< 1 Mafumu 14 >

1 Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
U to vrijeme razbolje se Avija sin Jerovoamov.
2 ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
I Jerovoam reèe ženi svojoj: ustani i preobuci se da te ne poznadu da si žena Jerovoamova; pak idi u Silom. Eto, ondje je Ahija prorok, koji mi je kazao da æu biti car nad ovijem narodom.
3 Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
I ponesi deset hljebova i kolaèa i žban meda, pa otidi k njemu; on æe ti kazati šta æe biti od djeteta.
4 Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
I uèini tako žena Jerovoamova, i ustavši otide u Silom i uðe u kuæu Ahijinu. Ahija pak ne mogaše vidjeti, jer mu oèi bijahu potamnjele od starosti.
5 Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
Ali Gospod reèe Ahiji: eto ide žena Jerovoamova da te pita za sina svojega, jer je bolestan; ti joj kaži to i to; a ona kad doðe uèiniæe se da je druga.
6 Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
I Ahija èuvši šuštanje nogu njezinijeh kad uðe na vrata, reèe: hodi, ženo Jerovoamova; što se èiniš da si druga? Ja sam poslan k tebi da ti zlo kažem.
7 Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Idi, reci Jerovoamu: ovako veli Gospod Bog Izrailjev: što sam te podigao izmeðu naroda i postavio te voðem narodu svojemu Izrailju,
8 Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
I otrgav carstvo od doma Davidova dadoh tebi, a ti ne bi kao sluga moj David, koji je držao zapovijesti moje i hodio za mnom svijem srcem svojim èineæi samo što je pravo preda mnom;
9 Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
Nego si radio gore od svijeh koji biše prije tebe, i otišao si i naèinio sebi druge bogove i likove livene da bi me dražio, pa si me bacio za leða svoja;
10 “‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
Zato, evo, ja æu pustiti zlo na dom Jerovoamov, i istrijebiæu Jerovoamu i ono što mokri uza zid, i uhvaæenoga i ostavljenoga u Izrailju, i dom æu Jerovoamov omesti kao što se mete kao, da ga ne ostane ništa.
11 Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
Ko Jerovoamov pogine u gradu, izješæe ga psi, a ko pogine u polju, izješæe ga ptice nebeske; jer Gospod reèe.
12 “Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
A ti ustani, idi kuæi svojoj; i kad stupiš nogama svojim u grad, odmah æe umrijeti dijete.
13 Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
I sav æe Izrailj plakati za njim, i pogrepšæe ga; jer æe on sam od doma Jerovoamova doæi u grob, jer se na njemu samom u domu Jerovoamovu naðe nešto dobra pred Gospodom Bogom Izrailjevijem.
14 “Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
A Gospod æe podignuti sebi cara nad Izrailjem, koji æe istrijebiti dom Jerovoamov u onaj dan; da, šta? sad veæ.
15 Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
I udariæe Gospod Izrailja da æe se zaljuljati kao što se ljulja trska u vodi, i išèupaæe Izrailja iz ove dobre zemlje, koju je dao ocima njihovijem, i razasuæe ih daleko preko rijeke zato što naèiniše sebi lugove gnjeveæi Gospoda.
16 Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
I napustiæe Izrailja za grijehe Jerovoamove, kojima je griješio i na grijeh naveo Izrailja.
17 Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
Tada usta žena Jerovoamova, i otide i doðe u Tersu; i kad stupi na prag kuæni umrije dijete.
18 Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
I pogreboše ga, i sav Izrailj plaka za njim po rijeèi Gospodnjoj, koju reèe preko sluge svojega Ahije proroka.
19 Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
A ostala djela Jerovoamova, kako je vojevao i kako je carovao, eno zapisana su u dnevniku careva Izrailjevijeh.
20 Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
A carova Jerovoam dvadeset i dvije godine; i poèinu kod otaca svojih, a Nadav sin njegov zacari se na njegovo mjesto.
21 Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
A Rovoam sin Solomunov carovaše nad Judom; bješe Rovoamu èetrdeset i jedna godina kad poèe carovati, i carova sedamnaest godina u Jerusalimu gradu, koji izabra Gospod izmeðu svijeh plemena Izrailjevijeh da ondje namjesti ime svoje. Materi njegovoj bješe ime Nama Amonka.
22 Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
I Juda èinjaše što je zlo pred Gospodom; i grijesima svojim kojim griješahu dražiše ga veæma nego oci njihovi svijem što èiniše.
23 Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Jer i oni naèiniše sebi visine i stupove i lugove na svakom visokom humu i pod svakim zelenim drvetom.
24 Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
A bijaše i adžuvana u zemlji, i èinjahu sve gadove naroda koje bješe istjerao Gospod ispred sinova Izrailjevijeh.
25 Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
A pete godine carovanja Rovoamova doðe Sisak car Misirski na Jerusalim.
26 Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
I uze blago iz doma Gospodnjega i blago iz doma careva, sve to uze; i uze sve štitove zlatne koje naèini Solomun.
27 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
I na njihovo mjesto naèini car Rovoam štitove od mjedi, i predade ih starješinama nad stražarima, koji èuvahu vrata doma careva.
28 Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
I kad car iðaše u dom Gospodnji, nošahu ih stražari, a poslije ih opet ostavljahu u riznicu svoju.
29 Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
A ostala djela Rovoamova, i sve što je èinio, nije li zapisano u dnevniku careva Judinijeh?
30 Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
A bijaše rat izmeðu Rovoama i Jerovoama jednako.
31 Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
I poèinu Rovoam kod otaca svojih, i bi pogreben kod otaca svojih u gradu Davidovu. A ime materi njegovoj bješe Nama Amonka. A na mjesto njegovo zacari se Avijam sin njegov.

< 1 Mafumu 14 >