< 2 Mbiri 11 >

1 Rehobowamu atafika ku Yerusalemu anasonkhanitsa asilikali 180,000 a fuko la Yuda ndi Benjamini kuti akachite nkhondo ndi Israeli, kuti abwezeretse ufumu kwa Rehobowamu.
Forsothe Roboam cam in to Jerusalem, and clepide togidere al the hows of Juda and of Beniamyn, `til to nyne scoore thousynde of chosen men and werriouris, for to fiyte ayens Israel, and for to turne his rewme to hym.
2 Koma Yehova anayankhula ndi munthu wa Mulungu Semaya kuti,
And the word of the Lord was maad to Semeye, the man of God,
3 “Kawuze Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda ndi Aisraeli onse ali mu Yuda ndi Benjamini kuti,
and seide, Speke thou to Roboam, the sone of Salomon, kyng of Juda, and to al Israel, which is in Juda and Beniamyn; The Lord seith these thingis,
4 ‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu. Pitani kwanu, aliyense wa inu, pakuti izi ndikuchita ndine.’” Choncho anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera osapita kukamenyana ndi Yeroboamu.
Ye schulen not stie, nethir ye schulen fiyte ayens youre britheren; ech man turne ayen in to his hows, for this thing is doon bi my wille. And whanne thei hadden herd the word of the Lord, thei turneden ayen, and yeden not ayens kyng Jeroboam.
5 Rehobowamu amakhala mu Yerusalemu ndipo anamanga mizinda ya chitetezo iyi mu Yuda:
Forsothe Roboam dwellide in Jerusalem, and he bildide wallid citees in Juda;
6 Betelehemu, Etamu, Tekowa,
and bildide Bethleem, and Ethan, and Thecue, and Bethsur;
7 Beti Zuri, Soko, Adulamu,
and Sochot, and Odollam;
8 Gati, Maresa, Zifi,
also and Jeth, and Maresa, and Ziph;
9 Adoraimu, Lakisi, Azeka,
but also Huram, and Lachis, and Azecha;
10 Zora, Ayaloni ndi Hebroni. Iyi ndiye inali mizinda yotetezedwa ya Yuda ndi Benjamini.
and Saraa, and Hailon, and Ebron, that weren in Juda and Beniamyn, ful strong citees.
11 Iye anakhwimitsa chitetezo cha mizindayi ndipo anayikamo atsogoleri a ankhondo, pamodzi ndi chakudya, mafuta a olivi ndi vinyo.
And whanne he hadde closid tho with wallis, he settide `in tho citees princes, and bernes of metis, that is, of oile, and of wyn.
12 Mʼmizinda yonse anayikamo zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndipo anachititsa kuti mizindayo ikhale yamphamvu. Choncho iye amalamulira Yuda ndi Benjamini.
But also in ech citee he made placis of armuris of scheeldis, and speris, and he made tho strong with most diligence; and he regnyde on Juda and Beniamyn.
13 Ansembe ndi Alevi a mʼmadera onse a Israeli anakhala mbali ya Rehobowamu.
Sotheli the preestis and dekenes, that weren in al Israel, camen to hym fro alle her seetis,
14 Alevi anasiya malo awo owetera ziweto ndi katundu wawo, ndi kubwera ku Yuda ndi ku Yerusalemu chifukwa Yeroboamu ndi ana ake anawakana kukhala ansembe a Yehova.
and forsoken her subarbis and possessiouns, and thei passiden to Juda and to Jerusalem; for Jeroboam and hise aftir comeris hadden cast hem a wey, that thei schulden not be set in preesthod of the Lord;
15 Ndipo iye anasankha ansembe akeake a pa malo opatulika ndi a mafano a mbuzi ndi mwana wangʼombe amene anapanga.
which Jeroboam made to hym preestis of hiye places, and of feendis, and of caluys, which he hadde maad.
16 Anthu ochokera fuko lililonse la Israeli amene anatsimikiza mitima yawo kufunafuna Yehova Mulungu wa Israeli, ankapitabe ku Yerusalemu kukapereka nsembe kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
But also of alle the linagis of Israel, whiche euer yauen her herte to seke the Lord God of Israel, thei camen to Jerusalem for to offre her sacrifices bifor the Lord God of her fadris.
17 Iwo analimbikitsa ufumu wa Yuda, ndipo anathandiza Rehobowamu mwana wa Solomoni kwa zaka zitatu. Pa nthawi imeneyi iye amatsatira zochita za Davide ndi Solomoni.
And thei strengthiden the rewme of Juda, and strengthiden Roboam, the sone of Salomon, bi thre yeer; for thei yeden in the weies of Dauid, and of Salomon, oneli bi thre yeer.
18 Rehobowamu anakwatira Mahalati, amene abambo ake anali Yerimoti, mwana wa Davide, ndipo amayi ake anali Abihaili, mwana wa Eliabu, mwana wa Yese.
Forsothe Roboam weddide a wijf Malaoth, the douytir of Jerymuth, sone of Dauid, and Abiail, the douytir of Heliab, sone of Ysaye;
19 Mkaziyo anamubereka ana aamuna awa: Yeusi, Semariya ndi Zahamu.
and sche childide to hym sones, Yeus, and Somorie, and Zerei.
20 Kenaka anakwatira Maaka, mwana wamkazi wa Abisalomu, amene anamubereka Abiya, Atai, Ziza ndi Selomiti.
Also after this wijf he took Maacha, the douyter of Abissalon, and sche childide to hym Abia, and Thai, and Ziza, and Salomyth.
21 Rehobowamu ankamukonda Maaka mwana wa Abisalomu kuposa aliyense mwa akazi ake ndi azikazi. Iye anali ndi akazi 18, azikazi 60, ana aamuna 28 ndi ana aakazi 60.
Forsothe Roboam louyde Maacha, the douytir of Abissalon, aboue alle hise wyues and secundarie wyues. Forsothe he hadde weddid eiytene wyues, sotheli sixti secundarie wyues; and he gendride eiyte and twenti sones, and sixti douytris.
22 Rehobowamu anasankha Abiya mwana wa Maaka kuti akhale mtsogoleri pa abale ake, ndi cholinga choti adzakhale mfumu.
Sotheli he ordeynede Abia, the sone of Maacha, in the heed, duyk ouer alle hise britheren; for he thouyte to make Abia kyng,
23 Iye anachita mwanzeru, pomwaza ena mwa ana ake ku madera onse a Yuda ndi Benjamini, ndi ku mizinda yonse yotetezedwa. Iye anawapatsa zinthu zambiri ndiponso anawafunira akazi ambiri.
for he was wisere and myytiere ouer alle hise sones, and in alle the coostis of Juda and of Beniamyn, and in alle wallid citees; and he yaf to hem ful many metis, and he had many wyues.

< 2 Mbiri 11 >