< 1 Samueli 18 >

1 Davide atatha kuyankhula ndi Sauli, mtima wa Yonatani unagwirizana ndi mtima wa Davide, ndipo iye ankamukonda Davide monga momwe ankadzikondera yekha.
I kad svrši razgovor sa Saulom, duša Jonatanova prionu za dušu Davidovu, i Jonatan ga zapazi kao svoju dušu.
2 Choncho Sauli anamusunga Davideyo kuyambira tsiku limenelo ndipo sanamulole kuti abwerere ku nyumba ya abambo ake.
I uze ga Saul taj dan, i ne dade mu da se vrati kuæi oca svojega.
3 Ndipo Yonatani anapanga pangano ndi Davide chifukwa ankamukonda monga momwe ankadzikondera.
I Jonatan uèini vjeru s Davidom, jer ga ljubljaše kao svoju dušu.
4 Yonatani anavula mkanjo umene anavala ndipo anamupatsa Davide pamodzi ndi zovala za nkhondo, lupanga, uta ndi lamba.
I skide Jonatan sa sebe plašt, koji nošaše, i dade ga Davidu, i odijelo svoje i maè svoj i luk svoj i pojas svoj.
5 Davide ankapita kulikonse kumene Sauli ankamutuma kuti apite kukamenya nkhondo, ndipo ankapambana. Choncho Sauli anamupatsa udindo woyangʼanira gulu lankhondo. Ichi chinakondweretsa anthu onse ngakhalenso atsogoleri a nkhondo a Sauli.
I iðaše David na što ga god Saul pošiljaše, i bijaše sreæan, i postavi ga Saul nad vojnicima, i omilje svemu narodu, pa i slugama Saulovijem.
6 Anthu akubwerera kwawo Davide atapha Mfilisiti uja, amayi anatuluka mʼmizinda yonse ya Israeli, akuyimba ndi kuvina kukachingamira mfumu Sauli. Ankayimba ndi kuvina mokondwa, kwinaku ngʼoma ndi zitoliro zikulira.
A kad se vraæahu, i kad se David vraæaše ubivši Filistejina, izlaziše žene iz svakoga grada Izrailjeva pjevajuæi i igrajuæi na susret caru Saulu, s bubnjima i s veseljem i guslama.
7 Amayiwo ankalandizana nyimbo mokondwera namati: “Sauli wapha 1,000, Koma Davide wapha miyandamiyanda.”
I otpijevajuæi žene jedne drugima uza svirke govorahu: Saul zgubi svoju tisuæu, ali David svojih deset tisuæa.
8 Koma Sauli anapsa mtima kwambiri ndipo mawu amenewa anamuyipira. Iye anati, “Iwo amuwerengera Davide miyandamiyanda, koma ine 1,000 okha. Nanga chatsalanso nʼchiyani kuti atenge? Si ufumu basi?”
I razgnjevi se Saul vrlo, i ne biše mu po volji te rijeèi, i reèe: Davidu dadoše deset tisuæa, a meni dadoše tisuæu; još mu samo carstvo treba.
9 Ndipo kuyambira tsiku limeneli Sauli ankamuchitira nsanje Davide.
I od toga dana Saul gledaše poprijeko Davida.
10 Mmawa mwake mzimu woyipa uja unabwera mwamphamvu pa Sauli. Sauli anayamba kubwebweta mʼnyumba mwake. Davide ankamuyimbira zeze monga nthawi zonse. Sauli anali ndi mkondo mʼdzanja lake.
A sjutradan napade Saula zli duh Božji, te prorokovaše u kuæi, a David mu udaraše rukom svojom u gusle kao prije: a Saulu u ruci bješe koplje.
11 Tsono anawuponya mkondowo, namati mu mtima mwake, “Ndimubaya Davide ndi kumukhomera ku khoma.” Koma Davide anawulewa kawiri konse.
I Saul baci koplje govoreæi: da prikujem Davida za zid. Ali mu se David izmaèe dva puta.
12 Pambuyo pake Sauli amamuopa Davide chifukwa Yehova anali ndi Davideyo, nʼkumusiya Sauli.
I Saula bješe strah od Davida, jer Gospod bješe s njim, a od Saula bješe otstupio.
13 Kotero Sauli anamuchotsa Davide pamaso pake ndi kumuyika kukhala mtsogoleri wa ankhondo 1,000. Choncho Davide ankapita ndi kubwera akutsogolera ankhondowa.
Zato ga ukloni Saul od sebe, i postavi ga tisuænikom; i on odlažaše i dolažaše pred narodom.
14 Davide ankapambana kwambiri pa chilichonse chimene amachita chifukwa Yehova anali naye.
I David bijaše sreæan u svemu što èinjaše, jer Gospod bijaše s njim.
15 Sauli ataona momwe Davide ankapambanira, iye anamuopa kwambiri.
A Saul videæi da je veoma sreæan, bojaše ga se.
16 Koma Aisraeli onse ndi anthu a Yuda ankamukonda Davide chifukwa ankawatsogolera pa nkhondo zawo.
A sav Izrailj i Juda ljubljaše Davida, jer on odlažaše i dolažaše pred njima.
17 Tsiku lina Sauli anawuza Davide kuti, “Nayu Merabi mwana wanga wamkazi wamkulu. Ine ndakupatsa kuti umukwatire. Koma unditumikire molimba mtima pomenya nkhondo za Yehova.” Poteropo Sauli ankanena kuti, “Ndisamuphe ndi manja angawa koma aphedwe ndi Afilisti!”
I reèe Saul Davidu: evo, kæer svoju stariju Meravu daæu ti za ženu, samo mi budi hrabar i vodi ratove Gospodnje. Jer Saul govoraše: neæu da se digne moja ruka na nj, nego Filistejska ruka neka se digne na nj.
18 Ndipo Davide anati kwa Sauli, “Ine ndine yani, ndipo abale anga kapena banja la abambo anga ndife yani mʼdziko la Israeli kuti ndikhale mpongozi wa mfumu?”
A David reèe Saulu: ko sam ja i kakav je život moj ili dom oca mojega u Izrailju, da budem zet carev?
19 Koma pa nthawi yoti Merabi mwana wa Sauli akwatiwe ndi Davide, Sauli anamupereka kwa Adrieli wa ku Mehola kuti amukwatire.
A kad doðe vrijeme da Meravu kæer Saulovu dadu Davidu, dadoše je Adrilu Meolaæaninu za ženu.
20 Koma Mikala mwana wamkazi wa Sauli anamukonda Davide ndipo Sauli atamva za zimenezi, anakondwera.
Ali Davida ljubljaše Mihala kæi Saulova; a kad to javiše Saulu, bi mu po volji.
21 Sauli ankaganiza kuti, “Ndimupatse amukwatire kuti akhale ngati msampha kwa Davideyo, ndipo adzaphedwe ndi Afilisti.” Choncho Sauli anawuza Davide kachiwiri, “Tsopano udzakhala mkamwini wanga.”
I reèe Saul: daæu mu je da mu bude zamka i da se diže na nj ruka Filistejska. A Davidu reèe Saul: biæeš mi danas zet s drugom.
22 Sauli analamulanso nduna zake kuti, “Muyankhuleni Davide mwamseri ndi kumuwuza kuti, ‘Taona, mfumu imakondwera nawe, ndipo nduna zake zonse zimakukonda. Tsono ukhale mkamwini wa mfumu.’”
I zapovjedi Saul slugama svojim: recite Davidu tajno i govorite: gle, omilio si caru, i sve sluge njegove ljube te; budi sada zet carev.
23 Iwo anakamuwuza Davide mawu amenewa, koma Davide anati, “Kodi inu mukuganiza kuti ndi chinthu chapafupi kukhala mpongozi wa mfumu? Ine ndine wosauka ndiponso wosatchuka.”
I sluge Saulove rekoše te rijeèi Davidu, a David reèe: mislite li da je lako biti zet carev? ta ja sam siromah i mali èovjek.
24 Nduna za Sauli zinamuwuza zonse zimene anayankha Davide.
I Saulu javiše ovo sluge njegove govoreæi: ovako reèe David.
25 Sauli anayankha kuti, “Kamuwuzeni Davide kuti, ‘Mfumu sikufuna malowolo a mtundu wina uliwonse koma timakungu ta msonga za mavalo a Afilisti 100 kuti ilipsire adani ake.’” Maganizo a Sauli anali akuti Davide aphedwe ndi Afilisti.
A Saul reèe: ovako recite Davidu: ne traži car uzdarja, nego sto okrajaka Filistejskih, da se car osveti svojim neprijateljima. A Saul mišljaše kako bi David pao u ruke Filistejima.
26 Nduna za Saulizo zitamuwuza Davide zimenezi, anakondwera kuti akhale mpongozi wa mfumu. Koma nthawi imene anapatsidwa isanathe,
I sluge njegove kazaše Davidu te rijeèi, i Davidu bi po volji da postane carev zet. I vrijeme se još ne navrši.
27 Davide ndi anyamata ake anapita ndi kukapha Afilisti 200. Iye anabwera ndi timakungu tija natipereka tonse kwa mfumu kuti akhale mpongozi wa mfumu. Kotero Sauli anapereka mwana wake wamkazi, Mikala, kwa Davide kuti amukwatire.
A David usta i otide sa svojim ljudima, i pobi dvjesta Filisteja. I donese David okrajke njihove, i dadoše ih na broj caru da bi postao carev zet. I Saul mu dade za ženu Mihalu kæer svoju.
28 Sauli atazindikira kuti Yehova anali ndi Davide ndiponso kuti mwana wake Mikala amamukonda Davide,
I Saul vidje i pozna da je Gospod sa Davidom; i Mihala kæi Saulova ljubljaše ga.
29 iye anapitirirabe kumuopa Davide ndi kumadana naye moyo wake wonse.
A Saul se još veæma poboja Davida; i bijaše Saul jednako neprijatelj Davidu.
30 Nthawi zonse pamene atsogoleri a Afilisti ankatuluka kukamenya nkhondo, Davide ankapambana kuposa nduna zonse za Sauli. Choncho dzina lake linatchuka kwambiri.
A knezovi Filistejski udarahu; i kad god udarahu, David bijaše sreæniji od svijeh sluga Saulovijeh, i ime se njegovo vrlo proslavi.

< 1 Samueli 18 >