< 1 Samueli 10 >

1 Ndipo Samueli anatenga botolo la mafuta nathira mafutawo pa mutu wa Sauli ndipo anapsompsona nati, “Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake, Aisraeli. Iwe udzalamulira anthu a Yehova ndiponso udzawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo owazungulira. Chizindikiro chakuti Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake ndi ichi:
Tada Samuilo uze uljanicu, i izli mu ulje na glavu, pa ga cjelova, i reèe mu: eto, nije li te pomazao Gospod nad našljedstvom svojim da mu budeš voð?
2 Ukachoka pano lero lino, udzakumana ndi amuna awiri kufupi ndi manda a Rakele ku Zeliza mʼmalire mwa dziko la Benjamini ndipo adzakuwuza kuti, ‘Abulu amene munkafunafuna aja apezeka. Ndipo tsopano abambo ako asiya kuganiza za abulu ndipo akudera nkhawa za iwe.’ Iwo akufunsa kuti, ‘Kodi ndidzachita chiyani mmene mwana wanga sakuoneka?’”
Kad otideš danas od mene, naæi æeš dva èovjeka kod groba Rahiljina u kraju Venijaminovu u Selsi, koji æe ti reæi: našle su se magarice, koje si pošao da tražiš, i evo otac tvoj ne mareæi za magarice zabrinuo se za vas govoreæi: šta æu èiniti poradi sina svojega?
3 “Ndipo udzapyola pamenepo ndi kufika ku mtengo wa thundu wa ku Tabori. Kumeneko udzakumana ndi anthu atatu akupita kukapereka nsembe ku Nyumba ya Mulungu ku Beteli. Mmodzi adzakhala atanyamula ana ambuzi atatu, wina atanyamula malofu atatu a buledi, ndi winayo atanyamula thumba la vinyo.
I otišavši odande dalje kad doðeš u ravnicu Tavorsku, srešæe te ondje tri èovjeka iduæi k Bogu u Vetilj, noseæi jedan tri jareta, a drugi noseæi tri hljeba, a treæi noseæi mješinu vina.
4 Adzakupatsa moni ndi kukupatsa malofu awiri a buledi. Iwe udzalandire bulediyo.
Pa æe te upitati za zdravlje, i daæe ti dva hljeba, koje primi iz ruku njihovijeh.
5 “Pambuyo pake, udzafike ku Gibeyati-Elohimu, kumene kuli gulu la ankhondo la Afilisti. Pamene ukuyandikira mzindawo, udzakumana ndi gulu la aneneri akutsika kuchokera ku phiri, akuyimba zeze, ngʼoma, zitoliro ndi pangwe, ndiponso akulosera.
Potom æeš doæi na hum Božji, gdje je straža Filistejska, i kad uðeš u grad, srešæe te gomila proroka slazeæi s gore, a pred njima psaltiri i bubnji i svirale i gusle; i oni æe prorokovati.
6 Kenaka Mzimu wa Yehova udzabwera pa iwe ndi mphamvu, ndipo udzayamba kulosera nawo pamodzi. Ndipo udzasinthika kukhala munthu wina.
I siæi æe na te duh Gospodnji, te æeš prorokovati s njima, i postaæeš drugi èovjek.
7 Zizindikiro izi zikakachitika, dzachite chilichonse manja ako angathe kuchita, pakuti Mulungu ali nawe.
I kad ti doðu ti znaci, èini što ti doðe na ruku, jer je Bog s tobom.
8 “Tsono tsogola kupita ku Giligala. Ine ndidzabwera ndithu kudzapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Koma ukandidikire masiku asanu ndi awiri mpaka ine nditabwera kuti ndidzakuwuze zomwe udzachite.”
Potom æeš otiæi prije mene u Galgal, i gle, ja æu doæi k tebi da prinesem žrtve paljenice i da prinesem žrtve zahvalne. Sedam dana èekaj dokle doðem k tebi i kažem ti šta æeš èiniti.
9 Sauli akutembenuka kusiyana ndi Samueli, Mulungu anasintha mtima wa Sauli, ndipo zinthu zonsezi zinakwaniritsidwa tsiku lomwelo.
I kad se okrete da ide od Samuila, Bog mu dade drugo srce; i svi se oni znaci zbiše onaj dan.
10 Atafika ku Gibeya, anakumana ndi gulu la aneneri. Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwamphamvu, nayamba kulosa nawo.
I kad doðoše na hum, gle, srete ga gomila proroka, i doðe na nj duh Božji, i prorokova meðu njima.
11 Pamene onse amene ankamudziwa kale anamuona akulosera pamodzi ndi aneneri, anafunsana wina ndi mnzake. “Kodi nʼchiyani chachitika ndi mwana wa Kisi? Kodi Sauli alinso mʼgulu la aneneri?”
I kad ga vidješe svi koji ga poznavahu od preðe gdje prorokuje s prorocima, rekoše jedan drugome: šta to bi od sina Kisova? eda li je i Saul meðu prorocima?
12 Munthu wina wa kumeneko anayankha kuti, “Nanga enawa abambo awo ndani?” Kotero kunayambika mwambi wakuti, “Kodi Saulinso ali mʼgulu la aneneri?”
A jedan odande odgovori i reèe: ko li im je otac? Otuda posta prièa: eda li je i Saul meðu prorocima?
13 Sauli atasiya kuloserako, anapita ku kachisi ku phiri.
I prestavši prorokovati doðe na goru.
14 Tsono amalume ake a Sauli anamufunsa ndi mnyamata wake kuti, “Munapita kuti?” Iye anayakha, “Timakafunafuna abulu koma titaona kuti sakupezeka, tinapita kwa Samueli.”
A stric Saulov reèe njemu i momku njegovu: kuda ste išli? A on odgovori: da tražimo magarice; i kad vidjesmo da ih nigdje nema, otidosmo k Samuilu.
15 Amalume ake a Sauli anati, “Chonde, ndifotokozereniko zimene Samueli wakuwuzani.”
A stric Saulov reèe: kaži mi šta vam je rekao Samuilo?
16 Sauli anati, “Iye anatitsimikizira kuti abulu anapezeka.” Koma sanawawuze amalume akewo za nkhani ija ya ufumu imene Samueli anamuwuza.
A Saul reèe stricu svojemu: kazao nam je da su se našle magarice. Ali mu ne reèe za carstvo što mu je kazao Samuilo.
17 Samueli anayitana Aisraeli onse kuti asonkhane pamaso pa Yehova ku Mizipa.
A Samuilo sazva narod u Mispu ka Gospodu.
18 Ndipo anawuza Aisraeli onse kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi kukupulumutsani mʼdzanja la Igupto ndi mʼdzanja la mafumu onse amene ankakuzunzani.’
I reèe sinovima Izrailjevijem: ovako veli Gospod Bog Izrailjev: ja izvedoh Izrailja iz Misira, i izbavih vas iz ruku Misirskih i iz ruku svijeh carstava koja vas muèahu.
19 Koma lero mwamukana Mulungu wanu amene amakupulumutsani mʼmavuto anu onse ndi mʼzowawa zanu. Ndipo mukuti, ‘Ayi, koma mutipatse mfumu yotilamulira.’ Tsopanotu sonkhanani pamaso pa Yehova mwa mafuko ndi mabanja anu.”
A vi danas odbaciste Boga svojega, koji vas sam izbavlja od svijeh zala vaših i nevolja vaših, i rekoste mu: postavi cara nad nama. Sada dakle stanite pred Gospodom po plemenima svojim i po tisuæama svojim.
20 Samueli atasonkhanitsa mafuko onse a Israeli, fuko la Benjamini linasankhidwa.
I privede Samuilo sva plemena Izrailjeva, i pade na pleme Venijaminovo.
21 Anasonkhanitsa fuko la Benjamini banja ndi banja. Pomaliza anasonkhanitsa banja la Matiri mmodzimmodzi ndipo Sauli mwana wa Kisi anasankhidwa. Koma atamufunafuna, sanamupeze.
Potom privede pleme Venijaminovo po porodicama njegovijem, i pade na porodicu Matrijevu; potom pade na Saula sina Kisova. I tražiše ga, ali se ne naðe.
22 Tsono anthu anafunsanso kwa Yehova kuti, “Kodi munthuyu wabwera kale kuno?” Ndipo Yehova anayankha kuti, “Inde wabisala pakati pa katundu.”
Tada opet upitaše Gospoda: hoæe li još doæi ovamo taj èovjek? A Gospod reèe: eto sakrio se za prtljagom.
23 Iwo anathamanga ndi kukamutenga kumeneko. Atayimirira pakati pa anthu anapezeka kuti anali wamtali kuposa anthu ena mwakuti ankamulekeza mʼmapewa.
Tada otrèaše, i dovedoše ga odande. I stade usred naroda, i bijaše glavom viši od svega naroda.
24 Samueli anafunsa anthu onse kuti, “Kodi mukumuona munthu amene Yehova wasankha? Palibe wofanana naye pakati pa anthu onse.” Kenaka anthu onse anafuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
I reèe Samuilo svemu narodu: vidite li koga je izabrao Gospod da niko nije kao on u svemu narodu? I sav narod povika i reèe: da živi car!
25 Samueli anafotokozera anthu ntchito ndi udindo wa mfumu. Pambuyo pake analemba mʼbuku zonse zokhudza ntchito ndi udindo wa mfumu, ndipo bukulo analiyika pamaso pa Yehova. Kenaka Samueli analola aliyense kuti abwerere kupita kwawo.
Tada Samuilo kaza narodu prava carska i napisa u knjigu, i metnu je pred Gospodom. Potom Samuilo raspusti narod da ide svak svojoj kuæi.
26 Sauli anapitanso ku mudzi kwawo ku Gibeya, pamodzi ndi anthu amphamvu amene Mulungu anawafewetsa mitima.
I Saul takoðer otide svojoj kuæi u Gavaju, i s njim otidoše vojnici, kojima Bog taknu srca.
27 Koma anthu ena achabechabe anati, “Kodi munthu uyu angathe bwanji kutipulumutsa?” Iwo anayamba kumunyoza Sauliyo, ndipo sankamupatsa ngakhale mphatso. Koma iye sanalabadireko.
A ljudi nevaljali rekoše: taj li æe nas izbaviti? I prezirahu ga, niti mu donesoše dara. Ali se on uèini kao da nije èuo.

< 1 Samueli 10 >