< 1 Mafumu 15 >

1 Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
In the eighteenth year of King Jeroboam son of Nebat, Abijah began to reign over Judah.
2 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
He ruled for three years in Jerusalem. His mother's name was Maacah. She was the daughter of Abishalom.
3 Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
He walked in all the sins that his father had committed before his time; his heart was not devoted to Yahweh his God as the heart of David, his ancestor, had been.
4 Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
Nevertheless, for David's sake, Yahweh his God gave him a lamp in Jerusalem by raising up his son after him in order to strengthen Jerusalem.
5 pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
God did this because David had done what was right in his eyes; for all the days of his life, he had not turned away from anything that he commanded him, except only in the matter of Uriah the Hittite.
6 Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
Now there was war between Rehoboam and Jeroboam all the days of Abijah's life.
7 Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
As for the other matters of Abijah, all that he did, are they not written in the book of the events of the kings of Judah? There was war between Abijah and Jeroboam.
8 Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Abijah slept with his ancestors, and they buried him in the city of David. Asa his son became king in his place.
9 Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
In the twentieth year of Jeroboam king of Israel, Asa began to reign over Judah.
10 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
He ruled forty-one years in Jerusalem. His grandmother's name was Maacah, the daughter of Abishalom.
11 Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
Asa did what was right in the eyes of Yahweh, as David, his ancestor, had done.
12 Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
He expelled the cultic prostitutes from the land and removed all the idols that his ancestors had made.
13 Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
He also removed Maacah, his grandmother, from being queen, because she had made a disgusting figure out of an Asherah pole. Asa cut down the disgusting figure and burned it at the Kidron Valley.
14 Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
But the high places were not taken away. Nevertheless, Asa's heart was completely devoted to Yahweh all his days.
15 Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
He brought into the house of Yahweh the things that were set apart by his father, and his own things that had been set apart that were made of silver and gold, and vessels.
16 Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
There was war between Asa and Baasha king of Israel, all their days.
17 Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
Baasha king of Israel, acted aggressively against Judah and built up Ramah, so that he might not allow anyone to leave or enter into the land of Asa king of Judah.
18 Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
Then Asa took all the silver and gold left in the storerooms in the house of Yahweh, and the storerooms of the king's palace. He put it into the hands of his servants and sent it to Ben Hadad son of Tabrimmon son of Hezion, the king of Aram, who lived in Damascus. He said,
19 “Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
“Let there be a covenant between me and you, as there was between my father and your father. Look, I have sent to you a gift of silver and gold. Break your covenant with Baasha king of Israel, so that he may leave me alone.”
20 Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
Ben Hadad listened to King Asa and sent the commanders of his armies, and they attacked the cities of Israel. They attacked Ijon, Dan, Abel of Beth Maacah, and all Kinnereth, together with all the land of Naphtali.
21 Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
It came about that when Baasha heard this, he stopped building up Ramah and went back to Tirzah.
22 Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
Then King Asa made a proclamation to all Judah. No one was exempted. They carried away the stones and timbers of Ramah with which Baasha had been building up the city. Then King Asa used that building material to build up Geba of Benjamin and Mizpah.
23 Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
As for the other matters of Asa, all his might, all that he did, and the cities he built, are they not written in the book of the events of the kings of Judah? But during his old age he was diseased in his feet.
24 Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Then Asa slept with his ancestors and was buried with them in the city of David his father. Jehoshaphat his son became king in his place.
25 Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
Nadab son of Jeroboam began to reign over Israel in the second year of Asa king of Judah; he reigned over Israel two years.
26 Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
He did what was evil in the sight of Yahweh and walked in the way of his father, and in his own sin, by which he led Israel to sin.
27 Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
Baasha son of Ahijah, of the family of Issachar, conspired against Nadab; Baasha killed him down at Gibbethon, which belonged to the Philistines, for Nadab and all Israel were laying siege to Gibbethon.
28 Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
In the third year of Asa king of Judah, Baasha killed Nadab and became king in his place.
29 Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
As soon as he was king, Baasha killed all the family of Jeroboam. He left none of Jeroboam's descendants breathing; in this way he destroyed his royal line, just as Yahweh had spoken by his servant Ahijah the Shilonite,
30 chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
for the sins of Jeroboam which he committed and by which he led Israel to sin, because he provoked Yahweh, the God of Israel, to anger.
31 Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
As for the other matters concerning Nadab, and all that he did, are they not written in the book of the events of the kings of Israel?
32 Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
There was war between Asa and Baasha king of Israel all their days.
33 Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
In the third year of Asa king of Judah, Baasha son of Ahijah began to reign over all Israel in Tirzah and he reigned twenty-four years.
34 Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.
He did what was evil in the sight of Yahweh and walked in the way of Jeroboam and in his sin by which he led Israel to sin.

< 1 Mafumu 15 >