< 2 Mbiri 32 >

1 Zitatha zonse zimene Hezekiya anachita mokhulupirika, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kuthira nkhondo dziko la Yuda. Iye anazinga mizinda yotetezedwa ya Yuda, kuganiza kuti ayigonjetsa.
Aftir whiche thingis and sich treuthe, Senacherib, the kyng of Assiriens, cam and entride in to Juda; and he bisegide stronge citees, and wolde take tho.
2 Pamene Hezekiya anaona kuti Senakeribu wabwera ndipo wakonzeka kuchita nkhondo ndi Yerusalemu,
And whanne Ezechie hadde herd this thing, that is, that Senacherib was comun, and that al the fersnesse of batel was turned ayens Jerusalem,
3 iye anakambirana ndi akuluakulu ake pamodzi ndi atsogoleri a gulu lankhondo za kutseka akasupe ochoka ku kasupe amene anali kunja kwa mzinda, ndipo iwo anamuthandiza.
he took counsel with the princes and strongest men, that thei schulden stoppe the heedis of wellis, that weren without the citee; and whanne the sentence of alle men demyde this,
4 Gulu lalikulu la anthu linasonkhana, ndipo anatseka akasupe onse pamodzi ndi mtsinje umene umayenda mʼkati mwa nthakamo. Iwo ankanena kuti, “Nʼchifukwa chiyani mafumu a Asiriya akabwera kuno adzapeze madzi ambiri?”
he gaderide togidere a ful greet multitude, and thei stoppiden alle the wellis, and the ryuer, that flowide in the myddis of the lond; and seiden, Lest the kyngis of Assiriens comen, and fynden abundance of watris.
5 Kenaka iye anagwira ntchito molimbika kukonza madera ogumuka a khoma ndi kumangapo msanja. Anamanganso mpanda wina kunja kwa mpanda winawo ndipo anamanga zolimbitsa Milo ku mzinda wa Davide.
Also he dide wittili, and bildide al the wal that was distride, and he bildide touris aboue, and an other wal withoutforth. And he reparilide Mello in the citee of Dauid; and made armure of al kynde, and scheldis.
6 Iye anasankha atsogoleri a ankhondo olamulira anthu ndipo anawasonkhanitsa pamaso pake pa bwalo la chipata cha mzinda ndi kuwalimbikitsa ndi mawu awa:
And he ordeynede princes of werriouris in the oost; and he clepide togidere alle men in the street of the yate of the citee, and spake to the herte of hem,
7 “Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite mantha kapena kutaya mtima chifukwa cha mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lalikulu lankhondo limene ali nalo, pakuti ife tili ndi mphamvu yayikulu kuposa imene ili ndi iye.
and seide, Do ye manli, and be ye coumfortid; nyle ye drede, nether be ye aferd of the kyng of Assiriens, and of al the multitude which is with him; for many mo ben with vs than with him.
8 Iye ali ndi mphamvu ya anthu basi, koma ife tili ndi Yehova Mulungu wathu kutithandiza ndi kuchita nkhondo zathu.” Ndipo anthu anapeza chilimbikitso kuchokera pa zimene Hezekiya mfumu ya Yuda ananena.
Fleischli arm is with him; `oure Lord God is with vs, which is oure helpere, and schal fiyte for vs. And the puple was coumfortid with sich wordis of Ezechie, kyng of Juda.
9 Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:
And aftir that these thingis weren doon, Sennacherib sente hise seruauntis to Jerusalem; for he `with al the oost bisegide Lachis. He sente to Ezechie, kyng of Juda, and to al the puple that was in the citee,
10 “Senakeribu mfumu ya ku Asiriya akuti: Kodi inu mukukhulupirira chiyani, kuti mukukhalabe mu Yerusalemu mutazingidwa?
and seide, Sennacherib, the kyng of Assiriens, seith these thingis, In whom han ye trist, and sitten bisegid in Jerusalem?
11 Pamene Hezekiya akunena kuti ‘Yehova Mulungu wathu adzatipulumutsa kuchoka mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya,’ iye akukusocheretsani, kuti mufe ndi njala ndi ludzu.
Whether Ezechie disseyueth you, that he bitake you to deeth in hungur and thirst, and affermeth, that `youre Lord God schal delyuere you fro the hond of the kyng of Assyriens?
12 Kodi si Hezekiya amene anachotsa malo opembedzerapo Mulungu ameneyu ndi maguwa ansembe ndi kunena kwa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe limodzi ndi kupserezapo nsembe?’
Whether not this is Ezechie, that distriede hiy places, and auteris of hym, and comaundide to Juda and to Jerusalem, and seide, Ye schulen worschipe bifor oon auter, and therynne ye schulen brenne encense?
13 “Kodi inu simukudziwa zimene ine ndi makolo anga tachita kwa anthu a mitundu ina? Kodi milungu ya mitundu imeneyi inatha kupulumutsa dziko lawo kuchoka mʼdzanja langa?
Whether ye witen not what thingis Y haue do, and my fadir, to alle the puplis of londis? Whether the goddis of folkis and of alle londis myyten delyuere her cuntrei fro myn hond?
14 Kodi ndi milungu iti mwa milungu ya mitundu ina ya anthuwo, imene makolo anga anayiwononga kotheratu, inatha kupulumutsa anthu ake mʼdzanja langa? Nanga tsono Mulungu wanuyo adzakupulumutsani mʼdzanja langa motani?
Who is of alle goddis of folkis, whiche my fadris distrieden, that myyte delyuere his puple fro myn hond, that also youre God may delyuere you fro this hond?
15 Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”
Therfor Ezechie disseyue not you, nether scorne bi veyn counselyng, nethir bileue ye to hym; for if no god of alle folkis and cuntreis myyte delyuere his puple fro myn hond, and fro the hond of my fadris, suyngli nether youre God schal mowe delyuere you fro this myn hond.
16 Atsogoleri a ankhondo a Senakeribu anapitiriza kuyankhula zotsutsana ndi Yehova Mulungu ndi mtumiki wake Hezekiya.
But also hise seruauntis spaken many othir thingis ayenus the Lord God, and ayens Ezechie, his seruaunte.
17 Mfumunso inalemba makalata onyoza Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo inanena zotsutsana naye izi: “Monga momwe milungu ya anthu a mayiko ena sinathe kuwapulumutsa kuchoka mʼdzanja langa, chonchonso Mulungu wa Hezekiya sadzapulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa.”
Also he wroot epistlis ful of blasfemye ayens the Lord God of Israel, and he spak ayens God, As the goddis of othere folkis myyten not delyuere her puple fro myn hond, so and the God of Ezechie may not delyuere his puple fro myn hond.
18 Kenaka iwo anafuwula mu Chihebri kwa anthu a mu Yerusalemu amene anali pa khoma, kuwaopseza ndi kuwachititsa mantha ndi cholinga choti alande mzindawo.
Ferthermore and with greet cry in the langage of Jewis he sownede ayens the puple, that sat on the wallis of Jerusalem, to make hem aferd, and to take the citee.
19 Iwo anayankhula za Mulungu wa Yerusalemu monga anayankhulira za milungu ya anthu ena a pa dziko lapansi, ntchito ya manja a anthu.
And he spake ayens God of Israel, as ayens the goddis of the puplis of erthe, the werkis of mennus hondis.
20 Mfumu Hezekiya ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi anafuwulira kumwamba mʼpemphero chifukwa cha zimenezi.
Therfor Ezechie, the kyng, and Ysaie, the profete, the sone of Amos, preieden ayens this blasfemye, and crieden til in to heuene.
21 Ndipo Yehova anatumiza mngelo amene anadzapha anthu onse odziwa nkhondo ndi atsogoleri ndiponso oyangʼanira misasa ya mfumu ya ku Asiriya. Choncho Senakeribu anabwerera kwawo wamanyazi. Ndipo atalowa mʼnyumba ya mulungu wake, ena mwa ana ake anamupha ndi lupanga.
And the Lord sente his aungel, that killide ech strong man and werriour, and the prince of the oost of the kyng of Assiriens; and he turnede ayen with schenship `in to his lond. And whanne he hadde entrid in to the hows of his god, the sones, that yeden out of his wombe, killiden hym with swerd.
22 Kotero Yehova anapulumutsa Hezekiya ndi anthu a ku Yerusalemu kuchoka mʼdzanja la Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi mʼdzanja la anthu ena. Yehova anawateteza ku mbali zonse.
And the Lord sauyde Ezechie, and the dwelleris of Jerusalem, fro the hond of Senacherib, kyng of Assiriens, and fro the hond of alle men; and yaf to hem reste bi cumpas.
23 Anthu ambiri anabweretsa zopereka kwa Yehova ku Yerusalemu ndi mphatso zamtengowapatali kwa Hezekiya mfumu ya Yuda. Kuyambira nthawi imeneyo Hezekiya ankalemekezedwa kwambiri ndi mitundu ina yonse.
Also many men brouyten offryngis and sacrifices to the Lord in to Jerusalem, and yiftis to Ezechie, kyng of Juda; which was enhaunsid aftir these thingis bifor alle folkis.
24 Pa nthawi imeneyo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Iye anapemphera kwa Yehova, amene anamuyankha ndi kumupatsa chizindikiro chodabwitsa.
In tho daies Ezechie was sijk `til to the deth, and he preiede the Lord; and he herde hym, and yaf to hym a signe;
25 Koma Hezekiya anali ndi mtima wonyada ndipo sanachite molingana ndi kukoma mtima kumene Mulungu anamuonetsera. Choncho mkwiyo wa Yehova unali pa iye ndi pa Yuda ndi Yerusalemu.
but he yeldide not bi the benefices whiche he hadde take, for his herte was reisid; and ire was maad ayens hym, and ayens Juda, and ayens Jerusalem.
26 Koma kenaka Hezekiya analapa za kunyada kwakeko, monga anachitanso anthu a mu Yerusalemu. Choncho mkwiyo wa Yehova sunafike pa iwo pa nthawi ya Hezekiya.
And he was mekid aftirward, for his herte was reisid; bothe he was mekid, and the dwelleris of Jerusalem; and therfor the ire of the Lord cam not on hem in the daies of Ezechie.
27 Hezekiya anali ndi chuma ndi ulemu wambiri ndipo anamanga nyumba zosungiramo chuma cha siliva wake ndi golide ndi za miyala yokongola, zokometsera zakudya, zishango ndi mtundu uliwonse wa zinthu zamtengowapatali.
Forsothe Ezechie was riche, and ful noble, and gaderide to hym silf ful many tresours of siluer, of gold, and of preciouse stoon, of swete smellynge spices, and of armuris of al kynde, and of vessels of greet prijs.
28 Iye anamanganso nyumba zosungiramo tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta a olivi, ndiponso anamanga nyumba zodyeramo ngʼombe zosiyanasiyana, ndi makola a nkhosa.
Also he bildide large housis of wheete, of wyn, and of oile, and cratchis of alle beestis,
29 Iyeyo anamanga midzi ndipo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri, pakuti Mulungu anamupatsa chuma chambiri.
and fooldis to scheep, and sixe citees. For he hadde vnnoumbrable flockis of scheep and of grete beestis; for the Lord hadde youe to hym ful myche catel.
30 Ndi Hezekiya amene anatseka ku mtunda kwa kasupe wa Gihoni, ndi kumuwongolera kuti madzi ake apite mbali ya kumadzulo kwa Mzinda wa Davide. Iye ankachita bwino pa ntchito iliyonse imene ankagwira.
Thilke is Ezechie, that stoppide the hiyere welle of the watris of Gion, and turnede tho awei vndur the erthe at the west of the citee of Dauid; in alle hise werkis he dide `bi prosperite, what euer thing he wolde.
31 Koma pamene nthumwi zotumizidwa ndi atsogoleri a ku Babuloni zinabwera kudzamufunsa za chizindikiro chozizwitsa chimene chinachitika mʼdzikomo, Mulungu anamusiya yekha, kumuyesa kuti adziwe zonse zimene zinali mu mtima mwake.
Netheles in the message of the princes of Babiloyne, that weren sent to hym for to axe of the grete wondir, that bifelde on the lond, God forsook hym, that he were temptid, and that alle thingis weren knowun that weren in his herte.
32 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Hezekiya ndi ntchito za kudzipereka kwake zalembedwa mʼmasomphenya a Yesaya mwana wa Amozi, mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
Sotheli the residue of wordis of Ezechie, and of hise mercies, ben writun in the profesie of Ysaie, the profete, sone of Amos, and in the book of kyngis of Juda and of Israel.
33 Hezekiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pa phiri pamene pali manda a zidzukulu za Davide. Ayuda onse ndi anthu a mu Yerusalemu anamulemekeza atamwalira. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Ezechie slepte with hise fadris, and thei birieden hym aboue the sepulcris of the sones of Dauid. And al Juda and alle the dwelleris of Jerusalem maden solempne the seruyces of his biriyng; and Manasses, his sone, regnide for him.

< 2 Mbiri 32 >