< 2 Mbiri 35 >

1 Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.
Potem Jozjasz obchodził w Jerozolimie święto Paschy dla PANA. I zabito baranka paschalnego czternastego [dnia] pierwszego miesiąca.
2 Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova.
Ustanowił też kapłanów na swoich urzędach i zachęcił ich do służby w domu PANA.
3 Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli.
I powiedział Lewitom, którzy nauczali całego Izraela i byli poświęceni PANU: Ustawcie świętą arkę w domu, który zbudował syn Dawida Salomon, król Izraela. Nie będziecie już jej dźwigać na swoich ramionach. Teraz służcie PANU, swojemu Bogu, i jego ludowi Izraela;
4 Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.
Przygotujcie się według waszych rodów i według waszych zmian, jak napisał Dawid, król Izraela, i jak napisał jego syn Salomon;
5 “Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba.
I stójcie w świątyni według podziału na rody waszych braci, którzy są z ludu, i według podziału na rody Lewitów.
6 Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”
Wtedy zabijcie baranka paschalnego, poświęćcie się i przygotujcie waszych braci, by wszystko czynić według słowa PANA [przekazanego] przez Mojżesza.
7 Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.
Potem Jozjasz dał ludowi jagnięta i koźlęta z trzody, wszystkie na ofiary święta Paschy dla wszystkich obecnych w liczbie trzydziestu tysięcy, oraz trzy tysiące wołów. To [wszystko] pochodziło z dóbr króla.
8 Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300.
Jego książęta złożyli dobrowolne dary ludowi, kapłanom i Lewitom: Chilkiasz, Zachariasz, Jechiel, przełożeni domu Bożego, dali kapłanom na ofiary święta Paschy dwa tysiące sześćset [jagniąt] i trzysta wołów.
9 Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.
Ponadto Konaniasz i jego bracia Szemejasz i Netaneel oraz Chaszabiasz, Jejel i Jozabad, naczelnicy z Lewitów, dali [innym] Lewitom na ofiary święta Paschy pięć tysięcy [jagniąt] i pięćset wołów.
10 Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira.
Wszystko więc zostało przygotowane do służby, kapłani stanęli na swoich miejscach, a Lewici w swoich zmianach według rozkazu króla.
11 Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo.
I zabili baranki paschalne, kapłani kropili [ich] krwią, a Lewici obdzierali [je] ze skóry.
12 Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe.
Następnie oddzielili [część] z nich na całopalenie, aby dać [je] ludowi według podziału na rody jako ofiarę dla PANA, tak jak jest napisane w księdze Mojżesza. Podobnie też [uczyniono] z wołami.
13 Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse.
I piekli baranki paschalne na ogniu według zwyczaju, inne zaś [ofiary] święte gotowali w garnkach, kotłach i rondlach, po czym rozdawali szybko całemu ludowi.
14 Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.
Potem też przygotowali [posiłek] dla siebie i kapłanów. Kapłani bowiem, synowie Aarona, byli [zajęci] składaniem całopaleń i tłuszczu aż do nocy. Lewici więc przygotowali [posiłek] dla siebie i dla kapłanów, synów Aarona.
15 Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.
Śpiewacy, synowie Asafa, [stali] na swoich stanowiskach według rozkazu Dawida, Asafa, Hemana i Jedutuna, widzącego króla. Odźwierni też [stali] przy każdej bramie. Nie musieli opuszczać swojej służby, ponieważ ich bracia Lewici przygotowywali dla nich [posiłki].
16 Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya.
Tak więc cała służba została przygotowana w tym dniu, aby obchodzić święto Paschy i składać całopalenia na ołtarzu PANA według rozkazu króla Jozjasza.
17 Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri.
Synowie Izraela, którzy tam się znajdowali, obchodzili w tym czasie święto Paschy, a Święto Przaśników przez siedem dni.
18 Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu.
Żadne święto Paschy podobne do tego nie było obchodzone w Izraelu od czasów proroka Samuela i żaden z królów Izraela nie obchodził tak święta Paschy, jak obchodzili [je] Jozjasz, kapłani, Lewici, cały lud Judy i Izraela, który się tam znajdował, oraz mieszkańcy Jerozolimy.
19 Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.
Paschę tę obchodzono w osiemnastym roku panowania Jozjasza.
20 Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye.
Po tym wszystkim, gdy Jozjasz naprawił dom [Boży], nadciągnął Necho, król Egiptu, aby walczyć przeciw Karkemisz nad [rzeką] Eufrat, a Jozjasz wyruszył mu naprzeciw.
21 Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”
Ale on posłał do niego swoich posłańców ze słowami: Co ja mam z tobą, królu Judy? Nie przeciw tobie [ciągnę] dzisiaj, lecz przeciwko domowi, który ze mną walczy. I Bóg nakazał mi, abym się pospieszył. Przestań walczyć z Bogiem, który [jest] ze mną, aby cię nie zniszczył.
22 Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.
Ale Jozjasz nie odwrócił się od niego, lecz zmienił swoje szaty, aby z nim walczyć, i nie posłuchał słów Necho, [które pochodziły] z ust Boga. Tak więc wyruszył, aby walczyć na równinie Megiddo.
23 Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.”
A łucznicy ugodzili króla Jozjasza i wtedy król powiedział do swoich sług: Wyprowadźcie mnie, bo jestem ciężko ranny.
24 Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.
Jego słudzy więc wyciągnęli go z rydwanu i wsadzili na inny rydwan, który należał do niego: zawieźli go do Jerozolimy i tam umarł. Potem pogrzebali go w grobach jego ojców, a cały lud Judy i Jerozolimy opłakiwał Jozjasza.
25 Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.
Jeremiasz też lamentował nad Jozjaszem, a wszyscy śpiewacy i śpiewaczki wspominają Jozjasza w swoich lamentacjach aż do dziś, i uczynili z tego zwyczaj w Izraelu. Oto są zapisane w lamentacjach.
26 Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova,
A pozostałe dzieje Jozjasza, jego życzliwość według tego, co jest napisane w Prawie PANA;
27 zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.
I jego czyny pierwsze i ostatnie są zapisane w księdze królów Izraela i Judy.

< 2 Mbiri 35 >