< 2 Mbiri 24 >

1 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
[was] a son of Seven years Joash when became king he and forty year[s] he reigned in Jerusalem and [the] name of mother his [was] Zibiah from Beer Sheba.
2 Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
And he did Joash the right in [the] eyes of Yahweh all [the] days of Jehoiada the priest.
3 Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
And he took for him Jehoiada wives two and he fathered sons and daughters.
4 Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
And it was after this it was with [the] heart of Joash to renew [the] house of Yahweh.
5 Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
And he assembled the priests and the Levites and he said to them go out to [the] cities of Judah and collect from all Israel money to repair - [the] house of God your as often as a year in a year and you you will do quickly the matter and not they acted quickly the Levites.
6 Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
And he summoned the king Jehoiada the chief and he said to him why? not have you required on the Levites to bring from Judah and from Jerusalem [the] tax of Moses [the] servant of Yahweh and of the assembly of Israel to [the] tent of the testimony.
7 Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
For Athaliah the wickedness sons her they had broken into [the] house of God and also all [the] holy things of [the] house of Yahweh they had used for the Baals.
8 Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
And he said the king and they made a chest one and they put it at [the] gate of [the] house of Yahweh [the] outside towards.
9 Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
And they made a proclamation in Judah and in Jerusalem to bring to Yahweh [the] tax of Moses [the] servant of God on Israel in the wilderness.
10 Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
And they were glad all the officials and all the people and they brought and they threw to the chest until finished.
11 Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
And it was at [the] time [when] someone brought the chest to [the] overseer of the king by [the] hand of the Levites and just as saw they that [was] much the money and he came [the] scribe of the king and [the] officer of [the] priest of the head so they may pour out the chest and they took it and they returned it to place its thus they did to a day - in a day and they gathered money to abundance.
12 Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
And he gave it the king and Jehoiada to [the] doer of [the] work of [the] service of [the] house of Yahweh and they were hiring stone cutters and craftsmen to renew [the] house of Yahweh and also craftsmen of iron and bronze to repair [the] house of Yahweh.
13 Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
And they worked [the] doers of the work and it went up [the] repair for the work by hand their and they erected [the] house of God on measurement its and they strengthened it.
14 Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
And just as had finished they they brought before the king and Jehoiada [the] remainder of the money and someone made it articles for [the] house of Yahweh articles of service and offering up and pans and articles of gold and silver and they were offering up burnt offerings in [the] house of Yahweh continually all [the] days of Jehoiada.
15 Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
And he became old Jehoiada and he was satisfied days and he died a son of one hundred and thirty year[s] at death his.
16 Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
And people buried him in [the] city of David with the kings for he had done good in Israel and with God and house his.
17 Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
And after [the] death of Jehoiada they came [the] leaders of Judah and they bowed down to the king then he listened the king to them.
18 Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
And they abandoned [the] house of Yahweh [the] God of ancestors their and they served the Asherah poles and the idols and it was wrath towards Judah and Jerusalem in guilt their this.
19 Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
And he sent among them prophets to bring back them to Yahweh and they warned them and not they gave ear.
20 Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
And [the] spirit of God it clothed Zechariah [the] son of Jehoiada the priest and he stood above the people and he said to them thus - he says God why? [are] you transgressing [the] commandments of Yahweh and not you will prosper for you have forsaken Yahweh and he has forsaken you.
21 Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
And they conspired on him and they stoned him stone[s] by [the] command of the king in [the] courtyard of [the] house of Yahweh.
22 Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
And not he remembered Joash the king the loyalty which he had done Jehoiada father his with him and he killed son his and when dying he he said may he see Yahweh and may he require.
23 Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
And it was - to [the] circuit of the year it came up on him [the] army of Aram and they came to Judah and Jerusalem and they destroyed all [the] leaders of the people from [the] people and all booty their they sent to [the] king of Damascus.
24 Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
For with smallness of men they came - [the] army of Aram and Yahweh he gave in hand their an army for multitude exceedingly for they had forsaken Yahweh [the] God of ancestors their and with Joash they did judgment.
25 Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
And when went they from him for they had left him (with sicknesses *Qk) great they conspired on him own servants his in [the] blood of [the] sons of Jehoiada the priest and they killed him on bed his and he died and they buried him in [the] city of David and not they buried him in [the] graves of the kings.
26 Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
And these [are] the [ones who] conspired on him Zabad [the] son of Shimeath the Ammonite [woman] and Jehozabad [the] son of Shimrith the Moabite [woman].
27 Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And sons his (it will be numerous of *QK) the oracle on him and [the] founding of [the] house of God there they [are] written on [the] record of [the] scroll of the kings and he became king Amaziah son his in place of him.

< 2 Mbiri 24 >