< 2 Mbiri 2 >

1 Solomoni anatsimikiza zoti amange Nyumba ya Dzina la Yehova ndi nyumba yake yaufumu.
A umíniv Šalomoun stavěti dům jménu Hospodinovu, a dům svůj královský,
2 Iye analemba ntchito anthu 70,000 onyamula katundu ndi anthu 80,000 okumba miyala ku mapiri ndiponso akapitawo 3,600 oyangʼanira anthuwo.
Odečtl Šalomoun sedmdesát tisíc nosičů a osmdesát tisíc těch, kteříž tesali na hoře, a úředníků nad nimi tři tisíce a šest set.
3 Solomoni anatumiza uthenga uwu kwa Hiramu mfumu ya ku Turo: “Munditumizire mitengo ya mkungudza monga munachitira ndi abambo anga pamene munawatumizira mitengo ya mkungudza yomangira nyumba yaufumu yokhalamo.
Poslal také Šalomoun k Chíramovi králi Tyrskému, řka: Jakž jsi se choval k Davidovi otci mému, posílaje mu dříví cedrové, aby sobě stavěl dům k bydlení, tak čiň i mně.
4 Tsono ine ndikufuna kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wanga ndi kuyipereka kwa Iye kuti tiziyikamo buledi wopatulika nthawi zonse ndiponso kuperekeramo nsembe zopsereza mmawa uliwonse ndi madzulo ndi pa masabata ndi pa masiku a chikondwerero cha mwezi watsopano ndiponso pa masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova Mulungu wathu, monga mwa malamulo a Aisraeli mpaka muyaya.
Nebo aj, já stavěti chci dům jménu Hospodina Boha svého, aby posvěcen byl jemu k tomu, aby se před ním kadilo vonnými věcmi, a k ustavičnému předkládání chlebů, i k zápalným obětem, ranním i večerním, ve dny sobotní a novoměsíčné, i na slavnosti Hospodina Boha našeho, což v Izraeli na věky trvati má.
5 “Nyumba ya Mulungu imene ndidzamange idzakhala yayikulu, chifukwa Mulungu wathu ndi wamkulu kuposa milungu ina yonse.
Dům pak, kterýž stavěti chci, veliký býti má; nebo Bůh náš větší jest nade všecky bohy.
6 Koma ndani angathe kumumangira Iye Nyumba, pakuti mlengalenga, ngakhale kumwamba kwenikweni sikungamukwane? Tsono ine ndine yani kuti ndimangire Iyeyo Nyumba, kupatula malo chabe opserezerapo nsembe pamaso pake?
Ač kdo jest, ješto by mohl dům jemu vystavěti, poněvadž ho nebe i nebesa nebes obsáhnouti nemohou? Ano i já kdo jsem, abych jemu dům vystavěti měl, než toliko k tomu, aby se kadilo před ním?
7 “Tsono tumizireni munthu waluso pa ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, nsalu yapepo ndi yofiira ndi yobiriwira ndiponso waluso losema, kuti adzagwire ntchito mu Yuda ndi Yerusalemu pamodzi ndi anthu aluso amene abambo anga Davide anandipatsa.
Protož nyní pošli mi muže umělého, kterýž by uměl dělati na zlatě, na stříbře, na mědi, na železe, i z zlatohlavu a z červce, a z postavce modrého, a kterýž by uměl řezati řezby s jinými umělými, kteříž jsou u mne v Judstvu a v Jeruzalémě, kteréž zjednal David otec můj.
8 “Munditumizirenso mitengo ya mkungudza, payini ndiponso matabwa a mʼbawa wa ku Lebanoni, pakuti ndikudziwa kuti anthu anu ali ndi luso locheka matabwa kumeneko. Antchito anga adzagwira ntchito pamodzi ndi antchito anu
Přes to pošli mi také dříví cedrového a jedlového, a algumim z Libánu; nebo vím, že služebníci tvoji umějí sekati dříví Libánské. A hle, služebníci moji budou s služebníky tvými,
9 kuti andipatse matabwa ambiri, chifukwa Nyumba imene ndikumanga iyenera kukhala yayikulu ndi yokongola.
Aby mi připravili dostatek dříví; nebo dům, kterýž já stavěti chci, veliký býti má a slavný.
10 Ine ndidzalipira antchito anu amene adzacheke matabwa matani 1,000 a tirigu wopunthapuntha, matani 2,000 a barele, malita 440,000 a vinyo, ndiponso malita 440,000 a mafuta a olivi.”
A aj, dám na dělníky, kteříž sekati mají dříví, pšenice semlené služebníkům tvým dvadcet tisíc měr, a dvadcet tisíc měr ječmene, a dvadcet tisíc lák vína, a dvadcet tisíc tun oleje.
11 Hiramu, mfumu ya ku Turo, anamuyankha Solomoni pomulembera kalata kuti, “Chifukwa Yehova amakonda anthu ake, wayika iwe kukhala mfumu yawo.”
I odpověděl Chíram král Tyrský psáním, kteréž poslal k Šalomounovi: Jistě, žeť miluje Hospodin lid svůj, protož tě ustanovil nad nimi za krále.
12 Ndipo Hiramu anawonjezera kunena kuti, “Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi! Iye wamupatsa Davide mwana wanzeru, wodzaza ndi luntha ndi wozindikira, amene adzamanga Nyumba ya Mulungu ndi kudzimangira yekha nyumba yaufumu.
Řekl dále Chíram: Požehnaný Hospodin Bůh Izraelský, kterýž učinil nebe i zemi, a kterýž dal králi Davidovi syna moudrého, umělého, rozumného a opatrného, aby vystavěl dům Hospodinu a dům svůj královský.
13 “Ine ndikukutumizira Hiramu Abi, munthu wa luso lalikulu,
Protož posílámť teď muže moudrého, umělého a opatrného, kterýž byl u Chírama otce mého,
14 amene amayi ake anali wochokera ku Dani ndipo abambo ake anali a ku Turo. Iye anaphunzitsidwa kugwira ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, miyala yokongola ndi matabwa, ndiponso nsalu zofewa zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Alinso ndi luso la zosemasema ndipo atha kupanga chilichonse chimene wapatsidwa. Iye adzagwira ntchito ndi amisiri anu ndi a mbuye wanga, Davide abambo anu.
Syna jedné ženy ze dcer Dan, otce pak měl Tyrského, kterýž umí dělati na zlatě, na stříbře, na mědi, železe, kamení a na dříví, i z šarlatu, z postavce modrého, z kmentu a z červce, tolikéž řezati všelijaké řezby, a vymysliti všelijaké dílo, kteréž dáno mu bude s moudrými tvými, a s moudrými pána mého Davida otce tvého.
15 “Tsono mbuye wanga tumizirani antchito anu tirigu ndi barele, mafuta a olivi ndi vinyo zimene mwalonjeza,
Pšenice však toliko a ječmene, oleje a vína, což řekl pán můj, nechť pošle služebníkům svým.
16 ndipo ife tidzadula mitengo yonse imene mukuyifuna kuchokera ku Lebanoni ndipo tidzayimanga pamodzi ndi kuyiyadamitsa pa madzi mpaka ku Yopa. Ndipo inu mudzatha kuyitenga mpaka ku Yerusalemu.”
My pak nasekáme dříví z Libánu, což ho koli bude potřebí tobě, a připlavíme je tobě v vořích po moři k Joppe, a ty dáš je voziti do Jeruzaléma.
17 Solomoni anawerenga alendo onse amene anali mu Israeli, potsatira chiwerengero chimene abambo ake Davide anachita ndipo panapezeka kuti analipo anthu 153,600.
A tak sečtl Šalomoun všecky cizozemce, kteříž byli v zemi Izraelské po sečtení tom, kterýmž sečtl je David otec jeho, a nalezeno jich sto a padesát tisíc, tři tisíce a šest set.
18 Iye anayika anthu 70,000 kuti akhale onyamula katundu ndi anthu 80,000 kuti akhale ophwanya miyala mʼmapiri, anthu 3,600 anawayika kukhala akapitawo oyangʼanira anthu pa ntchitoyo.
I vybral z nich sedmdesát tisíc nosičů, a osmdesát tisíc těch, kteříž sekali na hoře, tři pak tisíce a šest set úředníků, kteříž lid k dílu přídrželi.

< 2 Mbiri 2 >