< 1 Samueli 3 >

1 Samueli ankatumikira Yehova moyangʼaniridwa ndi Eli. Masiku amenewo mawu a Yehova sankamveka pafupipafupi. Kuona zinthu mʼmasomphenya sikunkachitikanso kawirikawiri.
A dijete Samuilo služaše Gospodu pred Ilijem; i rijeè Gospodnja bješe rijetka u ono vrijeme, i ne javljahu se utvare.
2 Tsiku lina Eli, amene maso anali ofowoka ndi kuti sankatha kuona bwino, anagona pa malo ake.
Jednom u to vrijeme Ilije ležaše na svom mjestu; a oèi mu poèinjahu tamnjeti te ne mogaše vidjeti;
3 Nthawiyi nʼkuti nyale ya Mulungu isanazimitsidwe. Samueli anali gone mu Nyumba ya Yehova, kumene kunali Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
I Samuilo ležaše u domu Gospodnjem gdje bijaše kovèeg Božji, i žišci Gospodnji još ne bjehu pogašeni.
4 Yehova anayitana Samueli. Iye anayankha kuti, “Wawa.”
I viknu Gospod Samuila, a on reèe: evo me.
5 Ndipo iyeyo anathamangira kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera ndamva kuyitana.” Koma Eli anati, “Ine sindinakuyitane, bwerera kagone.” Ndipo iye anapita kukagona.
I pritrèa k Iliju, i reèe mu: evo me, što si me zvao? A on reèe: nijesam te zvao, idi lezi. I on otide i leže.
6 Yehova anayitananso, “Samueli!” Ndipo Samueli anadzuka ndi kupita kwa Eli nati, “Ndabwera popeza ndamva mukundiyitana.” Eli nati, “Mwana wanga, ine sindinakuyitane, bwerera kagone.”
A Gospod opet viknu Samuila, i Samuilo usta, i otide k Iliju, i reèe: evo me, što si me zvao? A on reèe: nijesam te zvao, sine; idi lezi.
7 Nthawiyi nʼkuti Samueli asanadziwe Yehova ndipo Mawu a Yehova nʼkuti asanawululidwe kwa iye.
A Samuilo još ne poznavaše Gospoda, i još mu ne bješe javljena rijeè Gospodnja.
8 Yehova anayitananso Samueli kachitatu ndipo Samueli anadzuka ndikupita kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera popeza mwandiyitana ndithu.” Apo Eli anazindikira kuti Yehova ndiye ankayitana mnyamatayo.
Tada opet viknu Gospod Samuila treæi put, i on usta i otide k Iliju, i reèe: evo me, što si me zvao? Tada razumje Ilije da Gospod zove dijete.
9 Tsono Eli anamuwuza Samueli kuti, “Pita ukagone ndipo akakuyitananso ukanene kuti, ‘Yankhulani Yehova, pakuti mtumiki wanu ndikumvetsera.’” Choncho Samueli anapita ndi kukagona pamalo pake.
I reèe Ilije Samuilu: idi lezi; a ako te zovne, a ti reci: govori Gospode, èuje sluga tvoj. I Samuilo otide, i leže na svoje mjesto.
10 Yehova anabwera ndi kuyima pomwepo, ndi kuyitana monga nthawi zina zija, “Samueli! Samueli!” Ndipo Samueli anayankha, “Yankhulani, pakuti mtumiki wanu akumvetsera.”
A Gospod doðe i stade; i zovnu kao prije: Samuilo! Samuilo! A Samuilo reèe: govori, èuje sluga tvoj.
11 Ndipo Yehova anati kwa Samueli, “Taona, patsala pangʼono kuti ndichite chinthu china mu Israeli chimene chidzadabwitsa aliyense amene adzamve.
I reèe Gospod Samuilu: evo uèiniæu nešto u Izrailju da æe zujati oba uha svakome ko èuje.
12 Tsiku limenelo ndidzachitadi zonse zimene ndinayankhula zokhudza banja la Eli kuyambira poyamba mpaka pomaliza.
U taj dan æu uèiniti Iliju sve što sam govorio za kuæu njegovu, od poèetka do kraja.
13 Pakuti ndinamudziwitsa kuti Ine ndikhoza kulanga banja lake kwamuyaya chifukwa cha zoyipa zimene ana ake ankadziyipitsa nazo. Iye ankadziwa zimenezi koma osawaletsa.
Jer sam mu javio da æu suditi domu njegovu dovijeka za nevaljalstvo, za koje je znao da njim navlaèe na se prokletstvo sinovi njegovi, pa im nije zabranio.
14 Nʼchifukwa chake ndinalumbira kuti, ‘Zoyipa zimene banja la Eli linandichita sizidzafafanizidwa mpaka muyaya ngakhale adzapereke nsembe kapena zopereka zina.’”
Zato se zakleh domu Ilijevu da se neæe oèistiti nevaljalstvo doma Ilijeva nikakvom žrtvom ni prinosom dovijeka.
15 Samueli anagona mpaka mmawa. Atadzuka anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova. Iye anachita mantha kumuwuza Eli za masomphenya ake.
I Samuilo spava do jutra, pa otvori vrata doma Gospodnjega. Ali se bojaše Samuilo kazati Iliju za utvaru.
16 Koma Eli anamuyitana nati, “Samueli mwana wanga.” Samueli anayankha kuti, “Wawa.”
A Ilije zovnu Samuila i reèe: Samuilo, sine! A on reèe: evo me.
17 Tsono Eli anafunsa kuti, “Yehova wakuwuza chiyani? Usandibisire. Mulungu akulange ndithu ngati undibisira chilichonse cha zimene wakuwuza.”
A on reèe: kakve su rijeèi što ti je kazao? nemoj zatajiti od mene; tako ti uèinio Bog i tako ti dodao, ako zatajiš od mene što god što ti je kazao.
18 Choncho Samueli anamuwuza zonse, sanamubisire kalikonse. Ndipo Eli anati, “Iye ndi Yehova, mulekeni achite chimene chamukomera.”
I Samuilo mu kaza sve, i ništa ne zataji od njega. A on reèe: Gospod je, neka èini što mu je volja.
19 Yehova anali ndi Samueli pamene amakula, ndipo zonse zimene ankayankhula zinkachitikadi.
A Samuilo rastijaše, i Gospod bijaše s njim, i ne pusti da padne na zemlju nijedna rijeè njegova.
20 Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dera la Dani mpaka ku Beeriseba anazindikira kuti Yehova analozadi chala pa Samueli kuti akhale mneneri wake.
I sav Izrailj od Dana do Virsaveje pozna da je Samuilo vjeran prorok Gospodnji.
21 Yehova anapitiriza kuoneka ku Silo, ndipo kumeneko anadziwulula yekha kwa Samueli mwa mawu ake.
I Gospod se stade opet javljati u Silomu, jer se Gospod javljaše Samuilu u Silomu rijeèju Gospodnjom.

< 1 Samueli 3 >