< 2 Mbiri 33 >

1 Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 55.
Dvanaest godina bješe Manasiji kad poèe carovati, i carova pedeset i pet godina u Jerusalimu.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira machitidwe a mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
A èinjaše što je zlo pred Gospodom po gadnijem djelima onijeh naroda koje odagna Gospod ispred sinova Izrailjevijeh.
3 Iyeyo anamanganso malo opembedzerapo mafano amene Hezekiya abambo ake anawaphwasula; anamanganso maguwa ansembe a Baala ndi kupanga mafano a Asera. Iye amagwadira zolengedwa zonse zamlengalenga ndi kumazipembedza.
Jer opet pogradi visine, koje bješe raskopao Jezekija otac njegov, i podiže oltare Valima, i naèini lugove, i klanjaše se svoj vojsci nebeskoj i služaše joj.
4 Manase anamanga maguwa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Ine ndidzakhala mu Yerusalemu mpaka muyaya.”
Naèini oltare i u domu Gospodnjem, za koji bješe rekao Gospod: u Jerusalimu æe biti ime moje dovijeka.
5 Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova anamangamo maguwa ansembe a zolengedwa zonse zamlengalenga.
Naèini oltare svoj vojsci nebeskoj u dva trijema doma Gospodnjega.
6 Iye ankakapereka ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza ku chigwa cha Hinomu, ankachita zamatsenga, kuwombeza ndi ufiti, ankakafunsira kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Iye anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova, kumukwiyitsa Iyeyo.
I provodi sinove svoje kroz oganj u dolini sina Enomova, i gledaše na vremena i gataše i vraèaše, i uredi one što se dogovaraju s duhovima i vraèare, i èinjaše vrlo mnogo što je zlo pred Gospodom gnjeveæi ga.
7 Manase anatenga fano losema limene anapanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Mulungu, zimene Mulungu ananena kwa Davide ndi kwa mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba ya Mulungu muno, mu Yerusalemu muno, malo amene ndawasankha pakati pa mafuko onse a Israeli, ndidzakhalamo mpaka muyaya.
I postavi lik rezan koji naèini u domu Božijem, za koji bješe rekao Bog Davidu i Solomunu sinu njegovu: u ovom domu i u Jerusalimu, koji izabrah izmeðu svijeh plemena Izrailjevijeh, namjestiæu ime svoje dovijeka.
8 Ine sindidzachotsanso phazi la Aisraeli kuchoka mʼdziko limene ndawapatsa makolo ako, ngatitu iwowa adzasamalira kuchita chilichonse chimene ndinawalamulira za malamulo onse, malangizo ndi miyambo imene inapatsidwa kudzera mwa Mose.”
I neæu više krenuti noge sinovima Izrailjevijem iz zemlje koju sam odredio ocima vašim, ako samo uzdrže i ustvore sve što sam im zapovjedio preko Mojsija, sav zakon i uredbe i sudove.
9 Koma Manase anasocheretsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu, kotero anachita zoyipa zambiri kupambana mitundu imene Yehova anayiwononga pamaso pa Aisraeli.
Ali Manasija zavede Judu i Jerusalim, te èiniše gore nego narodi koje istrijebi Gospod ispred sinova Izrailjevijeh.
10 Yehova anayankhula kwa Manase ndi anthu ake, koma iwo sanasamaleko.
I Gospod govoraše Manasiji i narodu njegovu, ali ne htješe slušati.
11 Kotero Yehova anawatumizira atsogoleri a ankhondo a ku Asiriya amene anagwira Manase ukapolo, anayika ngowe mʼmphuno mwake, namumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
Zato dovede Gospod na njih glavare od vojske cara Asirskoga, i uhvatiše Manasiju u trnju, i svezavši ga u dvoje verige mjedene odvedoše ga u Vavilon.
12 Ali pa mavuto akewo anafunafuna kuti Yehova Mulungu wake amukomere mtima ndipo anadzichepetsa kwakukulu pamaso pa Mulungu wa makolo ake.
I kad bijaše u nevolji, moljaše se Gospodu Bogu svojemu, i ponizi se veoma pred Bogom otaca svojih.
13 Ndipo atapemphera, Yehova anakhudzidwa ndi kupempha kwakeko ndipo anamvera madandawulo ake. Kotero anamubweretsanso ku Yerusalemu ndi ku ufumu wake. Ndipo Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu.
I moleæi se umoli mu se, te usliši molitvu njegovu i povrati ga u Jerusalim na carstvo njegovo. Tada pozna Manasija da je Gospod Bog.
14 Zitapita izi iye anamanga khoma la kunja kwa Mzinda wa Davide kumadzulo kwa kasupe wa Gihoni ku chigwa mpaka polowera ku Chipata cha Nsomba kuzungulira phiri la Ofeli. Iyeyo anakweza kwambiri khomalo. Anayikanso atsogoleri a nkhondo ku mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda.
A poslije toga ozida zid iza grada Davidova sa zapada Gionu, od samoga potoka pa do ribljih vrata i oko Ofila, i izvede ga vrlo visoko; i postavi vojvode po svijem tvrdijem gradovima Judinijem.
15 Iye anachotsa milungu yonse yachilendo ndi fano mʼNyumba ya Yehova komanso maguwa ansembe onse amene anamanga pa phiri la Nyumba ya Mulungu ndi mu Yerusalemu, nazitayira kunja kwa mzinda.
I iznese iz doma Gospodnjega bogove tuðe i lik i sve oltare koje bješe naèinio na gori doma Gospodnjega i u Jerusalimu, i baci iza grada.
16 Kenaka anabwezeretsa guwa lansembe la Yehova ndi kupereka zopereka zachiyanjano ndiponso zopereka zamatamando ndipo anawuza Yuda kuti atumikire Yehova Mulungu wa Israeli.
Pa opravi oltar Gospodnji i prinese na njemu žrtve zahvalne i u slavu, i zapovjedi Judejcima da služe Gospodu Bogu Izrailjevu.
17 Komabe anthu anapitiriza kupereka nsembe ku malo achipembedzo, koma kwa Yehova, Mulungu wawo yekha.
Ali narod još prinošaše žrtve na visinama, ali samo Gospodu Bogu svojemu.
18 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Manase, kuphatikiza mapemphero ake kwa Mulungu wake ndi mawu amene alosi anayankhula kwa iye mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli, zalembedwa mʼmabuku a mafumu a Israeli.
A ostala djela Manasijina i molitva njegova Bogu njegovu i rijeèi koje mu govoriše vidioci u ime Gospoda Boga Izrailjeva, to je sve u knjizi o carevima Izrailjevijem.
19 Pemphero lake ndi momwe Mulungu anakhudzidwira ndi kupempha kwakeko, pamodzinso ndi machimo ake onse ndi kusakhulupirika kwake, ndiponso malo onse amene anamanga, malo azipembedzo ndi mafano a Asera ndi mafano asanadzichepetse, zonse zalembedwa mʼmbiri ya alosi.
A molitva njegova i kako se umolio, i svi grijesi njegovi i prijestupi, i mjesta gdje je pogradio visine i podigao lugove i likove rezane prije nego se ponizi, to je sve zapisano u knjigama proroèkim.
20 Manase anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yake yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I poèinu Manasija kod otaca svojih, i pogreboše ga u domu njegovu. A na njegovo se mjesto zacari Amon sin njegov.
21 Amoni anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka ziwiri.
Dvadeset i dvije godine imaše Amon kad poèe carovati, i carova dvije godine u Jerusalimu.
22 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga anachitira Manase abambo ake. Amoni analambira ndi kupereka nsembe kwa mafano onse amene anapanga Manase.
I èinjaše što je zlo pred Gospodom kao što je èinio Manasija otac mu; jer svijem likovima rezanijem, koje naèini Manasija otac njegov, prinošaše Amon žrtve i služaše im.
23 Koma kusiyana ndi abambo ake Manase, iye sanadzichepetse pamaso pa Yehova. Amoni anawonjeza kulakwa kwake.
Ali se ne ponizi pred Gospodom, kao što se ponizi Manasija otac njegov; nego isti Amon još više griješaše.
24 Akuluakulu a Amoni anamuchita chiwembu ndipo anamupha mʼnyumba yake yaufumu.
I pobuniše se na nj sluge njegove, i ubiše ga u kuæi njegovoj.
25 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anakonzera chiwembu mfumu Amoni, ndipo anayika mwana wake Yosiya kukhala mfumu mʼmalo mwake.
Tada pobi narod zemaljski sve koji se bijahu pobunili na cara Amona, i zacari narod zemaljski Josiju sina njegova na njegovo mjesto.

< 2 Mbiri 33 >