< 1 Mafumu 3 >

1 Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu.
I Salomon spowinowacił się z faraonem, królem Egiptu. Pojął bowiem [za żonę] córkę faraona i przyprowadził ją do miasta Dawida, zanim skończył budować swój dom i dom PANA oraz mur dokoła Jerozolimy.
2 Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba.
Lud jednak składał ofiary na wyżynach, dlatego że do tego czasu nie został [jeszcze] zbudowany dom dla imienia PANA.
3 Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.
I Salomon miłował PANA, postępując zgodnie z przykazaniami Dawida, swego ojca, tylko że składał ofiary i spalał kadzidło na wyżynach.
4 Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe.
Król udał się więc do Gibeonu, aby tam złożyć ofiary, bo [tam] była wielka wyżyna. Na tym ołtarzu Salomon złożył tysiąc ofiar całopalnych.
5 Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
W Gibeonie PAN ukazał się Salomonowi w nocy we śnie. Bóg powiedział: Proś o to, co mam ci dać.
6 Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.
Salomon odpowiedział: Ty okazałeś swemu słudze Dawidowi, memu ojcu, wielkie miłosierdzie, gdyż postępował przed tobą w prawdzie, sprawiedliwości i prawości serca przy tobie. I zachowałeś dla niego tę wielką łaskę, że dałeś mu syna, który zasiadł na jego tronie, jak [to się dzieje] dziś.
7 “Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi.
Teraz więc, o PANIE, mój Boże, ty ustanowiłeś swego sługę królem w miejsce Dawida, mego ojca, a ja jestem małym dzieckiem i nie wiem, jak wyruszać ani jak wracać.
8 Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga.
Twój sługa jest wśród twego ludu, który wybrałeś, ludu wielkiego, którego z powodu wielkiej liczby nie można zliczyć ani spisać.
9 Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
Daj więc swemu słudze serce rozumne, aby mógł sądzić twój lud i rozróżniać między dobrem a złem. Któż bowiem może sądzić ten twój tak wielki lud?
10 Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi.
I spodobało się to PANU, że Salomon o to poprosił.
11 Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo,
Wtedy Bóg powiedział do niego: Ponieważ poprosiłeś o to, a nie poprosiłeś dla siebie o długie życie ani nie poprosiłeś dla siebie o bogactwo, ani też nie poprosiłeś o wytracenie swoich wrogów, ale poprosiłeś dla siebie o rozum dla rozróżnienia w [sprawach] sądowych;
12 Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako.
Oto uczyniłem według twoich słów: Dałem ci serce mądre i rozumne, tak że podobnego tobie nie było przed tobą ani po tobie nie powstanie nikt jak ty.
13 Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe.
Dam ci także to, o co nie prosiłeś, a więc bogactwo i sławę, tak że wśród królów nie będzie nikogo równego tobie po wszystkie twoje dni.
14 Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.”
A jeśli będziesz chodził moimi drogami, przestrzegając moich ustaw i przykazań, jak postępował Dawid, twój ojciec, wtedy przedłużę twoje dni.
15 Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto. Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.
A gdy Salomon obudził się, [zrozumiał, że] to był sen. Wrócił więc do Jerozolimy, stanął przed arką przymierza PANA i złożył całopalenia i ofiary pojednawcze oraz wyprawił ucztę wszystkim swoim sługom.
16 Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake.
Wtedy przyszły do króla dwie kobiety, nierządnice, i stanęły przed nim.
17 Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu.
Jedna z kobiet powiedziała: Proszę cię, mój panie, ja i ta kobieta mieszkamy w jednym domu. Ja urodziłam przy niej w tym domu.
18 Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.
A trzeciego dnia po moim porodzie urodziła również ta kobieta. I byłyśmy razem, nie było z nami nikogo innego w domu; tylko my dwie [byłyśmy] w tym domu.
19 “Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera.
W nocy umarł syn tej kobiety, ponieważ przygniotła go.
20 Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga.
Wstała więc o północy, wzięła mego syna od mego boku, gdy twoja służąca spała, i położyła go na swym łonie, a swego zmarłego syna położyła na moim łonie.
21 Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”
Kiedy wstałam rano, aby nakarmić swego syna piersią, oto był martwy. Lecz gdy przyjrzałam się rano, zobaczyłam, że to nie był mój syn, którego urodziłam.
22 Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.” Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.
Wtedy druga kobieta odezwała się: Nie! Moim synem [jest] ten żywy, a twoim synem [jest] ten umarły. Lecz tamta powiedziała: Nie! Twoim synem jest ten umarły, a moim synem jest ten żywy. I tak się spierały przed królem.
23 Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’”
Wtedy król powiedział: Ta mówi: Ten żywy jest moim synem, a twoim synem ten umarły, a tamta mówi: Nie tak – twoim synem jest ten umarły, a moim synem jest ten żywy.
24 Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu.
Król powiedział więc: Przynieście mi miecz. I przyniesiono miecz przed króla.
25 Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”
Wtedy król powiedział: Rozetnijcie żywe dziecko na dwoje i dajcie połowę jednej i połowę drugiej.
26 Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!” Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”
Lecz kobieta, do której należał żywy syn, zdjęta litością nad swoim synem, powiedziała do króla: Proszę, mój panie, dajcie jej to żywe dziecko, tylko nie zabijajcie go! Lecz druga powiedziała: Niech nie będzie ani moje, ani twoje, rozetnijcie [je].
27 Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”
Wtedy król odpowiedział: Dajcie jej żywe dziecko, a nie zabijajcie go. Ona jest jego matką.
28 Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.
A kiedy cały lud Izraela usłyszał o tym wyroku, który wydał król, bał się króla. Widzieli bowiem, że jest w nim mądrość Boża do sprawowania sądu.

< 1 Mafumu 3 >