< 2 Mafumu 14 >

1 Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
I Joahaz' Søns, Kong Joas af Israel, andet Regeringsår blev Amazja, Joas's Søn, Konge over Juda.
2 Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
Han var fem og tyve År gammel, da han blev Konge, og han herskede ni og tyve År i Jerusalem. Hans Moder hed Jehoaddan og var fra Jerusalem.
3 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
Han gjorde, hvad der var ret i HERRENs Øjne, om end ikke som hans Fader David; han handlede ganske som sin Fader Joas.
4 Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
Hun forsvandt Offerhøjene ikke. men Folket blev ved med at ofre og tænde Offerild på Højene.
5 Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
Da han havde sikret sig Magten, lod han dem af sine Folk dræbe, der havde dræbt hans Fader Kongen;
6 Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
men Mordernes Børn lod han ikke ihjelslå, i Henhold til hvad der står skrevet i Moses's Lovbog, hvor HERREN byder: "Fædre skal ikke lide Døden for Børns Skyld, og Børn skal ikke lide Døden for Fædres Skyld. Men enhver skal lide Døden for sin egen Synd."
7 Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
Det var ham, der slog Edom i Saltdalen, 10.000 Mand, og indtog Sela, og han kaldte det Jokte'el, som det hedder den Dag i Dag.
8 Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
Ved den Tid sendte Amazja Sendebud til Jebus Søn Joahaz's Søn, Kong Joas af Israel, og lod sige: "Kom, lad os se hinanden under Øjne!"
9 Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
Men Kong Joas af Israel sendte Kong Amazja af Juda det Svar: "Tidselen på Libanon sendte engang det Bud til Cederen på Libanon: Giv min Søn din Datter til Ægte! Men Libanons vilde byr løb hen over Tidselen og trampede den ned.
10 Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
Du har slået Edom, og det har gjort dig overmodig; lad dig nu nøje med den Ære og bliv, hvor du er! Hvorfor vil du udfordre Ulykken og udsætte både dig selv og Juda for Fald?"
11 Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
Men Amazja vilde intet høre. Så drog Kong Joas af Israel ud, og han og Kong Amazja af Juda så hinanden under Øjne ved Bet Sjemesj i Juda;
12 Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
Juda blev slået af Israel, og de flygtede hver til sit.
13 Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
Men Kong Joas af Israel tog Ahazjas Søn Joas's Søn. Kong Amazja af Juda, til Fange ved BetSjemesj og førte ham til Jerusalem. Derpå nedrev han Jerusalems Mur på en Strækning af 400 Alen, fra Efraimsporten til Hjørneporten;
14 Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
og han tog alt det Guld og Sølv og alle de Kar, der fandtes i HERRENs Hus og i Skatkammeret i Kongens Palads; desuden tog han Gidsler og vendte så tilbage til Samaria.
15 Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
Hvad der ellers er at fortælle om Joas, alt, hvad han udførte, og alle hans Heltegerninger, og hvorledes han førte Krig med Kong Amazja af Juda, står jo optegoet i Israels Kongers Krønike.
16 Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
Så lagde Joas sig til Hvile hos sine Fædre og blev jordet i Samaria hos Israels Konger; og hans Søn Jeroboam blev Konge i hans Sted.
17 Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
Joas's Søn, Kong Amazja af Juda, levede endnu femten År, efter at Joahaz's Søn, Kong Joas af Israel, var død.
18 Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Hvad der ellers er at fortælle om Amazja, står jo optegnet i Judas Kongers Krønike.
19 Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
Da der stiftedes en Sammensværgelse mod ham i Jerusalem, flygtede han til Lakisj; men der blev sendt Folk efter ham til Lakisj, og de dræbte ham der.
20 Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
Så løftede man ham op på Heste, og han blev jordet i Jerusalem hos sine Fædre i Davidsbyen.
21 Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
Hele Folket i Juda tog så Azarja, der dengang var seksten År gammel, og gjorde ham til Konge i hans Fader Amazjas Sted.
22 Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
Det var ham, der befæstede Elat og atter forenede det med Juda, efter at Kongen havde lagt sig til Hvile hos sine Fædre.
23 Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
I Joas's Søns, Kong Amazja af Judas, femtende Regeringsår ble Jeroboam, Joas's Søn, Konge over Israel, og han herskede een og fyrretyve År i Samaria.
24 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
Han gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne, og veg ikke fra nogen af de Synder, Jeroboam, Nebats Søn, havde forledt Israel til.
25 Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
Han tog Israels Landområde tilbage fra Egnen hen imod Hamat og til Arabasøen, efter det Ord, HERREN, Israels Gud, havde talet ved sin Tjener, Profeten Jonas, Amittajs Søn, fra Gat-Hefer.
26 Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
Thi HERREN havde set Israels bitre Kvide, hvorledes de reves bort alle som een, fordi Israel ikke havde nogen Hjælper;
27 Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
og HERREN havde ikke talet om, at han vilde udslette Israels Navn under Himmelen, derfor frelste han dem ved Jeroboam, Joas's Søn.
28 Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
Hvad der ellers er at fortælle om Jeroboam, alt, hvad han udførte, og hans Heltegerninger, hvorledes han førte Krig, og hvorledes han tog Damaskus og Hamat til bage til Israel, står jo optegnet i Israels Kongers Krønike.
29 Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Så lagde Jeroboam sig til Hvile hos sine Fædre og blev jordet i Samaria hos Israels Konger; og hans Søn Zekarja blev Konge i hans Sted.

< 2 Mafumu 14 >