< 1 Samueli 23 >

1 Davide atawuzidwa kuti “Onani, Afilisti akuthira nkhondo mzinda wa Keila ndi kulanda zokolola zawo za mʼnkhokwe,”
Tada javiše Davidu govoreæi: evo Filisteji udariše na Keilu, i haraju gumna.
2 anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite ndikamenyane nawo Afilistiwa?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, kamenyane nawo Afilisti ndi kupulumutsa mzinda wa Keila.”
I upita David Gospoda govoreæi: hoæu li iæi i udariti na te Filisteje? A Gospod reèe Davidu: idi, i pobiæeš Filisteje i izbaviti Keilu.
3 Koma anthu amene anali ndi Davide anati, “Ngati tikuchita mantha ku Yuda konkuno, nanji kupita ku Keila kukamenyana ndi ankhondo a Afilisti!”
A Davidu rekoše ljudi njegovi: evo nas je strah ovdje u Judinoj zemlji, a šta æe biti kad poðemo u Keilu na oko Filistejski.
4 Davide anafunsanso Yehova, ndipo Yehova anamuyankha kuti, “Pita ku Keila pakuti ndapereka Afilisti mʼdzanja lako.”
Zato David opet upita Gospoda, a Gospod mu odgovori i reèe: ustani, idi u Keilu, jer æu ja predati Filisteje u ruke tvoje.
5 Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Keila kukamenyana ndi Afilisti. Anapha Afilisti ambiri ndi kutenga ziweto zawo. Choncho anapulumutsa anthu a ku Keila.
Tada otide David sa svojim ljudima u Keilu, i udari na Filisteje, i otjera im stoku, i pobi ih ljuto; tako izbavi David stanovnike Keilske.
6 (Pamene Abiatara mwana wa Ahimeleki anathawira kwa Davide anabwera ndi efodi mʼmanja mwake).
A kad Avijatar sin Ahimelehov pobježe k Davidu u Keilu, donese sobom opleæak.
7 Sauli atamva kuti Davide wapita ku Keila anati, “Mulungu wamupereka kwa ine, pakuti Davide wadzitsekera yekha mʼndende polowa mu mzinda umene uli ndi zipata ndi zotsekera zake.”
Potom javiše Saulu da je David došao u Keilu; i reèe Saul: dao ga je Bog u moje ruke, jer se zatvorio ušavši u grad, koji ima vrata i prijevornice.
8 Choncho Sauli anasonkhanitsa ankhondo ake nawatuma ku Keila kuti akamuzungulire Davide ndi anthu ake.
I sazva Saul sav narod na vojsku da ide na Keilu i opkoli Davida i ljude njegove.
9 Davide atadziwa kuti Sauli akufuna kumuchita chiwembu, anawuza Abiatara wansembe uja kuti, “Bwera nayo efodiyo.”
Ali David doznavši da mu Saul zlo kuje, reèe Avijataru svešteniku: uzmi na se opleæak.
10 Tsono Davide anayankhula ndi Yehova kuti, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, ine mtumiki wanu ndamva ndithu kuti Sauli akufuna kubwera ku Keila ndi kudzawononga mzindawu chifukwa cha ine.
I reèe David: Gospode Bože Izrailjev! èuo je sluga tvoj da se Saul sprema da doðe na Keilu da raskopa grad mene radi.
11 Kodi anthu a Keila adzandipereka mʼmanja mwa Sauli? Kodi Sauli abweradi monga ndamvera ine mtumiki wanu? Inu Yehova Mulungu wa Israeli, chonde, ndiwuzeni ine mtumiki wanu.” Ndipo Yehova anati, “Sauli abweradi.”
Hoæe li me Keiljani predati u njegove ruke? hoæe li doæi Saul kao što je èuo sluga tvoj? Gospode Bože Izrailjev! kaži sluzi svojemu. A Gospod odgovori: doæi æe.
12 Davide anafunsanso, “Kodi anthu a ku Keila adzapereka ine ndi anthu angawa kwa Sauli?” Ndipo Yehova anayankha, “Iwo adzakuperekanidi.”
Opet reèe David: Keiljani hoæe li predati mene i moje ljude u ruke Saulove? A Gospod odgovori: predaæe.
13 Choncho Davide ndi anthu ake, omwe analipo 600, anachoka ku Keila namayenda mothawathawa. Sauli atamva kuti Davide wathawa ku Keila, sanatumizeko ankhondo ake aja.
Tada se David podiže sa svojim ljudima, oko šest stotina ljudi, i otidoše iz Keile, i idoše kuda mogoše. A kad Saulu javiše da je David pobjegao iz Keile, tada on ne htje iæi.
14 Davide ankakhala mʼmapanga mʼdziko lamapiri ku chipululu cha Zifi. Sauli ankamufufuza tsiku ndi tsiku, koma Mulungu sanapereke Davide mʼmanja mwake.
A David se bavljaše u pustinji po tvrdijem mjestima, i namjesti se na jednom brdu u pustinji Zifu. A Saul ga tražaše jednako, ali ga Gospod ne dade u njegove ruke.
15 Davide anaona kuti Sauli akufunafuna kuti amuphe. Nthawiyi nʼkuti Davide ali mʼchipululu cha Zifi ku Horesi.
I David videæi da je Saul izašao te traži dušu njegovu, osta u pustinji Zifu, u šumi.
16 Ndipo Yonatani mwana wa Sauli anapita kwa Davide ku Horesi ndipo anamulimbitsa mtima pomuwuza kuti Yehova ali naye.
A Jonatan sin Saulov podiže se i doðe k Davidu u šumu, i ukrijepi mu ruku u Gospodu;
17 Iye anamuwuza kuti, “Usaope, abambo anga sadzakupha. Iwe udzakhala mfumu ya Israeli ndipo ine ndidzakhala wachiwiri wako. Ngakhale abambo anga Sauli akudziwa zimenezi.”
I reèe mu: ne boj se, jer te neæe stignuti ruka cara Saula oca mojega; nego æeš carovati nad Izrailjem, a ja æu biti drugi za tobom; i Saul otac moj zna to.
18 Awiriwa anachita pangano pamaso pa Yehova. Ndipo Yonatani anabwerera kwawo, koma Davide anakhalabe ku Horesi.
I uèiniše njih dvojica vjeru pred Gospodom; i David osta u šumi, a Jonatan otide kuæi svojoj.
19 Anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ku Gibeya ndipo anamuwuza kuti, “Davide akubisala kwathu, mʼmapanga a ku Horesi, mʼphiri la Hakila, kummwera kwa Yesimoni.
Tada doðoše Zifeji k Saulu u Gavaju, i rekoše: ne krije li se David kod nas po tvrdijem mjestima u šumi na brdu Eheli nadesno od Gesimona?
20 Tsopano inu, mubwere nthawi iliyonse imene mukufuna, ndipo ife tidzamupereka kwa mfumu.”
Sada dakle po svoj želji duše svoje, care, izidi, a naše æe biti da ga predamo u ruke caru.
21 Sauli anayankha kuti, “Yehova akudalitseni pakuti mwandichitira chifundo.
A Saul reèe: Gospod da vas blagoslovi, što me požaliste.
22 Pitani mukatsimikizire. Mukaone kumene amakhala ndiponso mupeze munthu amene wamuona. Anthu amandiwuza kuti ndi wochenjera kwambiri.
Idite sada i doznajte još bolje i razberite i promotrite gdje se sakrio i ko ga je ondje vidio; jer mi kažu da je vrlo lukav.
23 Kafufuzeni ndithu malo onse kumene amabisalako, ndipo mubwerenso kuno mudzandiwuze chenicheni. Pambuyo pake ine ndidzapita nanu. Ngatidi ali mʼderalo ndidzamusaka pakati pa mabanja onse a Yuda.”
Promotrite i vidite sva mjesta gdje se krije, pa opet doðite k meni kad dobro doznate, i ja æu poæi s vama; i ako bude u zemlji, tražiæu ga po svijem tisuæama Judinijem.
24 Kotero iwo ananyamuka ndi kupita ku Zifi, koma Sauli asananyamuke. Nthawi imeneyi Davide ndi anthu ake anali ku chipululu cha Maoni, ku Araba kummwera kwa Yesimoni.
Tada ustaše i otidoše u Zif prije Saula; a David i ljudi njegovi bijahu u pustinji Maonu u ravnici nadesno od Gesimona.
25 Sauli ndi anthu ake anapita kukamufufuza Davide. Koma Davide atamva izi anathawa ndi kukabisala ku thanthwe la chipululu cha Maoni. Sauli atamva kuti Davide anathawira ku Maoni anamutsatira ku chipululu komweko.
I Saul izide sa svojim ljudima da ga traži; a Davidu javiše, te on siðe sa stijene i stade u pustinji Maonu. A Saul kad to èu, otide za Davidom u pustinju Maon.
26 Sauli amayenda mbali ina ya phirilo, ndipo Davide ndi anthu ake nawonso anali mbali ina ya phirilo. Koma Davide ndi anthu ake anafulumira kumuthawa Sauli pamene Sauliyo ndi anthu ake ali pafupi kuwagwira.
I Saul iðaše jednom stranom planine, a David sa svojim ljudima drugom stranom planine; i David hiæaše da uteèe Saulu, jer Saul sa svojim ljudima opkoljavaše Davida i njegove ljude da ih pohvata.
27 Nthawi yomweyo munthu wina wamthenga anabwera kudzamuwuza Sauli kuti, “Bwerani msanga! Afilisti akuthira nkhondo dzikoli.”
U tom doðe glasnik Saulu govoreæi: brže hodi; jer Filisteji udariše na zemlju.
28 Choncho Sauli analeka kuthamangitsa Davide ndipo anapita kukamenyana ndi Afilisti. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Mwala wa Malekano.
Tada se vrati Saul ne tjerajuæi dalje Davida, i otide pred Filisteje. Otuda se prozva ono mjesto Sela-Amalekot.
29 Ndipo Davide anachoka kumeneko ndi kukakhala ku mapanga a ku Eni Gedi.
A David otišavši odande stade na tvrdijem mjestima Engadskim.

< 1 Samueli 23 >