< 2 Mbiri 14 >

1 Tsono Abiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Asa mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake ndipo pa masiku ake, dziko linakhala pa mtendere kwa zaka khumi.
A kad poèinu Avija kod otaca svojih i pogreboše ga u gradu Davidovu, zacari se na njegovo mjesto Asa sin njegov. Za njegova vremena poèinu zemlja deset godina.
2 Asa anachita zabwino ndi zolungama pamaso pa Yehova Mulungu wake.
I èinjaše Asa što je dobro i pravo pred Gospodom Bogom njegovijem.
3 Iye anachotsa maguwa achilendo ndi malo opembedzerapo mafano, anaphwanya zipilala za miyala yachipembedzo ndi kugwetsa mafano a Asera.
Jer obori oltare tuðe i visine, i izlomi likove njihove i isijeèe lugove njihove.
4 Asa analamula Yuda kuti afunefune Yehova Mulungu wa makolo awo ndi kumvera malamulo ndi zolamulira zake.
I zapovjedi sinovima Judinijem da traže Gospoda Boga otaca svojih i da izvršuju zakon i zapovijest njegovu.
5 Iye anachotsa malo opembedzera mafano ndi maguwa ofukizira lubani mu mzinda uliwonse wa mu Yuda, ndipo mu ufumu wake munali mtendere pa nthawi ya ulamuliro wake.
Obori po svijem gradovima Judinijem visine i sunèane likove, i poèinu carstvo za njegova vremena.
6 Asa anamanga mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda pakuti dziko linali pa mtendere. Panalibe amene anachita naye nkhondo mʼzaka zimenezo, pakuti Yehova anamupatsa mpumulo.
I sazida tvrde gradove u zemlji Judinoj, jer zemlja bijaše u miru, niti bješe rata s njim onijeh godina, jer mu Gospod dade mir.
7 Iye anati kwa Yuda “Tiyeni timange mizinda iyi ndipo timange makoma ndi nsanja, zitseko ndi zotchinga. Dzikoli likanali lathu chifukwa tafuna Yehova Mulungu wathu; tinamufuna Iye ndipo watipatsa mpumulo mbali zonse.” Kotero iwo anamanga ndi kukhala pa ulemerero.
I reèe Judi: da sazidamo ove gradove i da ih opašemo zidom i kulama i vratima i prijevornicama, dok je zemlja naša; jer tražismo Gospoda Boga svojega, tražismo ga i dade nam mir otsvuda. I tako zidaše, i biše sreæni.
8 Asa anali ndi ankhondo 300,000 ochokera ku Yuda, okhala ndi zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndiponso ankhondo 280,000 ochokera ku Benjamini, okhala ndi zishango ndi mauta. Onsewa anali ankhondo amphamvu ndi olimba mtima.
I imaše Asa vojske trista tisuæa od Jude sa štitovima i kopljima, a od Venijamina dvjesta i osamdeset tisuæa sa štitovima i lukovima. Svi bijahu hrabri vojnici.
9 Zera wa ku Kusi anapita kukamenyana nawo ali ndi gulu lalikulu kwambiri la asilikali ndi magaleta 300 ndipo anafika mpaka ku Maresa.
I izide na njih Zara Etiopljanin s tisuæu tisuæa vojske i s trista kola, i doðe do Marise.
10 Asa anapita kukakumana naye ndipo anakhala pa mizere yawo ya nkhondo mʼchigwa cha Zefata pafupi ndi Maresa.
I Asa izide preda nj; i uvrstaše se vojske u dolini Sefati kod Marise.
11 Kenaka Asa anafuwulira Yehova Mulungu wake ndipo anati “Yehova palibe wina wofanana nanu kuti angathandize anthu opanda mphamvu pakati pa amphamvu. Tithandizeni Inu Yehova Mulungu wathu pakuti ife timadalira Inu ndipo mʼdzina lanu ife tabwera kudzalimbana ndi gulu la ankhondo lalikulu kwambiri ngati ili. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu, musalole kuti munthu akupambaneni.”
I zavapi Asa ka Gospodu Bogu svojemu govoreæi: Gospode, tebi je ništa pomoæi množini ili nejakomu; pomozi nam, Gospode Bože naš, jer se u te uzdamo, i u tvoje ime doðosmo na ovo mnoštvo. Gospode, ti si Bog naš, ne daj da može što na te èovjek.
12 Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Ayuda. Akusi anathawa,
I razbi Gospod Etiopljane pred Asom i pred Judom, i pobjegoše Etiopljani.
13 ndipo Asa ndi ankhondo ake anawathamangitsa mpaka ku Gerari. Gulu lonse lalikulu lija la Akusi linaphedwa. Sanapezeke mmodzi wamoyo pakati pawo. Iwo anakanthidwa pamaso pa Yehova ndi asilikali ake. Anthu a ku Yuda anatenga katundu wambiri olanda ku nkhondo.
I tjera ih Asa i narod koji bijaše s njim dori do Gerara. I popadaše Etiopljani da ih nijedan ne osta živ, jer se satrše pred Gospodom i pred vojskom njegovom; i oni odnesoše plijen velik veoma.
14 Iwo anawononga midzi yonse yozungulira Gerari pakuti mantha aakulu wochokera kwa Yehova anagwera anthuwo. Analanda katundu wa midzi yonse, popeza kunali katundu wambiri kumeneko.
I pobiše sve gradove oko Gerara, jer doðe na njih strah Gospodnji, i oplijeniše sve one gradove, jer bijaše u njima mnogo plijena.
15 Anakathiranso nkhondo misasa ya anthu oweta ziweto ndipo anatenga nkhosa zambiri, mbuzi ndi ngamira. Atatero anabwerera ku Yerusalemu.
Pobiše i po stanovima pastirskim ljude, i odvedoše mnogo ovaca i kamila; i vratiše se u Jerusalim.

< 2 Mbiri 14 >