< 1 Mafumu 5 >

1 Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
I Hiram car Tirski posla sluge svoje k Solomunu èuvši da su ga pomazali za cara na mjesto oca njegova, jer Hiram ljubljaše Davida svagda.
2 Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
A Solomun posla ka Hiramu i poruèi mu:
3 “Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
Ti znaš da David otac moj nije mogao sagraditi doma imenu Gospoda Boga svojega od ratova kojima ga opkoliše, dokle ih Gospod ne položi pod noge njegove.
4 Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
A sada Gospod Bog moj dao mi je mir otsvuda, nemam nijednoga neprijatelja ni zle smetnje.
5 Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
Zato, evo, velim da sagradim dom imenu Gospoda Boga svojega, kao što je rekao Gospod Davidu ocu mojemu govoreæi: sin tvoj, kojega æu posaditi mjesto tebe na prijesto tvoj, on æe sagraditi dom imenu mojemu.
6 “Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
Zato zapovjedi sada neka mi nasijeku drva kedrovijeh na Livanu, a sluge æe moje biti sa slugama tvojim, a platu slugama tvojim daæu ti kako god reèeš; jer ti znaš da u nas nema ljudi koji umiju sjeæi drva kao Sidonci.
7 Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
I kad Hiram èu rijeèi Solomunove, obradova se veoma i reèe: da je blagosloven Gospod danas, koji dade Davidu mudra sina nad onijem narodom velikim.
8 Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
I posla Hiram Solomunu, i poruèi: èuo sam èega radi si slao k meni; ja æu uèiniti svu volju tvoju za drva kedrova i za drva jelova.
9 Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
Moje æe sluge snijeti s Livana na more, i ja æu ih povezati u splavove i spustiti morem do mjesta koje mi kažeš, i ondje æu razvezati, pa ih nosi; a ti æeš uèiniti moju volju i dati hranu èeljadi mojoj.
10 Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
I tako davaše Hiram Solomunu drva kedrova i drva jelova, koliko mu bješe volja.
11 ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
A Solomun davaše Hiramu dvadeset tisuæa kora pšenice za hranu èeljadi njegovoj, i dvadeset kora ulja cijeðenoga; toliko davaše Solomun Hiramu svake godine.
12 Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
I Gospod dade mudrost Solomunu kako mu bješe obrekao, i bješe mir izmeðu Hirama i Solomuna, i uhvatiše vjeru meðu sobom.
13 Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
I odredi Solomun ljude iz svega Izrailja, i bi odreðenijeh trideset tisuæa ljudi.
14 Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
I slaše ih na Livan po deset tisuæa svakoga mjeseca naizmjence; jedan mjesec bijahu na Livanu, a dva mjeseca kod kuæa svojih. A Adoniram bješe nad ovijem poslenicima.
15 Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
I imaše Solomun sedamdeset tisuæa nosilaca i osamdeset tisuæa tesaèa u planini,
16 ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
Osim nastojnika Solomunovijeh, koji bijahu nad tijem poslom, tri tisuæe i trista, koji upravljahu narodom koji poslovaše taj posao.
17 Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
I zapovjedi car da snose veliko kamenje, skupocjeno kamenje za temelj domu, tesano kamenje.
18 Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.
I tesahu poslenici Solomunovi i poslenici Hiramovi i Givleji, i pripravljahu drvo i kamenje da se zida dom.

< 1 Mafumu 5 >