< 1 Samueli 24 >

1 Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.”
I kad se Saul vrati odagnavši Filisteje, rekoše mu govoreæi: eno Davida u pustinji Engadskoj.
2 Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.
Tada uze Saul tri tisuæe ljudi izabranijeh iz svega Izrailja, i otide da traži Davida i ljude njegove po vrletima gdje su divokoze.
3 Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo.
I doðe k torovima ovèijim ukraj puta gdje bijaše peæina; i Saul uðe u nju rad sebe; a David i njegovi ljudi sjeðahu u kraju u peæini.
4 Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
I rekoše Davidu ljudi njegovi: evo dana, za koji ti reèe Gospod: evo ja ti predajem neprijatelja tvojega u ruke da uèiniš s njim što ti je volja. I David usta, te polako otsijeèe skut od plašta Saulova.
5 Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
A poslije zadrhta srce Davidu što otsijeèe skut Saulu.
6 Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.”
I reèe svojim ljudima: ne dao Bog da to uèinim gospodaru svojemu, pomazaniku Gospodnjemu, da podignem ruku svoju na nj. Jer je pomazanik Gospodnji.
7 Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.
I odvrati rijeèima David ljude svoje i ne dade im da ustanu na Saula. I Saul izašav iz peæine poðe svojim putem.
8 Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi.
Potom David usta, i izašav iz peæine stade vikati za Saulom govoreæi: care gospodine! A Saul se obazre, a David se savi licem do zemlje i pokloni se.
9 Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’
I reèe David Saulu: zašto slušaš što ti kažu ljudi koji govore: eto David traži zlo tvoje?
10 Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’
Evo, danas vidješe oèi tvoje da te je Gospod bio predao danas u moje ruke u ovoj peæini, i rekoše mi da te ubijem: ali te poštedjeh, i rekoh: neæu dignuti ruke svoje na gospodara svojega, jer je pomazanik Gospodnji.
11 Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.
Evo, oèe moj, evo vidi skut od plašta svojega u mojoj ruci; otsjekoh skut od plašta tvojega, a tebe ne ubih; poznaj i vidi da nema zla ni nepravde u ruci mojoj, i da ti nijesam zgriješio; a ti vrebaš dušu moju da je uzmeš.
12 Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani.
Gospod neka sudi izmeðu mene i tebe, i neka me osveti od tebe; ali ruka se moja neæe podignuti na te.
13 Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.
Kako kaže stara prièa: od bezbožnijeh izlazi bezbožnost; zato se ruka moja neæe podignuti na te.
14 “Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi?
Za kim je izašao car Izrailjev? koga goniš? mrtva psa, buhu jednu.
15 Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”
Gospod neka bude sudija, i neka rasudi izmeðu mene i tebe; on neka vidi i raspravi moju parnicu i izbavi me iz ruke tvoje.
16 Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza.
A kad izgovori David ove rijeèi Saulu, reèe Saul: je li to tvoj glas, sine Davide? I podigavši Saul glas svoj zaplaka.
17 Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa.
I reèe Davidu: praviji si od mene, jer si mi vratio dobro za zlo koje sam ja tebi uèinio.
18 Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe.
I danas si mi pokazao da mi dobro èiniš; jer me Gospod dade tebi u ruke, a ti me opet ne ubi.
19 Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi.
I ko bi našavši neprijatelja svojega pustio ga da ide dobrijem putem? Gospod neka ti vrati dobro za ovo što si mi uèinio danas.
20 Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako.
I sada, evo, znam da æeš zacijelo biti car, i jako æe biti u tvojoj ruci carstvo Izrailjevo.
21 Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”
Zato mi se sada zakuni Gospodom da neæeš istrijebiti sjemena mojega poslije mene, ni imena mojega zatrti u domu oca mojega.
22 Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.
I zakle se David Saulu; i Saul otide kuæi svojoj, a David i ljudi njegovi otidoše na tvrdo mjesto.

< 1 Samueli 24 >