< 1 Samueli 7 >

1 Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
Tada doðoše ljudi iz Kirijat-Jarima, i uzeše kovèeg Gospodnji, i odnesoše ga u kuæu Avinadavovu na brdu, a Eleazara sina njegova posvetiše da èuva kovèeg Gospodnji.
2 Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
A kad kovèeg osta u Kirijat-Jarimu, proðe mnogo vremena, dvadeset godina, i plakaše sav dom Izrailjev za Gospodom.
3 Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
A Samuilo reèe svemu domu Izrailjevu govoreæi: ako se svijem srcem svojim obraæate ka Gospodu, povrzite tuðe bogove izmeðu sebe i Astarote, i spremite srce svoje za Gospoda, njemu jedinomu služite, pa æe vas izbaviti iz ruku Filistejskih.
4 Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
I povrgoše sinovi Izrailjevi Vale i Astarote, i služiše Gospodu jedinomu.
5 Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
Potom reèe Samuilo: skupite svega Izrailja u Mispu, da se pomolim Gospodu za vas.
6 Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
I skupiše se u Mispu, i crpuæi vodu proljevaše pred Gospodom, i postiše onaj dan, i ondje rekoše: sagriješismo Gospodu. I Samuilo suðaše sinovima Izrailjevijem u Mispi.
7 Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
A Filisteji kad èuše da su se sinovi Izrailjevi skupili u Mispu, izidoše knezovi Filistejski na Izrailja. A kad to èuše sinovi Izrailjevi, uplašiše se od Filisteja.
8 Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
I rekoše sinovi Izrailjevi Samuilu: ne prestaj vapiti za nas ka Gospodu Bogu našemu, eda bi nas izbavio iz ruku Filistejskih.
9 Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
Tada Samuilo uze jedno jagnje odojèe, i prinese ga svega Gospodu na žrtvu paljenicu; i vapi Samuilo ka Gospodu za Izrailja, i usliši ga Gospod.
10 Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
I kad Samuilo prinošaše žrtvu paljenicu, približiše se Filisteji da udare na Izrailja; ali zagrmje Gospod grmljavinom velikom u onaj dan na Filisteje i smete ih, i biše pobijeni pred Izrailjem.
11 Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
A Izrailjci izidoše iz Mispe, i potjeraše Filisteje, i biše ih do pod Vet-Har.
12 Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
Tada uze Samuilo kamen, i metnu ga izmeðu Mispe i Sena, i nazva ga Even-Ezer, jer reèe: dovde nam Gospod pomože.
13 Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
Tako biše pokoreni Filisteji, i više ne dolaziše na meðu Izrailjevu. I ruka Gospodnja bješe protiv Filisteja svega vijeka Samuilova.
14 Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
I povratiše se Izrailju gradovi, koje bjehu uzeli Filisteji Izrailju, od Akarona do Gata, i meðe njihove izbavi Izrailj iz ruku Filistejskih; i bi mir meðu Izrailjem i Amorejima.
15 Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
A Samuilo suðaše Izrailju svega vijeka svojega.
16 Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
I iduæi svake godine obilažaše Vetilj i Galgal i Mispu, i suðaše Izrailju u svijem tijem mjestima.
17 Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.
Potom se vraæaše u Ramu, jer ondje bijaše kuæa njegova, i suðaše ondje Izrailju, i ondje naèini oltar Gospodu.

< 1 Samueli 7 >