< 1 Samueli 13 >

1 Sauli analowa ufumu ali ndi zaka makumi atatu, ndipo analamulira Israeli kwa zaka 42.
Saul was a child of o yeer whanne he bigan to regne; forsothe he regnede on Israel twei yeer.
2 Nthawi ina Sauli anasankha Aisraeli 3,000. Mwa iwowa, 2,000 anali ndi Sauliyo ku Mikimasi ndi ku dziko la mapiri ku Beteli, ndipo 1,000 anali ndi Yonatani ku Gibeya ku Benjamini. Anthu ena onse otsala anawabweza kwawo.
And Saul chees to hym thre thousynde of Israel, and twei thousynde weren with Saul in Machynas, in the hil of Bethel; forsothe a thousynde weren with Jonathas in Gabaath of Beniamyn; sotheli he sente ayen the tother puple ech man in to `hise tabernaclis.
3 Yonatani anakantha mkulu wa ankhondo wa Afilisti ku Geba, ndipo Afilisti anamva kuti Aheberi awukira. Tsono Sauli anawuza amithenga kuti alize lipenga mʼdziko lonse la Israeli.
And Jonathas smoot the stacioun of Filisteis, that was in Gabaa. And whanne Filisteis hadden herd this, Saul sownede with a clarioun in al the lond, and seide, Ebreys here.
4 Choncho Aisraeli onse anamva kuti Sauli wakantha mkulu wa ankhondo Wachifilisiti ndi kuti Afilisti anayipidwa nawo Aisraeli. Ndiye anthu anayitanidwa kuti abwere kwa Sauli ku Giligala.
And al Israel herde siche a fame, Saul smoot the stacioun of Filisteis; and Israel reiside hym silf ayens Filisteis; therfor the puple criede after Saul in Galgala.
5 Tsono Afilisti anasonkhana kuti amenyane ndi Aisraeli. Iwo anali ndi magaleta 3,000, okwera pa akavalo 2,000 ndiponso asilikali kuchuluka kwake ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Iwo anapita ndi kukamanga misasa yawo ku Mikimasi, kummawa kwa Beti-Aveni.
And Filisteis weren gaderid to fiyte ayens Israel; `of Filisteis weren thretti thousynde of charis, and sixe thousynde of knyytis, and the tother comyn puple, as grauel `which is ful myche in the brynke of the see; and thei stieden, and settiden tentis in Machynas, at the eest of Bethauen.
6 Pamene Aisraeli anaona kuti anali pamavuto akulu, poti anali atapanikizidwa kwambiri, anabisala mʼmapanga, mʼmaenje, mʼmatanthwe, mʼmakwalala ndi mʼzitsime.
And whanne men of Israel hadden seyn this, that thei weren set in streiytnesse, for the puple was turmentid, thei hidden hem silf in dennes, and in priuey places, and in stonys, and in dychis, and in cisternes.
7 Ahebri ena anawoloka Yorodani mpaka kukafika ku dziko la Gadi ndi ku Giliyadi. Koma Sauli anakhalabe ku Giligala ndipo ankhondo onse amene anali naye anali njenjenje ndi mantha.
Sotheli Ebreis passiden Jordan in to the lond of Gad and of Galaad. And whanne Saul was yit in Galgala, al the puple was aferd that suede hym.
8 Saulo anadikirira masiku asanu ndi awiri, monga mwa nthawi imene ananena Samueli. Koma Samueli sanabwere ku Giligala, ndipo anthu anayamba kumuthawa Sauli uja.
And seuene daies he abood Samuel bi couenaunt, and Samuel cam not in to Galgala; and the puple yede a wei fro Saul.
9 Kotero iye anati, “Bwera nayoni nsembe yopsereza ndi nsembe ya chiyanjano.” Ndipo Sauli anapereka nsembe yopsereza.
Therfor Saul seide, Brynge ye to me brent sacrifice, and pesible sacrifices; and he offride brent sacrifice.
10 Atangomaliza kupereka nsembe, anangoona Samueli watulukira ndipo Sauli anapita kukamulonjera.
And whanne he hadde endid offrynge brent sacrifice, lo! Samuel cam; and Saul yede out ayens hym, to greete Samuel.
11 Samueli anafunsa kuti, “Nʼchiyani chimene wachita?” Sauli anayankha kuti, “Nditaona kuti anthu ayamba kundithawa, ndi kuti inu simunabwere pa nthawi munanena ija, ndiponso kuti Afilisti akusonkhana ku Mikimasi,
And Samuel spak to hym, What hast thou do? Saul answeride, For Y siy that the puple yede awei fro me, and thou camest not bi the daies of couenaunt; certis Filisteis weren gaderid in Machynas;
12 ndinati, ‘Tsopano Afilisti abwera kudzandithira nkhondo ku Giligala kuno, chonsecho sindinapemphe Yehova kuti andikomere mtima.’ Motero ndinakakamizika kupereka nsembe yopsereza.”
Y seide, Now Filisteis schulen come doun to me in to Galgala, and Y haue not plesyd the face of the Lord; Y was compellid bi nede, and Y offryde brent sacrifice to the Lord.
13 Samueli anati, “Mwachita zopusa. Simunatsate zimene Yehova Mulungu wanu anakulamulani kuti muchite. Mukanazitsata, Yehova akanawukhazikitsa ufumu wanu mu Israeli mpaka kalekale.
And Samuel seide to Saul, Thou hast do folili, and thou `keptist not the heestis of thi Lord God, whiche he comaundide to thee; and if thou haddist not do this thing, riyt now the Lord hadde maad redi thi rewme on Israel with outen ende;
14 Koma tsopano ufumu wanu sudzakhalitsa. Yehova wapeza munthu wapamtima pake ndipo wamusankha kukhala mtsogoleri wa anthu ake chifukwa inu simunasunge malamulo a Yehova.”
but thi rewme schal not rise ferthere. The Lord hath souyt a man to hym silf after his herte; and the Lord comaundide to hym, that he schulde be duyk on his puple, for thou keptist not tho thingis whiche the Lord comaundide.
15 Kenaka Samueli anachoka ku Giligala ndi kupita ku Gibeyati ku dziko la Benjamini. Saulo anawerenga anthu amene anali naye ndipo analipo 600.
Forsothe Samuel roos, and stiede fro Galgala in to Gabaa of Beniamyn; and the `residue puplis stieden after Saul ayens the puple which fouyten ayens hem; and thei camen fro Galgala in to Gabaa, in the hil of Beniamyn. And Saul noumbride the puple, that weren foundun with hym as sixe hundrid men.
16 Sauli ndi mwana wake Yonatani pamodzi ndi asilikali amene anali naye aja amakhala ku Geba ku dziko la Benjamini. Koma Afilisti anamanga misasa yawo ku Mikimasi.
And Saul, and Jonathas his sone, and the puple that was foundun with hem, was in Gabaa of Beniamyn; forsothe Filisteis saten togidere in Machynas.
17 Ankhondo a Afilisti anatuluka mʼmisasa yawo mʼmagulu atatu. Gulu lina linapita ku Ofiri ku dziko la Suwala.
And thre cumpanyes yeden out of the `castels of Filisteis to take prey; o cumpany yede ayens the weie of Effraym to the lond of Saul;
18 Gulu lina linalunjika ku Beti-Horoni, ndipo gulu lachitatu linalunjika ku malire oyangʼanana ndi chigwa cha Zeboimu cha ku chipululu.
sothely an other cumpeny entride bi the weie of Bethoron; forsothe the thridde cumpenye turnede it silf to the weie of the terme in the lond of Sabaa; and that terme neiyeth to the valey of Seboym ayens the deseert.
19 Nthawi imeneyo nʼkuti mulibe osula zitsulo mʼdziko lonse la Israeli, pakuti Afilisti anati, “Tisawalole Aheberi kudzipangira okha malupanga kapena mikondo!”
Forsothe `no smyyth of yrun was foundun in al the lond of Israel; for Filisteis `weren war, ether eschewiden, lest perauenture Ebreis maden a swerd ether a spere.
20 Kotero Aisraeli onse amapita kwa Afilisti kukanoletsa mapulawo, makasu, nkhwangwa ndi zikwakwa zawo.
Therfor al Israel yede doun to Filisteis, that ech man schulde scharpe his schar, and picoise, and ax, `and sarpe;
21 Mtengo wonolera mapulawo ndi makasu unali zigawo ziwiri za sekeli, mtengo wonolera zisonga ndi nkhwangwa unali gawo limodzi la Sekeli.
`and so alle egis weren bluntid `of scharris, and of picoisis, and of `forkis of thre teeth, and of axis, `til to a pricke to be amendid.
22 Motero tsiku la nkhondolo panalibe lupanga kapena mkondo mʼdzanja la aliyense amene anatsatira Saulo ndi Yonatani. Koma Saulo ndi Yonatani, iwo okha ndiwo anali ndi zida.
And whanne the dai of batel cam, no swerd and spere was foundun in the hond of al the puple that was with Saul and Jonathas, outakun Saul, and Jonathas his sone.
23 Tsono gulu lina lankhondo la Chifilisti linapita kukalonda mpata wa Mikimasi.
Forsothe the stacioun of Filisteis yede out, that it schulde passe in to Machynas.

< 1 Samueli 13 >