospoda i navede ih da griješe grijehom velikim.
22 Aisraeli anakakamira machimo onse amene Yeroboamu anachita ndipo sanawasiye
I hodiše sinovi Izrailjevi u svijem grijesima Jerovoamovijem koje je on èinio, i ne otstupiše od njih;
23 mpaka pamene Yehova anawachotsa pamaso pake monga anawachenjezera kudzera mwa atumiki ake onse, aneneri. Choncho Aisraeli anachotsedwa mʼdziko lawo kupita ku ukapolo ku Asiriya ndipo ali komweko mpaka lero lino.
Dokle Gospod ne odbaci Izrailja od sebe kao što je govorio preko svijeh sluga svojih proroka, i tako preseljen bi Izrailj iz zemlje svoje u Asirsku do današnjega dana.
24 Mfumu ya ku Asiriya inabweretsa anthu a ku Babuloni, Kuta, Awa, Hamati ndi a ku Sefaravaimu kudzawakhazika mʼmizinda ya Samariya kulowa mʼmalo mwa Aisraeli. Iwo anatenga Samariya ndi kukhala mʼmizinda yake.
Potom dovede car Asirski ljude iz Vavilona i iz Hute i iz Ave i iz Emata i iz Sefarvima, i naseli ih u gradovima Samarijskim mjesto Izrailjaca, i naslijediše Samariju, i življahu po gradovima njezinijem.
25 Iwo atayamba kukhala kumeneko, sanapembedze Yehova choncho Yehova anatumiza mikango pakati pawo ndipo inapha ena mwa iwo.
A kad poèeše živjeti ondje, ne bojahu se Gospoda, a Gospod posla na njih lavove, koji ih davljahu.
26 Tsono mfumu ya ku Asiriya inawuzidwa za nkhaniyi kuti, “Anthu amene munawatumiza ndi kuwakhazika mʼmizinda ya Samariya sakudziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna. Choncho Iye watumiza mikango pakati pawo imene ikuwapha chifukwa anthuwo sadziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
Zato rekoše caru Asirskom govoreæi: ovi narodi koje si doveo i naselio u gradovima Samarijskim ne znaju zakona Boga one zemlje; zato posla na njih lavove, koji ih eto more, jer ne znaju zakona Boga one zemlje.
27 Tsono mfumu ya ku Asiriya inalamula kuti, “Tengani wansembe mmodzi mwa amene munawagwira ukapolo, mupite naye kumeneko ndipo akakhale komweko nakaphunzitse anthu zimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
Tada zapovjedi car Asirski i reèe: odvedite onamo jednoga od sveštenika koje ste doveli odande, pa neka ide i sjedi ondje, neka ih uèi zakonu Boga one zemlje.
28 Choncho mmodzi mwa ansembe amene anawatenga ku Samariya anabwera kudzakhala ku Beteli ndipo ankaphunzitsa anthuwo kupembedza Yehova.
I tako jedan od sveštenika, koje bijahu odveli iz Samarije, doðe i nastani se u Vetilju, i uèaše ih kako æe se bojati Gospoda.
29 Koma mtundu uliwonse wa anthu unkapangabe mafano a milungu yawoyawo mʼmizinda yambiri imene anthuwo ankakhala, ndipo anayika milunguyo mʼnyumba za milungu zimene anthu a ku Samariya anamanga ku malo opembedzera mafano.
Ali naèiniše sebi svaki narod svoje bogove, i pometaše ih u kuæe visina, koje bijahu naèinili Samarijani, svaki narod u svojim gradovima u kojima življahu.
30 Anthu a ku Babuloni anapanga Sukoti-Benoti, anthu a ku Kuti anapanga Nerigali, ndipo anthu a ku Hamati anapanga Asima;
Jer Vavilonjani naèiniše Sokot-Venotu, a Huæani naèiniše Nergala, a Emaæani naèiniše Asima;
31 Aava anapanga Nibihazi ndi Taritaki, ndipo Asefaravaimu ankawotcha ana awo pa moto ngati nsembe kwa Adirameleki ndi Anameleki, milungu ya Asefaravaimu.
I Avljani naèiniše Nivaza i Tartaka, a Sefarvimci spaljivahu sinove svoje ognjem Adramelehu i Anamelehu bogovima Sefarvimskim.
32 Iwo ankapembedza Yehova, koma ankadzisankhira okha pakati pawo anthu wamba kuti akhale ansembe awo ku nyumba za milungu za ku malo opembedzera mafano.
Ali se bojahu Gospoda, i postaviše izmeðu sebe sveštenike visinama, koji im služahu u domovima visina;
33 Iwowo ankapembedza Yehova, komanso ankatumikira milungu yawo molingana ndi miyambo ya mitundu ya kumene ankachokera.
Bojahu se Gospoda, ali i svojim bogovima služahu po obièaju onijeh naroda iz kojih ih preseliše.
34 Mpaka lero lino iwo akupitirizabe kuchita zimene ankachita poyamba. Sapembedza Yehova kapenanso kutsata malangizo ake ndi malamulo ake, chiphunzitso chake monga mwa malamulo amene Yehova anawapereka kwa zidzukulu za Yakobo, amene anamutcha Israeli.
I do današnjega dana rade po starijem obièajima; ne boje se Gospoda a ne rade ni po svojim uredbama i obièajima, ni po zakonu i zapovijesti što je zapovjedio Gospod sinovima Jakova, kojemu nadje ime Izrailj;
35 Pamene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli, Iye anawalamula kuti, “Musapembedze milungu ina kapena kuyigwadira iyo, kuyitumikira kapena kupereka nsembe kwa iyoyo.
S kojima uèini Gospod zavjet i zapovjedi im i reèe: ne bojte se drugih bogova niti im se klanjajte niti im služite niti im prinosite žrtava;
36 Koma Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndiye amene muyenera kumupembedza.
Nego Gospoda, koji vas je izveo iz zemlje Misirske silom velikom i mišicom podignutom, njega se bojte i njemu se klanjajte i njemu prinosite žrtve;
37 Muyenera kusamalitsa nthawi zonse kusunga malangizo anga ndi malemba anga, chiphunzitso ndi malamulo amene anakulemberani. Musapembedze milungu ina.
I uredbe i pravila i zakon i zapovijesti što vam je napisao držite izvršujuæi ih vazda, i ne bojte se drugih bogova.
38 Musayiwale pangano limene ndinapangana nanu ndipo musamapembedze milungu ina.
I ne zaboravljajte zavjeta koji je uèinio s vama, i ne bojte se drugih bogova.
39 Mʼmalo mwake muzipembedza Yehova Mulungu wanu pakuti ndiye amene adzakulanditsani mʼdzanja la adani anu onse.”
Nego Gospoda Boga svojega bojte se, i on æe vas izbaviti iz ruku svijeh neprijatelja vaših.
40 Komabe iwo sanamvere ndipo anapitiriza kuchita zomwe ankachita kale.
Ali ne poslušaše, nego radiše po starom svom obièaju.
41 Ngakhale anthuwo ankapembedza Yehova, ankatumikiranso mafano awo. Mpaka lero lino ana awo ndi zidzukulu zawo zikupitiriza kuchita zomwe ankachita makolo awo.
Tako ovi narodi bojahu se Gospoda i idolima svojim služahu; i sinovi njihovi i sinovi sinova njihovijeh èine do današnjega dana onako kako su èinili oci njihovi.

< 2 Mafumu 17 >