< 1 Samueli 10 >

1 Ndipo Samueli anatenga botolo la mafuta nathira mafutawo pa mutu wa Sauli ndipo anapsompsona nati, “Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake, Aisraeli. Iwe udzalamulira anthu a Yehova ndiponso udzawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo owazungulira. Chizindikiro chakuti Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake ndi ichi:
Forsothe Samuel took `a vessel of oyle, and schedde out on the heed of Saul, and kisside hym, and seide, Lo! the Lord hath anoyntid thee in to prince on hys eritage; and thou schalt delyuere his puple fro the hond of his enemyes, that ben `in his cumpas. And this a tokene to thee, that the Lord hath anoyntid thee in to prince;
2 Ukachoka pano lero lino, udzakumana ndi amuna awiri kufupi ndi manda a Rakele ku Zeliza mʼmalire mwa dziko la Benjamini ndipo adzakuwuza kuti, ‘Abulu amene munkafunafuna aja apezeka. Ndipo tsopano abambo ako asiya kuganiza za abulu ndipo akudera nkhawa za iwe.’ Iwo akufunsa kuti, ‘Kodi ndidzachita chiyani mmene mwana wanga sakuoneka?’”
whanne thou schalt go fro me to day, thou schalt fynde twei men bisidis `the sepulcre of Rachel, in `the endis of Beniamyn, in myddai, clensynge grete dichis; and thei schulen seie to thee, The femel assis ben foundun, whiche thou yedist to seke; and while the assis ben lefte, thi fadir is bisy for you, and seith, What schal Y do of my sone?
3 “Ndipo udzapyola pamenepo ndi kufika ku mtengo wa thundu wa ku Tabori. Kumeneko udzakumana ndi anthu atatu akupita kukapereka nsembe ku Nyumba ya Mulungu ku Beteli. Mmodzi adzakhala atanyamula ana ambuzi atatu, wina atanyamula malofu atatu a buledi, ndi winayo atanyamula thumba la vinyo.
And whanne thou hast go fro thennus, and hast passid ferthere, and hast come to the ook of Tabor, thre men, stiynge to God in to Bethel, schulen fynde thee there, o man berynge thre kydis, and another man berynge thre kakis of breed, and an other man berynge a galoun of wyn.
4 Adzakupatsa moni ndi kukupatsa malofu awiri a buledi. Iwe udzalandire bulediyo.
And whanne thei han gret thee, thei schulen yyue to thee twei loues, and thou schalt take of `the hond of hem.
5 “Pambuyo pake, udzafike ku Gibeyati-Elohimu, kumene kuli gulu la ankhondo la Afilisti. Pamene ukuyandikira mzindawo, udzakumana ndi gulu la aneneri akutsika kuchokera ku phiri, akuyimba zeze, ngʼoma, zitoliro ndi pangwe, ndiponso akulosera.
After these thingis thou schalt come in to the `hil of the Lord, where is the stondyng, that is, forselet, of Filisteis; and whanne thou schalt entre in to the citee, there thou schalt haue metynge thee the flok of prophetis comynge doun fro the hiy place, and a sautree, and tympane, and pipe, and harpe bifor hem, and hem prophesiynge.
6 Kenaka Mzimu wa Yehova udzabwera pa iwe ndi mphamvu, ndipo udzayamba kulosera nawo pamodzi. Ndipo udzasinthika kukhala munthu wina.
And the Spirit of the Lord schal skippe in to thee, and thou schalt prophecie with hem, and thou schalt be chaungid in to another man.
7 Zizindikiro izi zikakachitika, dzachite chilichonse manja ako angathe kuchita, pakuti Mulungu ali nawe.
Therfor whanne alle thesse signes bifallen to thee, do thou, what euer thingis thin hond fyndith, `that is, dispose thee to regne comelili and myytily, for the Lord is with thee.
8 “Tsono tsogola kupita ku Giligala. Ine ndidzabwera ndithu kudzapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Koma ukandidikire masiku asanu ndi awiri mpaka ine nditabwera kuti ndidzakuwuze zomwe udzachite.”
And thou schalt go doun bifor me in to Galgala; for Y schal come doun to thee, that thou offre an offryng, and offre pesible sacrifices; bi seuene daies thou schalt abide, til I come to thee, and shewe to thee what thou schal do.
9 Sauli akutembenuka kusiyana ndi Samueli, Mulungu anasintha mtima wa Sauli, ndipo zinthu zonsezi zinakwaniritsidwa tsiku lomwelo.
Therfor whanne Saul hadde turnede awei his schuldre to go fro Samuel, God chaungide another herte to Saul, and alle these signes camen in that dai.
10 Atafika ku Gibeya, anakumana ndi gulu la aneneri. Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwamphamvu, nayamba kulosa nawo.
And thei camen to the forseid hil, and lo! a cumpeny of prophetis metynge hym; and the Spirit of the Lord `scippide on hym, and he propheciede in the myddis of hem.
11 Pamene onse amene ankamudziwa kale anamuona akulosera pamodzi ndi aneneri, anafunsana wina ndi mnzake. “Kodi nʼchiyani chachitika ndi mwana wa Kisi? Kodi Sauli alinso mʼgulu la aneneri?”
Sotheli alle men, that knewen hym yisterdai and the thrid dai ago, sien that he was with the prophetis, and that he prophesiede, and thei seiden togidere, What thing bifelde to the sone of Cys? Whether also Saul is among prophetis?
12 Munthu wina wa kumeneko anayankha kuti, “Nanga enawa abambo awo ndani?” Kotero kunayambika mwambi wakuti, “Kodi Saulinso ali mʼgulu la aneneri?”
And o man answeride to another man, and seide, And who is `his fadir? Therfor it was turned in to a prouerbe, Whether also Saul is among prophetis?
13 Sauli atasiya kuloserako, anapita ku kachisi ku phiri.
Forsothe Saul ceside to prophesie, and he cam to an hiy place.
14 Tsono amalume ake a Sauli anamufunsa ndi mnyamata wake kuti, “Munapita kuti?” Iye anayakha, “Timakafunafuna abulu koma titaona kuti sakupezeka, tinapita kwa Samueli.”
And the brothir of `the fadir of Saul seide to hym, and to his child, Whidur yeden ye? And thei answeriden, To seke the femal assis; and whanne we founden `not thoo, we camen to Samuel.
15 Amalume ake a Sauli anati, “Chonde, ndifotokozereniko zimene Samueli wakuwuzani.”
And the brother of his fadir seide to hym, Schewe thou to me what Samuel seide to thee.
16 Sauli anati, “Iye anatitsimikizira kuti abulu anapezeka.” Koma sanawawuze amalume akewo za nkhani ija ya ufumu imene Samueli anamuwuza.
And Saul seide to `the brother of hys fadir, He schewide to vs, that the femal assis weren foundun. Sotheli Saul schewide not to hym of the word of rewme, `which word Samuel spak to hym.
17 Samueli anayitana Aisraeli onse kuti asonkhane pamaso pa Yehova ku Mizipa.
And Samuel clepide togidere the puple to the Lord in Masphat;
18 Ndipo anawuza Aisraeli onse kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi kukupulumutsani mʼdzanja la Igupto ndi mʼdzanja la mafumu onse amene ankakuzunzani.’
and he seide to the sones of Israel, The Lord God of Israel seith these thingis, Y ledde Israel out of the lond of Egipt, and Y delyuerede you fro the hond of Egipcians, and fro the hond of alle kyngis that turmentiden you.
19 Koma lero mwamukana Mulungu wanu amene amakupulumutsani mʼmavuto anu onse ndi mʼzowawa zanu. Ndipo mukuti, ‘Ayi, koma mutipatse mfumu yotilamulira.’ Tsopanotu sonkhanani pamaso pa Yehova mwa mafuko ndi mabanja anu.”
Forsothe to day ye han caste awei youre Lord God, which aloone sauyde you fro alle youre yuelis and tribulaciouns; and ye seiden, Nay, but ordeyne thou a kyng on vs. Now therfor stonde ye bifor the Lord bi youre lynagis, and bi meynees.
20 Samueli atasonkhanitsa mafuko onse a Israeli, fuko la Benjamini linasankhidwa.
And Samuel settide to gidere alle the lynages of Israel, and lot felde on the lynage of Beniamyn.
21 Anasonkhanitsa fuko la Benjamini banja ndi banja. Pomaliza anasonkhanitsa banja la Matiri mmodzimmodzi ndipo Sauli mwana wa Kisi anasankhidwa. Koma atamufunafuna, sanamupeze.
And he settide togidere the lynage of Beniamyn, and the meynees therof; and lot felde on the meynees of Mathri, and it cam `til to Saul, the son of Cys. Therfor thei souyten hym, and he was not foundun there.
22 Tsono anthu anafunsanso kwa Yehova kuti, “Kodi munthuyu wabwera kale kuno?” Ndipo Yehova anayankha kuti, “Inde wabisala pakati pa katundu.”
And aftir these thingis thei counseliden the Lord, whether Saul schulde come thidur. And the Lord answeride, Lo! he is hid at hoom.
23 Iwo anathamanga ndi kukamutenga kumeneko. Atayimirira pakati pa anthu anapezeka kuti anali wamtali kuposa anthu ena mwakuti ankamulekeza mʼmapewa.
Therfor thei runnen, and token hym fro thennus; and he stood in the myddil of the puple, and was hiyere than al the puple fro the schulder and `aboue.
24 Samueli anafunsa anthu onse kuti, “Kodi mukumuona munthu amene Yehova wasankha? Palibe wofanana naye pakati pa anthu onse.” Kenaka anthu onse anafuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
And Samuel seide to al the puple, Certis ye seen whom the Lord hath chose; for noon in al the puple is lijk hym. And al the puple cryede, and seide, Lyue the kyng!
25 Samueli anafotokozera anthu ntchito ndi udindo wa mfumu. Pambuyo pake analemba mʼbuku zonse zokhudza ntchito ndi udindo wa mfumu, ndipo bukulo analiyika pamaso pa Yehova. Kenaka Samueli analola aliyense kuti abwerere kupita kwawo.
Forsothe Samuel spak to the puple the lawe of rewme, and wroot in a book, and puttide vp bifor the Lord. And Samuel dilyuerede al the puple, ech man in to his hows;
26 Sauli anapitanso ku mudzi kwawo ku Gibeya, pamodzi ndi anthu amphamvu amene Mulungu anawafewetsa mitima.
but also Saul yede in to his hous in to Gabaath; and the part of the oost yede with hym, whose hertis God hadde touchid.
27 Koma anthu ena achabechabe anati, “Kodi munthu uyu angathe bwanji kutipulumutsa?” Iwo anayamba kumunyoza Sauliyo, ndipo sankamupatsa ngakhale mphatso. Koma iye sanalabadireko.
Forsothe the sones of Belyal seiden, Whether this man may saue vs? And thei dispisiden hym, and brouyten not yiftis, `that is, preisyngis, to him; forsothe he `dissymelide hym to here.

< 1 Samueli 10 >