< 2 Mbiri 5 >

1 Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.
Et ainsi fut terminé tout l'ouvrage exécuté par Salomon pour le Temple de l'Éternel, et Salomon introduisit ce que David, son père, avait consacré; et l'argent et l'or et tout le mobilier, il le mit dans le Trésor de la Maison de Dieu.
2 Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide.
Alors Salomon assembla les Anciens d'Israël et tous les chefs des Tribus, les princes des maisons patriarcales des enfants d'Israël, à Jérusalem pour transférer l'Arche d'Alliance de l'Éternel de la Cité de David, c'est-à-dire, de Sion.
3 Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
Et auprès du roi s'assemblèrent tous les hommes d'Israël à la Fête (c'était le septième mois).
4 Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano,
Et vinrent tous les Anciens d'Israël, et les Lévites portèrent l'Arche.
5 ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula,
Et ils apportèrent l'Arche et la Tente du Rendez-vous et tout le mobilier sacré qui était dans la Tente, ces objets furent apportés par les Prêtres, les Lévites.
6 ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.
Et le roi Salomon et toute l'Assemblée d'Israël qui s'était réunie auprès de lui, devant l'Arche sacrifièrent des brebis et des bœufs qui ne pouvaient se nombrer, ni se compter, tant il y en avait.
7 Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi.
Et les Prêtres introduisirent l'Arche d'Alliance de l'Éternel à sa place, dans le Sanctuaire de l'édifice, dans le Lieu Très-Saint au-dessous des ailes des Chérubins.
8 Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira.
Et les Chérubins avaient les ailes étendues sur l'emplacement de l'Arche, et les Chérubins couvraient l'Arche et ses barres d'en haut.
9 Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino.
Et les barres étaient assez longues pour que de l'Arche devant le Sanctuaire on pût en voir les extrémités, mais du dehors on ne les apercevait pas, et elle y a été jusqu'à ce jour.
10 Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
Il n'y avait rien dans l'Arche que les deux Tables qu'y avait mises Moïse en Horeb, quand l'Éternel fit alliance avec les enfants d'Israël à leur sortie de l'Egypte.
11 Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera.
Et lorsque les Prêtres sortirent du Lieu-Saint, (car tous les Prêtres présents s'étaient mis en état de sainteté, sans égard à la distinction des classes)
12 Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi.
et lorsque les Lévites, les Chantres, eux tous, savoir Asaph, Heiman et Jeduthun, et leurs fils et leurs frères, vêtus de byssus et munis de cymbales, de harpes et de luths furent debout, au côté oriental de l'autel accompagnés de cent vingt Prêtres sonnant des trompettes,
13 Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti, “Yehova ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.” Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo,
et lorsque, comme un seul homme, les trompettes et les chantres entonnèrent tout d'une voix la louange de l'Éternel et l'action de grâces à l'Éternel, et lorsqu'ils poussèrent leur voix au bruit des trompettes et des cymbales et des instruments à cordes et louant l'Éternel de ce qu'il est bon et sa miséricorde éternelle, alors l'édifice, le temple de l'Éternel se remplit d'une nuée,
14 choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.
et les Prêtres ne pouvaient y tenir pour faire leur service, par l'effet de la nuée, caria gloire de l'Éternel avait rempli la Maison de Dieu.

< 2 Mbiri 5 >