< 1 Samueli 2 >

1 Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
And Anna worschipide, and seide, Myn herte fulli ioiede in the Lord, and myn horn is reisid in my God; my mouth is alargid on myn enemyes, for Y was glad in thin helthe.
2 “Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
Noon is hooli as the Lord is; `for noon other is, outakun thee, and noon is strong as oure God.
3 “Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
Nyle ye multiplie to speke hiye thingis, and haue glorie; elde thingis go awey fro youre mouth; for God is Lord of kunnyngis, and thouytis ben maad redi to hym.
4 “Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
The bouwe of strong men is ouercomun, and sijk men ben gird with strengthe.
5 Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
Men fillid bifore settiden hem silf to hire for looues, and hungri men ben fillid; while the bareyn womman childide ful manye, and sche that hadde many sones, was sijke.
6 “Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol h7585)
The Lord sleeth, and quikeneth; he ledith forth to hellis, and bryngith ayen. (Sheol h7585)
7 Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
The Lord makith pore, and makith riche; he makith low, and reisith.
8 Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
He reisith a nedi man fro poudur, and `he reisith a pore man fro dryt, that he sitte with princes, and holde the seete of glorie; for the endis of erthe ben of the Lord, and he hath set the world on tho.
9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
He schal kepe `the feet of hise seyntis, and wickid men schulen be stille to gidere in derknessis; for a man schal not be maad strong in his owne strengthe.
10 Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
Aduersaries of the Lord schulen drede hym, and in heuenes he schal thundre on hem; the Lord schal deme the endis of erthe, and he schal yyue lordschip to his kyng, and he schal enhaunse the horn, `that is, power, of his Crist.
11 Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
And Helcana yede in to Ramatha, in to his hows; forsothe the child was seruaunt in the siyt of the Lord bifor the face of Ely the preest.
12 Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
Forsothe the sones of Hely weren sones of Belial,
13 Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
and knewen not the Lord, nether the office of preestis to the puple; but who euer hadde offrid sacrifice, the child of the preest cam, while the fleischis weren in sething, and he hadde a fleischhook with thre teeth in his hond;
14 Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
and he sente it in to the `grete vessel of stoon, ethir in to the caudrun, ethir in to the pot, ethir in to the panne; and what euer thing the fleischhook reiside, the preest took to hym silf; so thei diden to al Israel of men comynge in to Silo.
15 Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
Yhe bifor that `the sones of Hely brenten the ynnere fatnesse, the `child of the preest cam, and seyde to the offerere, Yyue `thou fleisch to me, that Y sethe to the preest; for Y schal not take of thee sodun fleisch, but raw.
16 Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
And `the offrere seide to hym, The ynnere fatnesse be brent first to day bi the custom, and take thou to thee hou myche euer thi soule desirith. Whiche answeride, and seide to hym, Nay, for thou schalt yyue now; ellis Y schal take bi violence.
17 Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
Therfor the synne of the children was ful greuouse bifor the Lord; for thei withdrowen men fro the `sacrifice of the Lord.
18 Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
`Forsothe Samuel, a child gird with a lynnun clooth, mynystride bifor the face of the Lord.
19 Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
And his moder made to hym a litil coote, which sche brouyte in daies ordeyned, and stiede with hir hosebonde, that he schulde offre a solempne offryng, and his auow.
20 Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
And Heli blesside Helcana and his wijf; and Heli seide `to hym, The Lord yelde to thee seed of this womman, for the yifte which thou hast youe to the Lord. And thei yeden in to her place.
21 Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
Therfor the Lord visitide Anna, and sche conseyuede, and childide thre sones and twei douytris. And the child Samuel was `magnyfied at the Lord.
22 Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Forsothe Hely was ful eld, and he herde alle `thingis whiche hise sones diden in al Israel, and hou thei slepten with wymmen, that awaitiden at the dore of the tabernacle.
23 Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
And he seide to hem, Whi doen ye siche thingis, the worste thingis whiche Y here of al the puple?
24 Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
Nyle ye, my sones; it is not good fame, which Y here, that ye make the `puple of the Lord to do trespas.
25 Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
If a man synneth ayens a man, God may be plesid to him; forsothe if a man synneth ayens the Lord, who schal preye for hym? And thei herden not the vois of her fadir, for God wolde sle hem.
26 Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
Forsothe the child Samuel profitide, and encreessyde, and pleside bothe God and men.
27 Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
Sotheli a man of God cam to Hely, and seide to hym, The Lord seith these thingis, Whether Y was not schewid apertli to the hows of thi fadir, whanne he was in Egipt, in the hows of Farao?
28 Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
And Y chees hym of alle lynagis of Israel `in to preest to me, that he schulde stie to myn auter, and schulde brenne encense to me, and that he schulde bere bifor me preestis cloth; and Y yaf to `the hows of thi fadir alle thingis of the sacrifices of the sones of Israel.
29 Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
Whi hast thou cast awey with the heele my sacrifice, and my yiftis, whiche Y comaundide to be offrid in the temple; and thou onouridst more thi sones than me, that ye eeten the principal partis of ech sacrifice of `Israel, my puple?
30 “Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
Therfor the Lord God of Israel seith these thingis, Y spekynge spak, that thin hows and `the hows of thi fadir schulde mynystre in my siyt til in to with outen ende; `now forsothe the Lord seith, Fer be this fro me; but who euere onourith me, Y schal glorifie hym; forsothe thei that dispisen me, schulen be vnnoble.
31 Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
Lo! daies comen, and Y schal kitte awei thin arm, and the arm of the hows of thi fadir, that an eld man be not in thin hows.
32 Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
And thou schalt se thin enemy in the temple, in alle prosperitees of Israel; and an eld man schal not be in thin hows in alle daies.
33 Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
Netheles Y schal not outerli take awei of thee a man fro myn auter, but that thin iyen faile, and thi soule faile; and greet part of thin hows schal die, whanne it schal come to mannus age.
34 “‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
Forsothe this schal be signe, that schal come to thi twei sones Ophym and Fynees, bothe schulen die in o dai.
35 Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
And Y schal reise to me a feithful preest, that schal do bi myn herte and my soule; and Y schal bilde to hym a feithful hows, and he schal go bifore my Crist in alle daies.
36 Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”
Forsothe it schal come, that who euer dwellith in thin hows, he come that `me preie for him, and that he offre a peny of siluer, and a cake of breed, and seie, Y biseche, suffre thou me to o `part of the preest, that Y ete a mussel of breed.

< 1 Samueli 2 >