< 2 Mbiri 26 >

1 Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
Tada sav narod Judin uze Oziju, kome bijaše šesnaest godina, i zacariše ga na mjesto oca njegova Amasije.
2 Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
On sazida Elot povrativ ga Judi pošto car poèinu kod otaca svojih.
3 Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
Oziji bijaše šesnaest godina kad se zacari, i carova pedeset i dvije godine u Jerusalimu. Materi mu bijaše ime Jeholija iz Jerusalima.
4 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
On èinjaše što je pravo pred Gospodom sasvijem kako je èinio Amasija otac njegov.
5 Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
I tražaše Boga dokle živ bijaše Zaharija koji razumijevaše utvare Božije; i dokle god tražaše Gospoda, davaše mu sreæu Bog.
6 Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
Jer izašav vojevaše s Filistejima, i obori zidove Gatu i zidove Javni i zidove Azotu; i sazida gradove u zemlji Azotskoj i po Filistejima.
7 Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
I Bog mu pomože protiv Filisteja i protiv Arapa, koji življahu u Gurvalu, i protiv Maonaca.
8 Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
I Amonci davahu dare Oziji, i raznese se ime njegovo do Misira, jer osili veoma.
9 Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
I sazida Ozija kule u Jerusalimu na vratima na uglu, i na vratima u dolu, i na uglu, i utvrdi ih.
10 Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
Sazida i u pustinji kule, i iskopa mnogo studenaca, jer imaše mnogo stoke i u dolinama i u ravnicama, i ratara i vinogradara po brdima i na Karmilu, jer mu mila bješe poljska radnja.
11 Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
I imaše Ozija ubojitu vojsku, koja iðaše u rat u èetama brojem, kako ih izbroji Jeilo pisar i Masija upravitelj, pod upravom Ananije vojvode careva.
12 Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
Svega na broj bijaše glavara domova otaèkih hrabrijeh junaka dvije tisuæe i šest stotina,
13 Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
A pod njihovom rukom vojske tri stotine i sedam tisuæa i pet stotina hrabrijeh vojnika, da pomažu caru protiv neprijatelja.
14 Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
I naèini Ozija svoj vojsci štitove i koplja i šljemove i oklope i lukove i kamenje za praæe.
15 Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
I naèini u Jerusalimu bojne sprave vrlo vješto izmišljene da stoje na kulama i na uglovima da meæu strijele i veliko kamenje; i raznese se ime njegovo daleko, jer mu se divno pomagaše dokle osili.
16 Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
Ali kad osili, ponese se srce njegovo, te se pokvari, i sagriješi Gospodu Bogu svojemu, jer uðe u crkvu Gospodnju da kadi na oltaru kadionom;
17 Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
A za njim uðe Azarija sveštenik i s njim osamdeset sveštenika Gospodnjih hrabrijeh ljudi;
18 Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
I opriješe se caru Oziji govoreæi: nije tvoje, Ozija, kaditi Gospodu, nego sveštenika sinova Aronovijeh koji su posveæeni da kade; izidi iz svetinje, jer si zgriješio, i neæe ti biti na èast pred Gospodom Bogom.
19 Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
Tada se razgnjevi Ozija držeæi u ruci kadionicu da kadi; i kad se gnjevljaše na sveštenike, izide mu guba na èelu pred svijem sveštenicima u domu Gospodnjem kod oltara kadionoga.
20 Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
I pogleda ga Azarija poglavar sveštenièki i svi sveštenici, a on gubav na èelu; i brže ga izvedoše napolje, a i sam pohitje da izide, jer ga Gospod udari.
21 Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
I osta car Ozija gubav do smrti svoje, i sjeðaše u odvojenom domu gubav, jer bi odluèen od doma Gospodnjega; a Jotam sin njegov upravljaše domom carevijem i suðaše narodu u zemlji.
22 Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
A ostala djela Ozijina prva i pošljednja napisao je prorok Isaija sin Amosov.
23 Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I poèinu Ozija kod otaca svojih, i pogreboše ga kod otaca njegovijeh u grobnom polju carskom, jer rekoše: gubav je. I zacari se na njegovo mjesto Jotam sin njegov.

< 2 Mbiri 26 >