< 2 Mbiri 29 >

1 Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya.
Hezekiah began to reign when he was twenty-five years old; he reigned twenty-nine years in Jerusalem. His mother's name was Abijah; she was the daughter of Zechariah.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.
He did what was right in the eyes of Yahweh, just as David his father had done.
3 Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza.
In the first year of his reign, in the first month, Hezekiah opened the doors of the house of Yahweh and repaired them.
4 Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa
He brought in the priests and the Levites, and gathered them together into the courtyard on the east side.
5 ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika.
He said to them, “Listen to me, you Levites! Consecrate yourselves, and consecrate the house of Yahweh, the God of your ancestors, and carry away the filthiness from the holy place.
6 Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira.
For our ancestors trespassed and did what was evil in the sight of Yahweh our God; they forsook him, turned away their faces from the place where Yahweh lives, and turned their backs on it.
7 Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli.
Also they shut up the doors of the porch and put out the lamps; they did not burn incense or offer burnt offerings in the holy place to the God of Israel.
8 Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino.
Therefore the wrath of Yahweh had fallen on Judah and Jerusalem, and he has made them to be an object of terror, of horror, and of scorn, as you can see with your own eyes.
9 Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo.
This is why our fathers have fallen by the sword, and our sons, our daughters, and our wives are in captivity for this.
10 Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere.
Now it is in my heart to make a covenant with Yahweh, the God of Israel, so that his fierce anger may turn away from us.
11 Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”
My sons, do not be lazy now, for Yahweh has chosen you to stand before him, to worship him, and that you should be his servants and burn incense.”
12 Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito: Kuchokera ku banja la Kohati, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya; kuchokera ku banja la Merari, Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; kuchokera ku banja la Geresoni, Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;
Then the Levites arose: Mahath son of Amasai, and Joel son of Azariah, of the people of the Kohathites; and of the people of Merari, Kish son of Abdi, and Azariah son of Jehallelel; and of the Gershonites, Joah son of Zimmah, and Eden son of Joah;
13 kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani, Simiri ndi Yeiyeli; kuchokera kwa zidzukulu za Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
of the sons of Elizaphan, Shimri and Jeuel; and of the sons of Asaph, Zechariah and Mattaniah;
14 kuchokera kwa zidzukulu za Hemani, Yehieli ndi Simei; kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni, Semaya ndi Uzieli.
of the sons of Heman, Jehuel and Shimei; and of the sons of Jeduthun, Shemaiah and Uzziel.
15 Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova.
They gathered their brothers, they consecrated themselves, and they went in, as the king commanded, following the words of Yahweh, to cleanse the house of Yahweh.
16 Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni.
The priests went in to the inner part of the house of Yahweh to cleanse it; they brought out all the filth that they found in the temple of Yahweh into the courtyard of the house. The Levites took it to carry it out to the brook Kidron.
17 Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.
Now they began the consecration on the first day of the first month. By the eighth day of the month they reached the porch of Yahweh. Then for eight more days they consecrated the house of Yahweh. On the sixteenth day of the first month they finished.
18 Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse.
Then they went to Hezekiah, the king, inside the palace and said, “We have cleansed all the house of Yahweh, the altar for burnt offerings with all its implements, and the table of the bread of the presence, with all its implements.
19 Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”
So we have prepared and we have consecrated all the items that King Ahaz removed when he acted unfaithfully during his reign. See, they are in front of the altar of Yahweh.”
20 Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova.
Then Hezekiah the king rose early in the morning and gathered the leaders of the city; he went up to the house of Yahweh.
21 Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova.
They brought seven bulls, seven rams, seven lambs, and seven male goats as a sin offering for the kingdom, for the sanctuary, and for Judah. He commanded the priests, the sons of Aaron, to offer them on the altar of Yahweh.
22 Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe.
So they killed the bulls, and the priests received the blood and sprinkled it on the altar. Then they killed the rams and sprinkled their blood on the altar; and they also killed the lambs and sprinkled their blood on the altar.
23 Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo.
They brought the male goats for the sin offering before the king and the assembly; they laid their hands on them.
24 Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.
The priests killed them, and they made a sin offering with their blood on the altar to make atonement for all Israel, for the king had commanded that a burnt offering and a sin offering should be made for all Israel.
25 Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri.
Hezekiah placed the Levites in the house of Yahweh with cymbals, harps, and lyres, arranging them by the command of David, Gad, the king's seer, and Nathan, the prophet, for the command was from Yahweh by means of his prophets.
26 Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.
The Levites stood with the instruments of David, and the priests with the trumpets.
27 Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli.
Hezekiah commanded them to offer the burnt offering on the altar. When the burnt offering began, the song of Yahweh began also, with the trumpets, together with the instruments of David, king of Israel.
28 Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.
All the assembly worshiped, the singers sang, and the trumpeters played; all this continued until the burnt offering was finished.
29 Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira.
When they had finished the offerings, the king and all who were present with him bowed and worshiped.
30 Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.
Moreover, Hezekiah, the king, and the leaders commanded the Levites to sing praises to Yahweh with the words of David and of Asaph, the seer. They sang praises with gladness, and they bowed down and worshiped.
31 Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.
Then Hezekiah said, “Now you have consecrated yourselves to Yahweh. Come here and bring sacrifices and thank offerings into the house of Yahweh.” The assembly brought sacrifices and thank offerings, and all who had a willing heart brought burnt offerings.
32 Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova.
The number of the burnt offerings that the assembly brought was seventy bulls, one hundred rams, and two hundred male lambs. All these were for a burnt offering to Yahweh.
33 Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000.
The consecrated offerings were six hundred oxen and three thousand sheep.
34 Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe.
But the priests were too few to skin all the burnt offerings, so their brothers, the Levites, helped them until the work was done, and until the priests could consecrate themselves, for the Levites had been more careful to consecrate themselves than the priests.
35 Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza. Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso.
In addition, there were very many burnt offerings; they were performed with the fat of the fellowship offerings, and there were drink offerings for every burnt offering. So the service of the house of Yahweh was set in order.
36 Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.
Hezekiah rejoiced, and all the people also, because of what God had prepared for the people, for the work had been done quickly.

< 2 Mbiri 29 >