< 2 Mbiri 1 >

1 Solomoni mwana wa Davide anakhazikika molimbika mu ufumu wake, pakuti Yehova Mulungu wake anali naye ndipo anamukweza kwambiri.
I Solomun sin Davidov utvrdi se u carstvu svom, i Gospod Bog njegov bješe s njim, i uzvisi ga veoma.
2 Tsono Solomoni anayankhula kwa Aisraeli onse, olamulira a anthu 1,000, olamulira a anthu 100, oweruza ndiponso kwa atsogoleri onse a Israeli ndi atsogoleri amabanja.
I Solomun reèe svemu Izrailju, tisuænicima i stotinicima i sudijama i svijem knezovima svega Izrailja, glavarima domova otaèkih,
3 Solomoni pamodzi ndi gulu lonse la anthu anapita ku malo ofunika kwambiri pachipembedzo ku Gibiyoni. Tenti ya msonkhano ya Mulungu inali kumeneko, imene Mose mtumiki wa Yehova anayipanga mʼchipululu muja.
Te otidoše, Solomun i sav zbor s njim, na visinu koja bijaše u Gavaonu; jer ondje bijaše šator od sastanka Božijega, koji naèini Mojsije sluga Gospodnji u pustinji.
4 Davide anabweretsa Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriyati Yearimu, ndi kulikhazika kumalo kumene analikonzera popeza analimangira tenti mu Yerusalemu.
A kovèeg Božji bješe prenio David iz Kirijat-Jarima na mjesto koje mu spremi David; jer mu razape šator u Jerusalimu.
5 Koma guwa lansembe lamkuwa limene Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri analipanga linali ku Gibiyoni kutsogolo kwa tenti ya Yehova. Kotero kuti Solomoni ndi gulu lonse anakapembedza kumeneko.
I oltar mjedeni koji naèini Veseleilo, sin Urija sina Orova, bijaše ondje pred šatorom Gospodnjim. I potraži ga Solomun i sav zbor.
6 Solomoni anapita pamene panali guwa lansembe lamkuwa pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano ndipo anapereka nsembe zopsereza 1,000.
I prinese Solomun ondje pred Gospodom na oltaru mjedenom, koji bijaše pred šatorom od sastanka, prinese na njemu tisuæu žrtava paljenica.
7 Usiku umenewo Mulungu anaonekera kwa Solomoni ndipo anati kwa iye, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
Onu noæ javi se Bog Solomunu i reèe mu: išti šta hoæeš da ti dam.
8 Solomoni anayankha Mulungu kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwakukulu kwa Davide abambo anga ndipo mwayika ine kukhala mfumu mʼmalo mwake.
A Solomun reèe Bogu: ti si uèinio veliku milost Davidu ocu mojemu i postavio si mene carem na njegovo mjesto.
9 Tsopano Inu Yehova Mulungu, lolani kuti lonjezo lanu kwa abambo anga Davide likwaniritsidwe, pakuti mwandiyika kukhala mfumu ya anthu anu amene ndi ochuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi.
Neka dakle, Gospode Bože, bude tvrda rijeè tvoja, koju si rekao Davidu ocu mojemu, jer si me postavio carem nad narodom kojega ima mnogo kao praha na zemlji.
10 Mundipatse nzeru ndi luntha zolamulira anthu awa, pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
Zato daj mi mudrost i znanje da polazim pred narodom ovijem i dolazim, jer ko može suditi narodu tvojemu tako velikomu?
11 Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza izi ndi zokhumba za mtima wako ndipo sunapemphe katundu, chuma kapena ulemu, kapena imfa ya adani ako, ndiponso poti sunapemphe moyo wautali koma nzeru ndi luntha kuti ulamulire anthu anga amene Ine ndakuyika kukhala mfumu yawo,
Tada reèe Bog Solomunu: što ti je to u srcu, a ne išteš bogatstva, blaga ni slave, ni duša nenavidnika svojih, niti išteš duga života, nego išteš mudrosti i znanja da možeš suditi narodu mojemu, nad kojim te postavih carem,
12 Ine ndidzakupatsa nzeru ndi chidziwitso. Ndipo ndidzakupatsanso katundu, chuma ndi ulemu, zinthu zoti palibe mfumu imene inali nazo iwe usanakhalepo ndipo palibe wina amene adzakhale nazo iweyo ukadzafa.”
Mudrost i znanje daje ti se; a daæu ti i bogatstva i slave, kakove nijesu imali carevi prije tebe niti æe poslije tebe imati.
13 Kotero Solomoni anabwerera ku Yerusalemu kuchoka kumalo opembedzerako a ku Gibiyoni, ku tenti ya msonkhano ndipo analamulira Israeli.
I vrati se Solomun s visine koja bijaše u Gavaonu ispred šatora od sastanka u Jerusalim, i carovaše nad Izrailjem.
14 Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi akavalo; anali ndi magaleta 1,400 ndi akavalo 12,000, amene anawayika mʼmizinda yosungira magaleta ndipo ena anali ndi iye mu Yerusalemu.
I nakupi Solomun kola i konjika, i imaše tisuæu i èetiri stotine kola i dvanaest tisuæa konjika, koje namjesti po gradovima gdje mu bijahu kola i kod sebe u Jerusalimu.
15 Mfumu inasandutsa siliva ndi golide kukhala ngati miyala wamba mu Yerusalemu. Inasandutsanso mkungudza kukhala wochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa.
I uèini car te bijaše u Jerusalimu srebra i zlata kao kamena, a kedrovijeh drva kao divljih smokava koje rastu po polju, tako mnogo.
16 Solomoni amagula akavalo ku Igupto ndi Kuwe pakuti anthu amalonda a mfumu amakawagula ku Kuwe.
I dovoðahu Solomunu konje iz Misira i svakojaki trg, jer trgovci carevi uzimahu svakojaki trg za cijenu.
17 Anthu ankagula galeta ku Igupto pa mtengo wa masekeli asiliva 600 ndipo kavalo pa mtengo wa ndalama zasiliva 150. Iwo ankazigulitsanso kwa mafumu onse a Ahiti ndi a Aramu.
I odlažahu, te dogonjahu iz Misira kola po šest stotina sikala srebra, a konje po sto pedeset; i tako svi carevi Hetejski i carevi Sirski preko njih dobivahu.

< 2 Mbiri 1 >