< 1 Samueli 4 >

1 Ndipo mawu a Samueli anafika kwa Aisraeli onse. Aisraeli anapita kukamenya nkhondo ndi Afilisti. Aisraeli anamanga misasa yawo ku Ebenezeri, ndipo Afilisti anamanga ku Afeki.
And it was doon in tho daies Filisteis camen to gidere in to batel; for Israel yede out ayens Filisteis in to batel, and settiden tentis bisidis the stoon of help. Forsothe Filisteis camen in to Aphet,
2 Afilisti anandanda kuyangʼana Aisraeli nayamba kumenyana. Nkhondo inakula ndipo Afilisti anagonjetsa Aisraeli napha anthu 4,000 pa malo a nkhondopo.
and maden redi scheltrun ayens Israel. Sotheli whanne the batel was bigunnun, Israel turned backis to Filisteis; and as foure thousynde of men weren slayn in that batel `euery where bi feeldis;
3 Asilikali atabwerera ku misasa, akuluakulu a Israeli anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Yehova walola kuti tigonjetsedwe lero pamaso pa Afilisti? Tiyeni tikatenge Bokosi la Chipangano cha Yehova ku Silo kuti Yehovayo abwere kukhala pakati pathu ndi kutipulumutsa mʼmanja mwa adani athu.”
and the puple of Israel turnede ayen to tentis. And the grettere men in birthe of Israel seiden, Whi hath the Lord smyte vs to dai bifore Filisteis? Brynge we to vs fro Silo the arke of boond of pees of the Lord, and come it in to the myddis of vs, that it saue vs fro the hond of oure enemyes.
4 Choncho anatuma anthu ku Silo ndipo anakatenga Bokosi la Chipangano cha Yehova Wamphamvuzonse amene amakhala pa akerubi. Ndipo ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi anatsagana nalo Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
Therfor the puple sente in to Silo, and thei token fro thennus the arke of boond of pees of the Lord of oostis, `that sat on cherubyn. And Ophym and Fynees, twei sones of Heli, weren with the arke of boond of pees of the Lord.
5 Bokosi la Chipangano cha Yehova litafika ku msasa, Aisraeli onse anafuwula kwambiri mpaka nthaka inagwedezeka.
And whanne the arke of boond of pees of the Lord hadde come in to the castels, al Israel criede with grete cry, and the erthe sownede.
6 Atamva kufuwulaku, Afilisti anafunsa, “Kodi kufuwula kwakukulu kumeneku ku misasa ya Ahebri ndi kwachiyani?” Atamva kuti Bokosi la Yehova lafika ku msasako,
And Filisteis herden the vois of cry, and seiden, What is this vois of greet cry in the castels of Ebrews? And thei knewen, that the arke of boond of pees of the Lord hadde come in to castels.
7 Afilisti anachita mantha pakuti iwo ankanena kuti, “Milungu yafika ku msasa. Iwo anati, ‘Tili pamavuto. Chinthu choterechi sichinachitikepo nʼkale lomwe.
And Filisteis dredden, and seiden, God is come in to `the castels; and thei weiliden, and seiden, Wo to vs!
8 Atsoka ife! Adzatipulumutsa ndani mʼmanja mwa milungu yamphamvuyi? Iyi ndi milungu imene inakantha Aigupto ndi miliri yosiyanasiyana mʼchipululu.
for so greet ful ioiyng was not yistirdai, and the thridde day passid; wo to vs! who schal kepe vs fro the hond of `these hiye goddis? these ben the goddis, that smytiden Egipt with al veniaunce in deseert.
9 Limbani mtima Afilisti! Chitani chamuna, kuti mungakhale akapolo a Ahebri monga iwowa alili akapolo anu. Chitani chamuna ndipo menyani nkhondo!’”
Filisteis, be ye coumfortid, and be ye men, serue ye not Ebrews, as thei serueden vs; be ye coumfortid, and fiyte ye.
10 Choncho Afilisti anamenya nkhondo, ndipo anagonjetsa Aisraeli. Iwo anathawa aliyense kwawo. Ankhondo a Aisraeli oyenda pansi okwanira 30,000 anaphedwa.
Therfor Filisteis fouyten, and Israel was slayn, and ech man flei in to his tabernacle; and a ful greet veniaunce was maad, and thretti thousynde of foot men of Israel felden doun.
11 Ndipo Bokosi la Chipangano la Yehova linalandidwa, ndiponso ana awiri Eli, Hofini ndi Finehasi anaphedwa.
And the arke of God was takun; and, twei sones of Heli, Ophym and Fynees, weren deed.
12 Tsiku lomwelo munthu wina wa fuko la Benjamini anathawa ku nkhondo ndipo anafika ku Silo. Iyeyu zovala zake zinali zongʼamba ndipo anadzithira dothi kumutu kuonetsa chisoni.
Sotheli a man of Beniamyn ran fro the scheltrun, and cam in to Silo in that dai, with his cloth torent and his heed bispreynt with dust; and whanne he was comen,
13 Atafika, anapeza Eli atakhala pa mpando wake mʼmbali mwa msewu, akungoyangʼana, pakuti ankadera nkhawa Bokosi la Mulungu. Munthuyo atalowa mu mzindamo ndi kufotokoza zimene zinachitika ku nkhondo, anthu onse a mu mzindamo anayamba kulira.
Heli sat `on an hiye seete, `and bihelde ayens the weie; for his herte was dredyng for the arke of the Lord. Sotheli aftir that thilke man entride, he telde to the citee, and al the citee yellide.
14 Eli atamva kulirako anafunsa kuti, “Kodi phokosoli likutanthauza chiyani?” Tsono munthu wa fuko la Benjamini uja anapita msanga kwa Eli kukamufotokozera.
And Heli herde the soun of cry, and seide, What is this sown of this noise? And he hastide, and cam, and telde to Heli.
15 Nthawiyo nʼkuti Eli ali wa zaka 98 ndipo maso ake anali atachita khungu kotero kuti samatha kuona.
Forsothe Heli was of foure score yeer and eiytene, and hise iyen dasiwiden, and he myyte not se.
16 Munthuyo anamuwuza Eli kuti, “Ine ndabwera kuchokera ku nkhondo, ndathawako lero lomwe lino.” Eli anafunsa, “Nanga nkhondo yayenda bwanji mwana wanga?”
And he seide to Heli, Y am that cam fro batel, and Y am that flei to dai fro the scheltrun. To whom Ely seide, My sone, what is doon?
17 Iye anayankha kuti, “Aisraeli athawa pamaso pa Afilisti. Anthu ambirimbiri aphedwa. Ana anunso Hofini ndi Finehasi aphedwa. Bokosi la Mulungu nalonso lalandidwa.”
Forsothe he that telde answeride, and seide, Israel flei bifor Filisteis, and a greet fal is maad in the puple; ferthermore and thi twey sones, Ophym and Fynees, ben deed, and the arke of God is takun.
18 Atangotchula Bokosi la Yehova, Eli anagwa chagada, kuchoka pa mpando wake umene unali mʼmbali mwa chitseko cha mpanda. Khosi lake linathyoka ndipo anafa, pakuti anali okalamba ndi onenepa kwambiri. Iye anatsogolera Israeli zaka makumi anayi.
And whanne he hadde nemyd the arke of God, Hely felde fro `the hiye seete bacward bisidis the dore, and `was deed; for the nollis weren brokun. For he was an eld man, and of greet age; and he demyde Israel bi fourti yeer.
19 Nthawiyo, mpongozi wa Eli, mkazi wa Finehasi anali woyembekezera ndipo anali pafupi kuchira. Atamva kuti Bokosi la Mulungu lalandidwa ndi kuti mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake amwalira, ululu wa pobereka mwana unamufikira modzidzimutsa ndipo anabereka mwana.
Forsothe his douyter in lawe, `the wijf of Finees, was with childe, and niy the child bering; and whanne `the message was herd that the arke of God was takun, and that hir fadir in lawe was deed, and hir hosebonde, sche bowide hir silf, and childide; for sodeyn sorewis felden in to hir.
20 Popeza mkaziyo anali pafupi kumwalira, akazi amene amamuthandiza anati, “Usaope, wabereka mwana wamwamuna” Koma iye sanayankhe kapena kulabadirako.
Sotheli in that moment of hir deeth, wymmen that stoden aboute hir, seiden to hir, Drede thou not, for thou hast childid a sone. And sche answeride not to hem, for nether `sche perseyuede.
21 Tsono iye anatcha mwanayo dzina loti Ikabodi kutanthauza kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli,” chifukwa cha kulandidwa Bokosi la Mulungu ndi imfa ya mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake.
And sche clepide the child Ichaboth, and seide, The glorie of the Lord is translatid fro Israel, for the arke of God is takun; and for hir fadir in lawe and for hir hosebonde sche seide,
22 Ananena momwemo kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli, pakuti Bokosi la Mulungu lalandidwa.”
The glorie of God is translatid fro Israel, for the arke of God is takun.

< 1 Samueli 4 >