< 2 Mbiri 24 >

1 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
Joas var sju år gammal, då han Konung vardt, och regerade fyratio år i Jerusalem. Hans moder het Zibja af BerSeba.
2 Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
Och Joas gjorde det Herranom väl behagade, så länge Presten Jojada lefde.
3 Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
Och Jojada tog honom två hustrur, och han födde söner och döttrar.
4 Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
Derefter tog Joas till att förnya Herrans hus;
5 Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
Och församlade Prester och Leviter, och sade till dem: Farer ut till alla Juda städer, och församler penningar utaf hela Israel, till att förbättra edars Guds hus årliga, och skynder eder till att göra så; men Leviterna fördröjde dermed.
6 Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
Då kallade Konungen Jojada den yppersta, och sade till honom: Hvi hafver du icke akt på Leviterna, att de låta införa af Juda och Jerusalem den hjelpeskatten, som Mose Herrans tjenare påbudit hade, att samkas skulle i Israel, till vittnesbördsens tabernakel?
7 Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
Förty den ogudaktiga Athalia och hennes söner hafva förderfvat Guds hus; och allt det som till Herrans hus helgadt var, hafva de lagt till Baalim.
8 Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
Så befallde Konungen, att man skulle göra ena kisto; och de satte henne utantill vid dörrena af Herrans hus;
9 Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
Och lät utropa i Juda och Jerusalem, att man skulle införa Herranom den hjelpeskatten, som Guds tjenare Mose på Israel lagt hade i öknene.
10 Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
Då fröjdade sig alle öfverstar, och allt folket, och gjorde tillhopa, och lade i kistona, intilldess hon full vardt.
11 Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
Och då tid var att kistan skulle hafvas fram af Leviterna, efter Konungens befallning, då de sågo, att der många penningar uti voro, så kom Konungens skrifvare, och den som af öfversta Prestenom befallning hade, och tömde kistona, och båro henne i sitt rum igen. Så gjorde de hvar dag, tilldess de samkade en ganska stor hop penningar.
12 Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
Och Konungen och Jojada fingo det arbetarena, som skaffare voro på Herrans hus; de samme lejde stenhuggare och timbermän, till att förnya Herrans hus, desslikes de mästare på jern och koppar, till att bättra Herrans hus.
13 Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
Och arbetsmännerna arbetade, så att förbättringen på verket gick fram genom deras hand, och läto Guds hus komma sig till igen, och gjorde det fast.
14 Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
Och då de hade det lyktat, båro de penningarna, som öfver voro, in för Konungen och Jojada; deraf gjordes käril till Herrans hus, käril till tjensten, och till bränneoffer, skedar, och gyldene silfvertyg. Och de offrade bränneoffer vid Herrans hus framgent, så länge Jojada lefde.
15 Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
Och Jojada vardt gammal och mätt af ålder, och blef död, och var hundrade och tretio år gammal, då han blef död.
16 Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
Och de begrofvo honom uti Davids stad, ibland Konungarna, derföre att han hade gjort väl med Israel, och med Gud och hans hus.
17 Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
Efter Jojada död kommo de öfverste i Juda, och tillbådo Konungen; då hörde Konungen dem.
18 Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
Och de öfvergåfvo Herrans deras fäders Guds hus, och tjente lundom och afgudom; så kom vrede öfver Juda och Jerusalem för dessa deras brotts skull.
19 Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
Och han sände Propheter till dem, att de skulle omvända sig till Herran. Och de betygade dem; men de hörde dem intet.
20 Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
Och Guds Ande utiklädde Sacharia, Jojada Prestens son. Han steg fram för folket, och sade till dem: Detta säger Gud: Hvi öfverträden I Herrans bud, det eder icke väl bekommandes varder? Efter I hafven öfvergifvit Herran, så varder han ock öfvergifvandes eder.
21 Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
Men de gjorde ett förbund emot honom, och stenade honom, efter Konungens bud, i gårdenom för Herrans hus.
22 Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
Och Konung Joas tänkte intet på den barmhertighet, som Jojada hans fader med honom gjort hade, utan drap hans son; men då han blef död, sade han: Herren varder detta seendes och sökandes.
23 Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
Och då året var omgånget, drog upp de Syrers här, och kommo i Juda och Jerusalem, och förgjorde alla öfverstar i folkena; och allt deras rof sände de till Konungen i Damascon.
24 Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
Ty de Syrers magt kom med fögo folk, likväl gaf Herren i deras hand en ganska stor magt, derföre att de Herran deras fäders Gud öfvergifvit hade; desslikes lade de ock straff på Joas.
25 Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
Och då de drogo ifrå honom, läto de honom qvar i stora krankhet. Och hans tjenare gjorde ett förbund emot honom, för Prestens Jojada söners blods skull, och dråpo honom på hans säng, och han blef död; och man begrof honom uti Davids stad, dock icke ibland Konungagrifterna.
26 Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
De som förbundet gjorde emot honom voro desse: Sabad, Simeaths son, den Ammonitiskones, och Josabad, Simriths son, den Moabitiskones.
27 Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Men hans söner, och summan som under honom församlad var, och Guds hus byggning, si, de äro beskrifne uti Historien i Konungabokene. Och hans son Amazia vardt Konung i hans stad.

< 2 Mbiri 24 >