< 2 Mbiri 29 >

1 Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya.
Jezekiji bješe dvadeset i pet godina kad poèe carovati, i carova dvadeset i devet godina u Jerusalimu. Materi mu bješe ime Avija, kæi Zaharijina.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.
I èinjaše što je pravo pred Gospodom sasvijem kako je èinio David otac njegov.
3 Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza.
Prve godine svojega carovanja, prvoga mjeseca, otvori vrata na domu Gospodnjem, i opravi ih.
4 Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa
I sazva sveštenike i Levite, i sabra ih na istoènu ulicu,
5 ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika.
I reèe im: èujte me, Leviti, osveštajte se sada i osvetite dom Gospoda Boga otaca svojih, i iznesite neèistotu iz svetinje.
6 Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira.
Jer sagriješiše oci naši i èiniše što je zlo pred Gospodom Bogom našim, i ostaviše ga; i odvratiše lice svoje od šatora Gospodnjega i okrenuše mu leða;
7 Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli.
I zatvoriše vrata od trijema, i pogasiše žiške, i kadom ne kadiše, niti žrtava paljenica prinosiše u svetinji Bogu Izrailjevu.
8 Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino.
Zato se razgnjevi Gospod na Judu i na Jerusalim, te ih dade da se potucaju, i da budu èudo i potsmijeh, kako vidite svojim oèima.
9 Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo.
Jer eto padoše oci naši od maèa, i sinovi naši i kæeri naše i žene naše zarobiše se zato.
10 Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere.
Sada dakle naumio sam zadati vjeru Gospodu Bogu Izrailjevu, da bi se odvratila od nas žestina gnjeva njegova.
11 Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”
Sinovi moji, ne oklijevajte više, jer je vas izabrao Gospod da stojite pred njim i služite mu, i da mu budete sluge i da mu kadite.
12 Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito: Kuchokera ku banja la Kohati, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya; kuchokera ku banja la Merari, Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; kuchokera ku banja la Geresoni, Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;
Tada ustaše Leviti Mat sin Amasajev i Joilo sin Azarijin od sinova Katovijeh; a od sinova Merarijevih Kis sin Avdijev i Azarija sin Jaleleilov; i od sinova Girsonovijeh Joah sin Zimin i Eden sin Joahov;
13 kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani, Simiri ndi Yeiyeli; kuchokera kwa zidzukulu za Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
I od sinova Elisafanovijeh Simrije i Jeilo, i od sinova Asafovijeh Zaharija i Matanija;
14 kuchokera kwa zidzukulu za Hemani, Yehieli ndi Simei; kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni, Semaya ndi Uzieli.
I od sinova Amonovijeh Jeilo i Simej, i od sinova Jedutunovijeh Semaja i Ozilo;
15 Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova.
I skupiše braæu svoju, i osveštavši se doðoše, kako bješe zapovjedio car po rijeèi Gospodnjoj, da oèiste dom Gospodnji.
16 Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni.
I ušavši sveštenici u dom Gospodnji da ga oèiste, iznosiše svu neèistotu što naðoše u crkvi Gospodnjoj u trijem doma Gospodnjega; a Leviti kupiše i iznosiše napolje na potok Kedron.
17 Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.
A poèeše osveæivati prvoga dana prvoga mjeseca; a osmoga dana toga mjeseca uðoše u trijem Gospodnji, i osveæivaše dom Gospodnji osam dana, i šesnaestoga dana prvoga mjeseca svršiše.
18 Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse.
Potom doðoše k caru Jezekiji i rekoše: oèistismo sav dom Gospodnji i oltar za žrtve paljenice i sve sudove njegove i sto za postavljanje i sve sudove njegove,
19 Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”
I sve sudove koje bješe bacio car Ahaz dokle carovaše griješeæi, i spremismo i osvetismo, i eno ih pred oltarom Gospodnjim.
20 Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova.
Potom car Jezekija usta rano, i sazva upravitelje gradske, i otide u dom Gospodnji.
21 Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova.
I dovede sedam junaca i sedam ovnova i sedam jaganjaca i sedam jaraca za grijeh, za carstvo i za svetinju i za Judu; i reèe sinovima Aronovijem sveštenicima da prinesu na oltaru Gospodnjem.
22 Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe.
Tada zaklaše goveda, i sveštenici uzevši krv njihovu pokropiše oltar; zaklaše i ovnove, i krvlju njihovom pokropiše oltar; i zaklaše jaganjce i krvlju njihovom pokropiše oltar.
23 Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo.
Potom dovedoše jarce za grijeh pred cara i pred zbor, i oni metnuše ruke svoje na njih.
24 Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.
I zaklaše ih sveštenici, i oèistiše krvlju njihovom oltar na oèišæenje svemu Izrailju, jer car zapovjedi da se za sav narod Izrailjev prinese žrtva paljenica i žrtva za grijeh.
25 Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri.
I postavi Levite u domu Gospodnjem s kimvalima i psaltirima i guslama, kako bješe zapovjedio David i Gad vidjelac carev i Natan prorok; jer od Gospoda bješe zapovijest preko proroka njegovijeh.
26 Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.
I tako stajahu Leviti sa spravama Davidovijem a sveštenici s trubama.
27 Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli.
Tada zapovjedi Jezekija da prinesu žrtvu paljenicu na oltaru. I kad se poèe žrtva paljenica, poèe se pjesma Gospodnja uz trube i sprave Davida cara Izrailjeva.
28 Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.
I sav se zbor klanjaše, i pjevaèi pjevahu i trubaèi trubljahu, i to sve dokle se ne svrši žrtva paljenica.
29 Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira.
A kad svršiše žrtvu, car i svi koji bijahu s njim padoše i pokloniše se.
30 Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.
Potom reèe car i knezovi Levitima da hvale Gospoda rijeèima Davidovijem i Asafa vidioca; i hvališe s velikim veseljem, i savivši se pokloniše se.
31 Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.
Tada Jezekija progovori i reèe: sada posvetiste ruke svoje Gospodu, pristupite i donesite prinose i žrtve zahvalne u dom Gospodnji. I donese sav zbor prinose i žrtve zahvalne, i ko god bješe voljna srca žrtve paljenice.
32 Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova.
I na broj bješe žrtava paljenica što donese zbor, sedamdeset volova, sto ovnova, dvjesta jaganjaca, sve za žrtvu paljenicu Gospodu;
33 Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000.
A drugih stvari posveæenijeh bješe šest stotina volova i tri tisuæe ovaca.
34 Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe.
Ali malo bijaše sveštenika, te ne mogahu drijeti svijeh žrtava paljenica; zato im pomagahu braæa njihova Leviti, dokle se ne svrši posao i dokle se ne osveštaše drugi sveštenici; jer Leviti bijahu radiji osveštati se nego sveštenici.
35 Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza. Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso.
I bijaše vrlo mnogo žrtava paljenica s pretilinom od žrtava zahvalnijeh i naljeva na žrtve paljenice. Tako bi povraæena služba u domu Gospodnjem.
36 Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.
I radovaše se Jezekija i sav narod, što Bog upravi narod, jer ovo bi naglo.

< 2 Mbiri 29 >