< 1 Samueli 2 >

1 Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
Wtedy Anna modliła się i powiedziała: Moje serce raduje się w PANU, mój róg jest wywyższony w PANU. Moje usta szeroko otworzyły się przeciwko moim wrogom, gdyż raduję się z twego zbawienia.
2 “Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
Nikt nie jest tak święty jak PAN. Nie ma bowiem nikogo oprócz ciebie i nikt nie jest taką skałą jak nasz Bóg.
3 “Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
Nie mówcie już pysznych słów i niech z waszych ust nie wychodzą słowa wyniosłe. PAN bowiem [jest] Bogiem wiedzy, on waży czyny.
4 “Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
Łuki mocarzy [zostały] złamane, a słabi są przepasani mocą.
5 Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
Syci najmują się za chleb, a głodni przestali [głodować]. Nawet niepłodna urodziła siedmioro, a wielodzietna więdnie.
6 “Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol h7585)
PAN zabija i ożywia, wprowadza do grobu i wyprowadza. (Sheol h7585)
7 Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
PAN czyni ubogim i bogatym, poniża i wywyższa.
8 Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
Podnosi z prochu ubogiego, a z gnoju podnosi żebraka, by posadzić ich z książętami i pozwolić im odziedziczyć tron chwały. Do PANA bowiem należą filary ziemi, na nich osadził świat.
9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
Strzeże stóp swych świętych, a bezbożni zamilkną w ciemności, bo nie swoją siłą zwycięży człowiek.
10 Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
PAN pokruszy swoich przeciwników i zagrzmi przeciwko nim z nieba. PAN będzie sądził krańce ziemi, udzieli siły swemu królowi i wywyższy róg swego pomazańca.
11 Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
Potem Elkana wrócił do Rama, do swego domu, a dziecko służyło PANU przy kapłanie Helim.
12 Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
Lecz synowie Heliego byli synami Beliala i nie znali PANA.
13 Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
Był bowiem taki zwyczaj kapłanów wobec ludu: kiedy ktoś składał ofiarę, sługa kapłana przychodził, gdy mięso się gotowało, z trójzębnymi widelcami w ręce.
14 Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
I wkładał je do garnka, kotła, rondla lub misy i to, co wyjął widełkami, kapłan zabierał dla siebie. Tak czynili w Szilo wszystkim Izraelitom, którzy tam przychodzili.
15 Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
Ponadto, zanim jeszcze spalono tłuszcz, przychodził sługa kapłana i mówił do człowieka składającego ofiary: Daj mięso na pieczeń dla kapłana, bo nie weźmie on od ciebie mięsa gotowanego, tylko surowe.
16 Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
A jeśli taki człowiek mu odpowiedział: Niech najpierw spalą tłuszcz, a potem weź sobie, czego pragnie twoja dusza, wtedy on mówił: Nic z tego! Daj teraz! A jeśli nie dasz, zabiorę siłą.
17 Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
Tak więc grzech tych sług był bardzo wielki przed PANEM, gdyż ludzie lekceważyli ofiary PANA.
18 Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
Samuel zaś służył przed PANEM jako chłopiec, przepasany lnianym efodem.
19 Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
A jego matka robiła mu mały płaszcz i przynosiła mu [go] co roku, gdy chodziła z mężem składać doroczną ofiarę.
20 Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
I Heli błogosławił Elkanie i jego żonie, mówiąc: Niech PAN da ci potomstwo z tej kobiety za uproszonego, którego oddała PANU. I wracali do swojego domu.
21 Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
I PAN nawiedził Annę, a ona poczęła i urodziła trzech synów i dwie córki. A chłopiec Samuel dorastał przed PANEM.
22 Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Heli zaś bardzo się zestarzał i usłyszał o wszystkim, co jego synowie czynili wobec całego Izraela, oraz o tym, że obcowali z kobietami, które się zbierały przy wejściu do Namiotu Zgromadzenia.
23 Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
I powiedział do nich: Dlaczego czynicie takie rzeczy? Słyszę o waszych złych czynach od całego ludu.
24 Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
Nie, moi synowie, gdyż niedobra to wieść, którą słyszę. Doprowadzacie lud PANA do przestępstwa.
25 Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
Jeśli człowiek zgrzeszy przeciw człowiekowi, będzie go sądzić sędzia, ale jeśli człowiek zgrzeszy przeciw PANU, któż się za nim wstawi? Oni jednak nie posłuchali głosu swego ojca, bo PAN chciał ich zabić.
26 Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
A chłopiec Samuel rósł i podobał się zarówno PANU, jak i ludziom.
27 Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
Potem przyszedł mąż Boży do Heliego i powiedział mu: Tak mówi PAN: Czy nie objawiłem się wyraźnie domowi twego ojca, gdy byli w Egipcie w domu faraona?
28 Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
I wybrałem go sobie spośród wszystkich pokoleń Izraela na kapłana, aby składał ofiary na moim ołtarzu, palił kadzidło i nosił efod przede mną. Dałem też domowi twego ojca wszystkie ofiary ogniowe od synów Izraela.
29 Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
Dlaczego podeptaliście moją ofiarę krwawą i pokarmową, które rozkazałem [składać] w przybytku? Dlaczego [bardziej] uczciłeś swoich synów ode mnie, abyście utuczyli się z pierwocin wszystkich ofiar pokarmowych Izraela, mojego ludu?
30 “Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
Dlatego PAN, Bóg Izraela, mówi: Wprawdzie powiedziałem: Twój dom i dom twego ojca będzie chodzić przede mną na wieki, ale teraz PAN mówi: Nie będzie tak! Tych bowiem, którzy mnie czczą, ja będę czcić, a ci, którzy mną gardzą, będą wzgardzeni.
31 Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
Oto nadchodzą dni, gdy odetnę twe ramię i ramię domu twego ojca, aby już nie było starca w twoim domu;
32 Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
I zobaczysz przeciwnika w przybytku, wśród całego szczęścia, którego Bóg udzieli Izraelowi, i nie będzie starca w twoim domu po wszystkie dni.
33 Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
Lecz nie wytracę od swego ołtarza każdego człowieka spośród ciebie, aby trapić twe oczy i ścisnąć boleścią twoją duszę. Cały przyrost twego domu umrze w sile wieku.
34 “‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
A to będzie znakiem, który przyjdzie na twoich dwóch synów, Chofniego i Pinchasa: obydwaj umrą tego samego dnia.
35 Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
I wzbudzę sobie kapłana wiernego, [który] będzie postępował według mego serca i mojej myśli. Zbuduję mu trwały dom, a on będzie chodził przed moim pomazańcem po wszystkie dni.
36 Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”
I stanie się tak, że ktokolwiek pozostanie w twoim domu, ten przyjdzie i pokłoni mu się za srebrną monetę i za kawałek chleba, mówiąc: Dopuść mnie, proszę, do jednego z [urzędów] kapłańskich, abym mógł jeść kawałek chleba.

< 1 Samueli 2 >