< 1 Mafumu 21 >

1 Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya.
A poslije ovijeh stvari dogodi se: Navutej Jezraeljanin imaše vinograd u Jezraelu do dvora Ahava cara Samarijskoga.
2 Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”
I reèe Ahav Navuteju govoreæi: daj mi svoj vinograd da naèinim od njega vrt za zelje, jer je blizu do dvora mojega; a ja æu ti dati za nj bolji vinograd, ili ako voliš, daæu ti u novcu šta vrijedi.
3 Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”
A Navutej reèe Ahavu: saèuvaj Bože da bih ti dao našljedstvo otaca svojih.
4 Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.
Tada Ahav doðe kuæi zlovoljan i ljutit radi rijeèi koju mu reèe Navutej Jezraeljanin govoreæi: ne dam ti našljedstva otaca svojih. I leže na postelju svoju, i okrenu lice svoje na stranu, i ne jede hljeba.
5 Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”
Tada doðe k njemu Jezavelja žena njegova i reèe mu: zašto je duša tvoja zlovoljna te ne jedeš hljeba?
6 Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’”
A on joj reèe: jer govorih s Navutejem Jezraeljaninom i rekoh mu: daj mi vinograd svoj za novce, ili ako voliš, daæu ti drugi vinograd za taj. A on reèe: ne dam ti svoga vinograda.
7 Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”
Tada mu reèe Jezavelja žena njegova: ti li si car nad Izrailjem? Ustani, jedi hljeba i budi veseo. Ja æu ti dati vinograd Navuteja Jezraeljanina.
8 Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake.
I napisa knjigu na ime Ahavovo, i zapeèati je peèatom njegovijem i posla knjigu starješinama i glavarima koji bijahu u gradu njegovu, koji nastavahu s Navutejem.
9 Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti: “Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
A u knjizi napisa ovo: oglasite post, i posadite Navuteja meðu glavare narodne.
10 Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”
I postavite dva nevaljala èovjeka prema njemu, pa neka zasvjedoèe na nj govoreæi: hulio si na Boga i na cara. Tada ga izvedite i zaspite kamenjem, da pogine.
11 Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera.
I uèiniše ljudi onoga grada, starješine i glavari, koji življahu u gradu njegovu, kako im zapovjedi Jezavelja, kako bijaše napisano u knjizi koju im posla.
12 Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
I oglasiše post, i posadiše Navuteja meðu glavare narodne.
13 Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha.
I doðoše dva nevaljala èovjeka, i sjedoše prema njemu; i svjedoèiše na Navuteja ti nevaljali ljudi pred narodom govoreæi: Navutej je hulio na Boga i na cara. I izvedoše ga iza grada, i zasuše ga kamenjem, te pogibe.
14 Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”
Potom poslaše k Jezavelji i poruèiše joj: zasut je kamenjem Navutej, i poginuo je.
15 Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.”
A kad Jezavelja èu da je Navutej zasut kamenjem i poginuo, reèe Ahavu Jezavelja: ustani, uzmi vinograd Navuteja Jezraeljanina, kojega ti ne htje dati za novce, jer Navutej nije živ nego je umro.
16 Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.
A kad èu Ahav da je umro Navutej, usta i poðe u vinograd Navuteja Jezraeljanina da ga uzme.
17 Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
Ali doðe rijeè Gospodnja k Iliji Tesviæaninu govoreæi:
18 “Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake.
Ustani, izidi na susret Ahavu caru Izrailjevu, koji sjedi u Samariji; eno ga u vinogradu Navutejevu, kuda je otišao da ga uzme.
19 Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’”
I reci mu i kaži: ovako veli Gospod: nijesi li ubio i nijesi li prisvojio? Pa mu kaži i reci: ovako veli Gospod: kako psi lizaše krv Navutejevu, tako æe lizati psi i tvoju krv.
20 Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!” Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova.
A Ahav reèe Iliji: naðe li me, neprijatelju moj? A on reèe: naðoh, jer si se prodao da èiniš što je zlo pred Gospodom.
21 Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu.
Evo, pustiæu zlo na te, i uzeæu natražje tvoje, i istrijebiæu Ahavu i ono što uza zid mokri, i uhvaæenoga i ostavljenoga u Izrailju.
22 Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’
I uèiniæu s domom tvojim kao s domom Jerovoama sina Navatova i kao s domom Vase sina Ahijina, što si me gnjevio i što si naveo na grijeh Izrailja.
23 “Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’
Takoðe i za Jezavelju reèe Gospod govoreæi: psi æe izjesti Jezavelju ispod zidova Jezraelskih.
24 “Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”
Ko Ahavov pogine u gradu izješæe ga psi, a ko pogine u polju izješæe ga ptice nebeske.
25 (Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli.
I ne bi takoga kao Ahav, koji se prodade da èini što je zlo pred Gospodom, jer ga podgovaraše žena njegova Jezavelja.
26 Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).
I poèini vrlo grdna djela iduæi za gadnim bogovima sasvijem kao što èiniše Amoreji, koje izagna Gospod ispred sinova Izrailjevijeh.
27 Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.
A kad Ahav èu te rijeèi, razdrije haljine svoje, i priveza kostrijet oko tijela svojega, i pošæaše, i spavaše u kostrijeti, i hoðaše polagano.
28 Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
I doðe rijeè Gospodnja Iliji Tesviæaninu govoreæi:
29 “Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”
Jesi li vidio kako se Ahav ponizio preda mnom? Zato što se tako ponizio preda mnom, neæu pustiti onoga zla za njegova života; nego za sina njegova pustiæu ono zlo na dom njegov.

< 1 Mafumu 21 >