< 2 Mbiri 11 >

1 Rehobowamu atafika ku Yerusalemu anasonkhanitsa asilikali 180,000 a fuko la Yuda ndi Benjamini kuti akachite nkhondo ndi Israeli, kuti abwezeretse ufumu kwa Rehobowamu.
And when Rehoboam was come to Jerusalem, he assembled the house of Judah and Benjamin, an hundred and fourscore thousand chosen men, which were warriors, to fight against Israel, to bring the kingdom again to Rehoboam.
2 Koma Yehova anayankhula ndi munthu wa Mulungu Semaya kuti,
But the word of the LORD came to Shemaiah the man of God, saying,
3 “Kawuze Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda ndi Aisraeli onse ali mu Yuda ndi Benjamini kuti,
Speak unto Rehoboam the son of Solomon, king of Judah, and to all Israel in Judah and Benjamin, saying,
4 ‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu. Pitani kwanu, aliyense wa inu, pakuti izi ndikuchita ndine.’” Choncho anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera osapita kukamenyana ndi Yeroboamu.
Thus saith the LORD, Ye shall not go up, nor fight against your brethren: return every man to his house; for this thing is of me. So they hearkened unto the words of the LORD, and returned from going against Jeroboam.
5 Rehobowamu amakhala mu Yerusalemu ndipo anamanga mizinda ya chitetezo iyi mu Yuda:
And Rehoboam dwelt in Jerusalem, and built cities for defence in Judah.
6 Betelehemu, Etamu, Tekowa,
He built even Beth-lehem, and Etam, and Tekoa,
7 Beti Zuri, Soko, Adulamu,
And Beth-zur, and Soco, and Adullam,
8 Gati, Maresa, Zifi,
and Gath, and Mareshah, and Ziph,
9 Adoraimu, Lakisi, Azeka,
and Adoraim, and Lachish, and Azekah,
10 Zora, Ayaloni ndi Hebroni. Iyi ndiye inali mizinda yotetezedwa ya Yuda ndi Benjamini.
and Zorah, and Aijalon, and Hebron, which are in Judah and in Benjamin, fenced cities.
11 Iye anakhwimitsa chitetezo cha mizindayi ndipo anayikamo atsogoleri a ankhondo, pamodzi ndi chakudya, mafuta a olivi ndi vinyo.
And he fortified the strong holds, and put captains in them, and store of victual, and oil and wine.
12 Mʼmizinda yonse anayikamo zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndipo anachititsa kuti mizindayo ikhale yamphamvu. Choncho iye amalamulira Yuda ndi Benjamini.
And in every several city [he put] shields and spears, and made them exceeding strong. And Judah and Benjamin belonged to him.
13 Ansembe ndi Alevi a mʼmadera onse a Israeli anakhala mbali ya Rehobowamu.
And the priests and the Levites that were in all Israel resorted to him out of all their border.
14 Alevi anasiya malo awo owetera ziweto ndi katundu wawo, ndi kubwera ku Yuda ndi ku Yerusalemu chifukwa Yeroboamu ndi ana ake anawakana kukhala ansembe a Yehova.
For the Levites left their suburbs and their possession, and came to Judah and Jerusalem: for Jeroboam and his sons cast them off, that they should not execute the priest’s office unto the LORD:
15 Ndipo iye anasankha ansembe akeake a pa malo opatulika ndi a mafano a mbuzi ndi mwana wangʼombe amene anapanga.
and he appointed him priests for the high places, and for the he-goats, and for the calves which he had made.
16 Anthu ochokera fuko lililonse la Israeli amene anatsimikiza mitima yawo kufunafuna Yehova Mulungu wa Israeli, ankapitabe ku Yerusalemu kukapereka nsembe kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
And after them, out of all the tribes of Israel, such as set their hearts to seek the LORD, the God of Israel, came to Jerusalem to sacrifice unto the LORD, the God of their fathers.
17 Iwo analimbikitsa ufumu wa Yuda, ndipo anathandiza Rehobowamu mwana wa Solomoni kwa zaka zitatu. Pa nthawi imeneyi iye amatsatira zochita za Davide ndi Solomoni.
So they strengthened the kingdom of Judah, and made Rehoboam the son of Solomon strong, three years: for they walked three years in the way of David and Solomon.
18 Rehobowamu anakwatira Mahalati, amene abambo ake anali Yerimoti, mwana wa Davide, ndipo amayi ake anali Abihaili, mwana wa Eliabu, mwana wa Yese.
And Rehoboam took him a wife; Mahalath the daughter of Jerimoth the son of David, [and of] Abihail the daughter of Eliab the son of Jesse;
19 Mkaziyo anamubereka ana aamuna awa: Yeusi, Semariya ndi Zahamu.
and she bare him sons; Jeush, and Shemariah, and Zaham.
20 Kenaka anakwatira Maaka, mwana wamkazi wa Abisalomu, amene anamubereka Abiya, Atai, Ziza ndi Selomiti.
And after her he took Maacah the daughter of Absalom; and she bare him Abijah, and Attai, and Ziza, and Shelomith.
21 Rehobowamu ankamukonda Maaka mwana wa Abisalomu kuposa aliyense mwa akazi ake ndi azikazi. Iye anali ndi akazi 18, azikazi 60, ana aamuna 28 ndi ana aakazi 60.
And Rehoboam loved Maacah the daughter of Absalom above all his wives and his concubines: (for he took eighteen wives, and threescore concubines, and begat twenty and eight sons and threescore daughters.)
22 Rehobowamu anasankha Abiya mwana wa Maaka kuti akhale mtsogoleri pa abale ake, ndi cholinga choti adzakhale mfumu.
And Rehoboam appointed Abijah the son of Maacah to be chief, [even] the prince among his brethren: for [he was minded] to make him king.
23 Iye anachita mwanzeru, pomwaza ena mwa ana ake ku madera onse a Yuda ndi Benjamini, ndi ku mizinda yonse yotetezedwa. Iye anawapatsa zinthu zambiri ndiponso anawafunira akazi ambiri.
And he dealt wisely, and dispersed of all his sons throughout all the lands of Judah and Benjamin, unto every fenced city: and he gave them victual in abundance. And he sought [for them] many wives.

< 2 Mbiri 11 >