< 2 Mbiri 5 >

1 Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.
Therfor Salomon brouyte in alle thingis, siluer and gold, whiche Dauid, his fadir, hadde avowid; and he puttide alle vesselis in the tresouris of the hows of the Lord.
2 Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide.
After whiche thingis he gaderide togidere alle the grettere men in birthe of Israel, and alle the princes of lynagis, and the heedis of meynees, of the sones of Israel, in to Jerusalem, that thei schulden brynge the arke of boond of pees of the Lord fro the citee of Dauid, which is Syon.
3 Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
Therfor alle men of Israel camen to the kyng, in the solempne dai of the seuenthe monethe.
4 Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano,
And whanne alle the eldre men of Israel `weren comen, the dekenes baren the arke,
5 ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula,
and brouyten it in, and al the aray of the tabernacle. Forsothe the preestis with the dekenes baren the vessels of seyntuarie, that weren in the tabernacle.
6 ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.
Sotheli kyng Salomon, and alle the cumpenyes of Israel, and alle that weren gaderid to gidere, offriden bifor the arke wetheris and oxis with outen ony noumbre; for the multitude of slayn sacrifices was `so greet.
7 Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi.
And preestis brouyten the arke of boond of pees of the Lord in to his place, that is, to Goddis answeryng place of the temple, in to the hooli of hooli thingis, vndur the wyngis of cherubyns;
8 Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira.
so that cherubyns spredden forth her wyngis ouer the place, in which the arke was put, and hiliden thilke arke with hise barris.
9 Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino.
Sotheli the heedis, by which the arke was borun, weren opyn bifor Goddis answeryng place, for tho heedis weren a litil lengere; but if a man hadde be a litil with out forth, he myyt not se tho barris. Therfor the arke was there til in to present dai;
10 Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
and noon other thing was in the arke, no but twei tablis, whiche Moyses hadde put in Oreb, whanne the Lord yaf the lawe to the sones of Israel goynge out of Egipt.
11 Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera.
Forsothe the prestis yeden out of the seyntuarie, for alle preestis, that myyten be foundun there, weren halewid, and the whiles, and the ordre of seruyces among hem was not departid yit in that tyme;
12 Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi.
bothe dekenes and syngeris, that is, bothe thei that weren vndur Asaph, and thei that weren vndur Eman, and thei that weren vndur Idithum, her sones and britheren, clothid with white lynun clothis, sownyden with cymbalis and sautrees and harpis, and stoden at the west coost of the auter, and with hem weren sixe score preestis trumpynge.
13 Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti, “Yehova ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.” Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo,
Therfor whanne alle sungen togidur both with trumpis, and vois, and cymbalis, and orguns, and of dyuerse kynde of musikis, and reisiden the vois an hiy, the sown was herd fer, so that whanne thei hadden bigunne to preyse the Lord, and to seie, Knouleche ye to the Lord, for he is good, for his mercy is in to the world, `ether, with outen ende; the hows of God was fillid with a cloude,
14 choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.
and the preestis miyten not stonde and serue for the derknesse; for the glorie of the Lord hadde fillid the hows of the Lord.

< 2 Mbiri 5 >