< 2 Mbiri 25 >

1 Amaziya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
Forsothe Amasie, `his sone, regnede for hym; Amasie was of fyue and twenti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnyde nyne and twenti yeer in Jerusalem; the name of his modir was Joiaden, of Jerusalem.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osati ndi mtima wonse.
And he dide good in the siyt of the Lord, netheles not in perfit herte.
3 Pamene mphamvu zonse zaufumu zinali mʼmanja mwake, iye anapha akuluakulu amene anapha abambo ake, mfumu ija.
And whanne he siy the empire strengthid to hym silf, he stranglide the seruauntis, that killiden the kyng, his fadir;
4 Komabe iye sanaphe ana awo koma anatsatira zolembedwa mʼbuku la Mose, mʼmene Yehova analamula kuti, “Makolo sadzaphedwa chifukwa cha ana awo kapena ana kuphedwa chifukwa cha makolo awo. Aliyense adzafera machimo ake.”
but he killide not the sones of hem; as it is writun in the book of the lawe of Moises, where the Lord comaundide, seiynge, Fadris schulen not be slayn for the sones, nether the sones for her fadris; but ech man schal die in his owne synne.
5 Amaziya anasonkhanitsa anthu a ku Yuda ndipo anawapatsa zochita molingana ndi mabanja awo kukhala anthu olamulira 1,000, ndi olamulira 100 pa Ayuda onse ndi Benjamini. Ndipo iye anawerenga amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo napeza kuti analipo amuna 300,000 okonzeka kugwira ntchito ya usilikali, okhoza kugwiritsa ntchito mkondo ndi chishango.
Therfor Amasie gaderide togidere Juda, and ordeynede hem bi meynees and tribunes and centuriouns, in al Juda and Beniamyn; and he noumbride fro twenti yeer and aboue, and he foonde thritti thousynde of yonge men, that yeden out to batel, and helden spere and scheeld.
6 Iye analembanso ntchito anthu odziwa nkhondo 100,000 ochokera ku Israeli pa mtengo wa makilogalamu 3,400 a siliva.
Also for mede he hiride of Israel an hundrid thousynde of stronge men, for an hundrid talentis of siluer, that thei schulden fiyte ayens the sones of Edom.
7 Koma munthu wa Mulungu anabwera kwa iye ndipo anati, “Inu mfumu, asilikali awa ochokera ku Israeli asapite ndi inu, pakuti Yehova sali ndi Israeli kapena ndi aliyense wa anthu a Efereimu.
Forsothe a man of God cam to hym, and seide, A! kyng, the oost of Israel go not out with thee, for the Lord is not with Israel and with alle the sones of Effraym;
8 Ngakhale mupite ndi kuchita nkhondo molimba mtima, Mulungu adzakugonjetsani pamaso pa adani anu, pakuti Mulungu ali ndi mphamvu yothandiza kapena kugonjetsa.”
for if thou gessist that batels stonden in the myyt of oost, the Lord schal make thee to be ouercomun of enemyes, for it is of God for to helpe, and to turne in to fliyt.
9 Amaziya anafunsa munthu wa Mulungu kuti, “Koma nanga za makilogalamu aja a siliva amene ndapereka kwa asilikali a Israeli?” Munthu wa Mulungu anayankha kuti, “Yehova atha kukupatsani zambiri kuposa zimenezo.”
And Amasie seide to the man of God, What therfor schal be doon of the hundrid talentis, which Y yaf to the knyytis of Israel? And the man of God answeride to hym, The Lord hath, wherof he may yelde to thee myche mo thingis than these.
10 Choncho Amaziya anachotsa asilikali amene anabwera kwa iye kuchokera ku Efereimu ndipo anawatumiza kwawo. Iwo anakwiyira anthu a ku Yuda ndipo anapita kwawo atapsa mtima kwambiri.
Therfor Amasie departide the oost that cam to hym fro Effraym, that it schulde turne ayen in to his place; and thei weren wrooth greetli ayens Juda, and turneden ayen in to her cuntrei.
11 Ndipo Amaziya analimba mtima ndipo anatsogolera gulu lake lankhondo ku Chigwa cha Mchere, kumene anapha anthu 10,000 a ku Seiri.
Forsothe Amasie ledde out tristili his puple, and yede in to the valei of makyngis of salt, and he killide of the sones of Seir ten thousynde.
12 Gulu la ankhondo la Yuda linagwiranso anthu amoyo 10,000, napita nawo pamwamba pa thanthwe ndipo anawaponya pansi kotero kuti onse ananyenyeka.
And the sones of Juda token othere ten thousynde of men, and brouyten to the hiy scarre of summe stoon; and castiden hem doun fro the hiyeste in to the pit; whiche alle braken.
13 Pa nthawi imeneyi asilikali amene Amaziya anawabweza ndipo sanawalole kuti achite nawo nkhondo, anakathira nkhondo mizinda ya Yuda kuyambira ku Samariya mpaka ku Beti-Horoni. Iwo anapha anthu 3,000 ndipo anafunkha katundu wambiri.
And thilke oost whom Amasie hadde sent ayen, that it schulde not go with him to batel, was spred abrood in the citees of Juda fro Samarie `til to Betheron; and aftir `that it hadde slayn thre thousynde, it took awey a greet preie.
14 Amaziya atabwerera kuja anakapha Aedomu, anabweretsa milungu ya anthu a ku Seiri. Ndipo anayika kuti ikhale milungu yake, ankayipembedza ndi kupereka nsembe zopsereza.
And Amasie, after the sleyng of Idumeis, and after that he hadde brouyt the goddis of the sones of Seir, ordeynede hem `in to goddis to hym silf, and worschipide hem, and brente encense to hem.
15 Yehova anakwiyira Amaziya, ndipo anamutumizira mneneri amene anati, “Nʼchifukwa chiyani mukupembedza milungu ya anthu awa, imene sinathe kupulumutsa anthu ake mʼdzanja lanu?”
Wherfor the Lord was wrooth ayens Amasie, and sente to hym a profete, that seide to hym, Whi worschipist thou goddis that `delyueriden not her puple fro thin hond?
16 Iye ali kuyankhula, mfumu inati, “Kodi ife takusankha iwe kuti ukhale mlangizi wa mfumu? Khala chete! Ufuna kuphedweranji?” Choncho mneneriyo analeka koma anati, “Ine ndikudziwa kuti Mulungu watsimikiza kukuwonongani chifukwa mwachita izi ndipo simunamvere uphungu wanga.”
Whanne the profete spak these thingis, Amasie answeride to hym, Whether thou art a counselour of the king? ceesse thou, lest perauenture Y sle thee. Therfor the profete yede awei, and seide, Y woot, that the Lord thouyte to sle thee; for thou didist this yuel, and ferthermore thou assentidist not to my counsel.
17 Amaziya mfumu ya ku Yuda, atafunsa alangizi ake, anatumiza mawu awa kwa Yowasi mwana wa Yehowahazi mwana wa Yehu, mfumu ya Israeli: “Bwera udzakumane nane maso ndi maso.”
Therfor Amasie, the king of Juda, whanne he hadde take a ful yuel counsel, sente to the kyng of Israel Joas, the sone of Joachaz, the sone of Hieu, and seide, Come thou, se we vs togidere.
18 Koma Yowasi mfumu ya Israeli inayankha Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Nthawi ina kamtengo kaminga ka ku Lebanoni kanatumiza mawu kwa mkungudza wa ku Lebanoni kuti, ‘Pereka mwana wako wamkazi kwa mwana wanga kuti amukwatire!’ Koma chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa minga uja.
And he sente ayen messangeris, and seide, A `cardue, ether a tasil, which is in the Liban sente to the cedre of the Liban, and seide, Yyue thi douyter a wijf to my sone; and lo! beestis that weren in the wode of the Liban yeden and defouliden the cardue.
19 Iwe ukuti wagonjetsa Edomu, ndipo tsopano ukudzikuza ndi kudzitamandira, koma khala kwanu komweko! Nʼchifukwa chiyani ukufuna mavuto ndi kudzichititsa kuti ugwe pamodzinso ndi Yuda?”
Thou seidist, Y haue smyte Edom, and therfor thin herte is reysid in to pride; sitte thou in thin hows; whi stirist thou yuel ayens thee, that thou falle, and Juda with thee?
20 Komabe Amaziya sanamvere pakuti ndi Mulungu amene anakonzeratu kuti awapereke kwa Yehowasi, chifukwa iwo amapembedza milungu ya ku Edomu.
Amasie nolde here, for it was the wille of the Lord, that he schulde be bitakun in to the hondis of enemyes, for the goddis of Edom.
21 Kotero Yowasi mfumu ya Israeli inakamuthira nkhondo. Iye ndi Amaziya anayangʼanana maso ndi maso ku Beti-Semesi ku Yuda.
Therfor Joas, kyng of Israel, stiede, and thei siyen hem silf togidere. Sotheli Amasie, the kyng of Juda, was in Bethsames of Juda;
22 Yuda anagonjetsedwa ndi Israeli ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
and Juda felde doun bifor Israel, and fledde in to his tabernaclis.
23 Yehowahazi mfumu ya Israeli inagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Yehowasi anabwera naye ku Yerusalemu ndipo anagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira pa Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, khoma lotalika mamita 180.
Certis the kyng of Israel took in Bethsames Amasie, the kyng of Juda, the sone of Joas, sone of Joachaz, and brouyte in to Jerusalem; and he destriede the wallis therof fro the yate of Effraym `til to the yate of the corner, bi foure hundrid cubitis.
24 Iye anatenga golide ndi siliva yense ndi zida zonse zimene zimapezeka mʼNyumba ya Mulungu zimene ankazisamalira Obedi-Edomu, pamodzinso ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu ndipo anatenga anthu ngati chikole.
And be ledde ayen in to Samarie al the gold and siluer, and alle vessels whiche he foond in the hows of the Lord, and at Obededom, in the tresouris also of the kyngis hows, also and the sones of ostagis.
25 Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo kwa zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
Forsothe Amasie, kyng of Juda, the sone of Joas, lyuede fiftene yeer aftir that Joas, kyng of Israel, the sone of Joachaz, was deed.
26 Ntchito zina za mfumu Amaziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli?
Sotheli the residue of the formere and the laste wordis of Amasie ben writun in the book of kyngis of Juda and of Israel.
27 Kuyambira nthawi imene Amaziya analeka kutsatira Yehova anthu anamukonzera chiwembu mu Yerusalemu ndipo anathawira ku Lakisi, koma adaniwo anatumiza anthu ku Lakisiko ndipo anamupha komweko.
And aftir that he yede awei fro the Lord, thei settiden to hym tresouns in Jerusalem; and whanne he hadde fledde to Lachis, thei senten and killiden hym there;
28 Iwo anabwera naye ali pa kavalo ndipo anayikidwa mʼmanda ndi makolo ake mu mzinda wa Yuda.
and thei brouyten ayen on horsis, and birieden hym with his fadris in the citee of Dauid.

< 2 Mbiri 25 >