< 1 Samueli 30 >

1 Pa tsiku lachitatu, Davide ndi anthu ake anakafika ku Zikilagi. Tsono anapeza Aamaleki atawononga kale dera la Negevi ndi Zikilagi. Anathira nkhondo mzinda wa Zikilagi ndi kuwutentha ndi moto.
I treæi dan doðe David sa svojim ljudima u Siklag, a Amalici bijahu udarili na južnu stranu i na Siklag, i razvalili Siklag i ognjem ga spalili.
2 Anatenga akazi ndi onse amene anali mʼmenemo akuluakulu ndi angʼono omwe kuti akakhale akapolo. Sanaphe aliyense koma anawatenga amoyo napita nawo.
I bjehu zarobili ženskinje koje bješe ondje, i malo i veliko; ali ne bjehu ubili nikoga, nego ih bjehu odveli i otišli svojim putem.
3 Davide ndi anthu ake atafika ku Zikilagi anapeza kuti mzindawo watenthedwa ndi moto ndipo akazi awo, ana awo, amuna ndi akazi atengedwa ukapolo.
I kad David doðe sa svojim ljudima u grad, a to grad spaljen ognjem, i žene njihove i sinovi i kæeri njihove zarobljene.
4 Kotero Davide ndi anthu ake analira mofuwula mpaka analibenso mphamvu zolirira.
I podiže David i narod koji bijaše s njim glas svoj, i plakaše dokle veæ ne mogoše plakati.
5 Akazi awiri a Davide, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wa Nabala wa ku Karimeli anatengedwanso.
I obje žene Davidove zarobiše se, Ahinoama iz Jezraela i Avigeja iz Karmila žena Navalova.
6 Davide anavutika kwambiri mu mtima mwake chifukwa anthu amakamba zoti amuponye miyala popeza aliyense anali ndi chisoni pokumbukira ana ake aamuna ndi aakazi. Koma Davide anapeza mphamvu mwa Yehova Mulungu wake.
I David bješe na muci velikoj, jer narod govoraše da ga zaspu kamenjem; jer žalostan bješe sav narod, svaki za sinovima svojim i za kæerima svojim; ali se David ohrabri u Gospodu Bogu svojem.
7 Kenaka Davide anawuza wansembe Abiatara, mwana wa Ahimeleki kuti, “Ndipatse efodi ija.” Abiatara anabwera nayo efodiyo.
I reèe David Avijataru svešteniku sinu Ahimelehovu: uzmi opleæak za me. I uze Avijatar opleæak za Davida.
8 Tsono Davide anapempha nzeru kwa Yehova nati, “Kodi ndilitsatire gulu lankhondoli? Kodi ndidzawapambana?” Yehova anayankha kuti, “Litsatire, iwe udzawapambana ndithu ndipo udzapulumutsa anthu ako.”
I upita David Gospoda govoreæi: hoæu li potjerati tu èetu? hoæu li je stignuti? A Gospod mu reèe: potjeraj, jer æeš zacijelo stignuti i izbaviæeš.
9 Davide pamodzi ndi anthu ake 600 aja ananyamuka nafika ku mtsinje wa Besori. Kumeneko anasiyako anthu ena.
I poðe David sa šest stotina ljudi što bijahu s njim, i doðoše do potoka Vosora; i ondje ostaše jedni.
10 Davide ndi anthu ake 400 anapitirira kuwalondola Aamaleki aja. Koma anthu ena 200 anatsala popeza anatopa moti sakanatha kuwoloka mtsinje wa Besori uja.
A David sa èetiri stotine ljudi potjera dalje, a dvjesta ljudi osta, koji sustaše te ne mogoše prijeæi preko potoka Vosora.
11 Anthu amene anali ndi Davide anapeza Mwigupto mʼmunda wina ndipo anabwera naye kwa Davide. Iwo anamupatsa madzi kuti amwe ndi chakudya kuti adye.
I naðoše jednoga Misirca u polju, i dovedoše ga k Davidu, i dadoše mu hljeba da jede i vode da pije,
12 Anamupatsanso chidutswa cha keke yankhuyu ndi makeke awiri a mphesa zowumika kuti adye. Atadya anapezanso mphamvu popeza anakhala masiku atatu wosadya kapena kumwa kanthu kalikonse.
I dadoše mu grudu smokava i dva grozda suha. I pojedavši oporavi se, jer tri dana i tri noæi ne bješe ništa jeo niti vode pio.
13 Davide anafunsa kuti, “Kodi ndiwe yani, ndipo ukuchokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine Mwigupto, kapolo wa Mwamaleki. Mbuye wanga anandisiya nditayamba kudwala masiku atatu apitawo.
Tada mu reèe David: èiji si ti? i odakle si? A on reèe: ja sam rodom Misirac, sluga jednoga Amalika, a gospodar me ostavi, jer se razboljeh prije tri dana.
14 Ife tinathira nkhondo dera la kummwera kwa mayiko a Akereti, dera la Yuda, ndi dera la kummwera kwa mayiko a Kalebe. Mzinda wa Zikilagi tinawutentha ndi moto.”
Udarismo na južnu stranu Heretejsku i na Judinu i na južnu stranu Halevovu, i Siklag spalismo ognjem.
15 Davide anamupempha kuti, “Kodi unganditsogolere kumene kuli gulu lankhondoli?” Iye anayankha kuti, “Mukandilonjeza molumbira kuti simudzandipha kapena kundipereka kwa mbuye wanga, ine ndikulondolerani kumene kuli gululo.”
A David mu reèe: bi li me mogao odvesti k toj èeti? A on reèe: zakuni mi se Bogom da me neæeš pogubiti ni izdati u ruke mojemu gospodaru, pa æu te odvesti k toj èeti.
16 Mwigupto uja anaperekeza Davide. Tsono Aamaleki anali atamwazikana ponseponse. Iwo ankadya, kumwa ndi kuvina chifukwa cha zofunkha zambiri zimene anatenga ku dziko la Afilisti ndi ku dziko la Ayuda.
I odvede ga; i gle, oni se bijahu raširili po svoj zemlji onoj jeduæi i pijuæi i veseleæi se velikim plijenom koji zaplijeniše iz zemlje Filistejske i iz zemlje Judine.
17 Tsono Davide anawakantha kuyambira madzulo atsikulo mpaka madzulo a tsiku linalo. Palibe anapulumuka kupatula anyamata 400 amene anakwera pa ngamira nʼkuthawa.
I David ih bi od veèera do veèera drugoga dana, te niko ne uteèe, osim èetiri stotine mladiæa, koji sjedavši na kamile pobjegoše.
18 Choncho Davide analanditsa zinthu zonse zimene Aamaleki aja anatenga. Anapulumutsanso akazi ake awiri aja.
I tako izbavi David sve što bijahu uzeli Amalici, i obje žene svoje izbavi David.
19 Palibe chimene chinasowa anthu onse, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, mnyamata mpaka mtsikana anapulumutsidwa. Davide anapulumutsa chilichonse chimene anafunkha Aamaleki aja.
I ništa ne izgubiše, ni malo ni veliko, ni sinove ni kæeri, ni što od plijena i od svega što im bijahu uzeli; sve povrati David.
20 Anapulumutsanso nkhosa ndi ngʼombe zonse. Tsono anthu ankakusa ziwetozo namati, “Izi ndizo zofunkha za Davide.”
Takoðer uze David i ostale sve ovce i volove, koje goneæi pred svojom stokom govorahu: ovo je plijen Davidov.
21 Davide anafika ku malo kumene kunali anthu 200 otopa kwambiri aja amene sanathe kutsagana naye koma anangokhala ku mtsinje wa Besori. Tsono ananyamuka kuti akumane ndi Davide pamodzi ndi anthu amene anali naye. Davide anawayandikira nawalonjera.
I kad se vrati David k onijem dvjesta ljudi koji bjehu sustali te ne mogoše iæi za Davidom, i koje ostavi na potoku Vosoru, izidoše na susret Davidu i narodu koji bijaše s njim. I David pristupivši k narodu pozdravi ih.
22 Tsono anthu ena oyipa mtima achabechabe mwa amene anatsagana ndi Davide aja anati, “Popeza awa sanapite nafe, sitiwapatsako zofunkha zimene tapulumutsazi, kupatula kuti aliyense atenge mkazi wake ndi ana ake azipita.”
Tada progovoriše svi zli i nevaljali ljudi izmeðu onijeh koji su išli s Davidom, i rekoše: što nijesu išli s nama, zato da im ne damo od plijena koji izbavismo, nego svaki ženu svoju i sinove svoje neka uzmu, pa nek idu.
23 Koma Davide anawayankha kuti, “Ayi, abale anga, musachite zimenezi ndi zinthu zimene Yehova watipatsa. Iye watisunga ndi kupereka mʼmanja mwathu gulu la ankhondo limene linabwera kudzalimbana nafe.
Ali David reèe: nemojte tako èiniti, braæo moja, s onijem što nam je dao Gospod koji nas je saèuvao i dao nam u ruke èetu koja bješe izašla na nas.
24 Ndani angakumvereni zimene mukunenazi? Gawo la munthu amene anapita kukamenya nkhondo likhale lofanana ndi la munthu amene anatsala pano kuyangʼanira katundu wathu. Pasakhale kusiyana kulikonse.”
I ko æe vas poslušati u tome? jer kakav je dio onome koji ide u boj taki je i onome koji ostane kod prtljaga; jednako treba da podijele.
25 Choncho Davide anakhazikitsa ngati lamulo mʼchitidwe woterewu pakati pa Aisraeli kuyambira tsiku limenelo mpaka lero.
Tako bi od toga dana unapredak, i to posta uredba i zakon u Izrailju do danas.
26 Davide atafika ku Zikilagi, anatumiza zina mwa zofunkhazo kwa akuluakulu a Yuda, amene anali abwenzi ake. Anati, “Nayi mphatso yanu yochokera pa zofunkha za adani a Yehova.”
I kad doðe David u Siklag, posla od plijena starješinama Judinijem, prijateljima svojim, govoreæi: evo vam dar od plijena neprijatelja Gospodnjih;
27 Iye anatumiza mphatsozo kwa anthu a ku Beteli, Ramoti-Negavi, Yatiri,
Onima u Vetilju, i onima u Ramotu na jugu, i onima u Jatiru,
28 Aroeri, Sifimoti, Esitemowa
I onima u Aroiru, i onima u Sifmotu, i onima u Estemoji,
29 Rakala, mizinda ya fuko la Ayerahimeeli, mizinda ya fuko la Akeni,
I onima u Rahalu, i onima u gradovima Jerameilskim, i onima u gradovima Kenejskim,
30 a ku Horima, Borasani, Ataki,
I onima u Ormi, i onima u Hor-Asanu, i onima u Atahu,
31 Hebroni pamodzi ndi onse a kumalo kumene Davide ndi anthu ake anakhala akuyendayendako.
I onima u Hevronu i po svijem mjestima u koja je dolazio David s ljudima svojim.

< 1 Samueli 30 >