< 1 Mafumu 14 >

1 Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
W tym czasie zachorował Abiasz, syn Jeroboama.
2 ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
I Jeroboam powiedział do swojej żony: Wstań teraz, przebierz się, aby nie poznano, że jesteś żoną Jeroboama, i idź do Szilo. [Jest] tam prorok Achiasz, który mi powiedział, że będę królem nad tym ludem.
3 Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
Weź ze sobą dziesięć chlebów, placki i dzban miodu i idź do niego. On ci oznajmi, co się stanie z dzieckiem.
4 Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
Żona Jeroboama tak uczyniła. Wstała i poszła do Szilo, i przybyła do domu Achiasza. Lecz Achiasz już nie widział, gdyż jego oczy osłabły z powodu jego starości.
5 Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
A PAN powiedział do Achiasza: Oto żona Jeroboama nadchodzi, aby dowiedzieć się czegoś od ciebie o swoim synu, gdyż jest chory. Powiesz jej tak i tak, bo gdy wejdzie, będzie udawała kogoś innego.
6 Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
Gdy więc Achiasz usłyszał odgłos jej kroków, gdy wchodziła przez drzwi, powiedział: Wejdź, żono Jeroboama. Dlaczego udajesz kogoś innego? Zostałem posłany do ciebie z przykrą nowiną.
7 Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Idź, powiedz Jeroboamowi: Tak mówi PAN, Bóg Izraela: Mimo że wywyższyłem cię spośród ludu i ustanowiłem cię księciem nad moim ludem Izraelem;
8 Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
Wyrwałem domowi Dawida królestwo i dałem je tobie, ty jednak nie byłeś jak mój sługa Dawid, który przestrzegał moich przykazań i który chodził za mną całym swym sercem, czyniąc tylko to, co jest prawe w moich oczach;
9 Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
Lecz postępowałeś gorzej niż wszyscy, którzy byli przed tobą. Ty bowiem poszedłeś i uczyniłeś sobie obcych bogów i odlane posągi, aby mnie pobudzić do gniewu, mnie zaś rzuciłeś za plecy.
10 “‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
Dlatego sprowadzę nieszczęście na dom Jeroboama i wytępię z Jeroboama każdego, aż do najmniejszego szczenięcia, każdego więźnia i opuszczonego w Izraelu, i usunę ostatki domu Jeroboama, jak usuwa się gnój, aż do końca.
11 Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
Tego, kto [z domu] Jeroboama umrze w mieście, zjedzą psy, a tego, kto umrze na polu, zjedzą powietrzne ptaki, ponieważ tak powiedział PAN.
12 “Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
Ty zaś wstań i idź do swego domu, [a] gdy wejdziesz do miasta, dziecko umrze.
13 Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
I cały Izrael będzie je opłakiwał, i pogrzebie je, bo jedynie ono [z domu] Jeroboama zejdzie do grobu, gdyż w nim znalazło się [coś] dobrego względem PANA, Boga Izraela, w domu Jeroboama.
14 “Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
PAN zaś ustanowi sobie króla nad Izraelem, który wytępi dom Jeroboama w tym samym dniu. A co [mówię, wzbudzi]? I owszem, już [wzbudził].
15 Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
I PAN uderzy Izraela [tak], że [się zachwieje], jak się chwieje trzcina w wodzie, i wykorzeni Izraela z tej dobrej ziemi, którą dał ich ojcom, i rozproszy ich za rzeką za to, że uczynili sobie gaje, pobudzając PANA do gniewu.
16 Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
I tak porzuci on Izraela z powodu grzechów Jeroboama, który grzeszył i skłonił Izraela do grzechu.
17 Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
Wtedy żona Jeroboama wstała, wyruszyła i przybyła do Tirsy. Gdy przekroczyła próg domu, dziecko umarło.
18 Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
I pogrzebali je, i cały Izrael je opłakiwał zgodnie ze słowem PANA, które zapowiedział przez swego sługę, proroka Achiasza.
19 Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
Pozostałe zaś dzieje Jeroboama, jak walczył i jak królował, są zapisane w kronikach o królach Izraela.
20 Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
A czas, który królował Jeroboam, wynosił dwadzieścia dwa lata. Potem zasnął ze swoimi ojcami, a jego syn Nadab królował w jego miejsce.
21 Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
Roboam zaś, syn Salomona, królował w Judzie. Roboam [miał] czterdzieści jeden lat, gdy zaczął królować, a królował siedemnaście lat w Jerozolimie, w mieście, które PAN wybrał spośród wszystkich pokoleń Izraela, aby tam przebywało jego imię. Jego matka miała na imię Naama, [była] Ammonitką.
22 Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
I Juda czynił to, co złe w oczach PANA, i swoimi grzechami, które popełniali, pobudzali go do zazdrości bardziej niż to wszystko, co czynili ich ojcowie.
23 Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Pobudowali sobie bowiem wyżyny, posągi i gaje na każdym wysokim wzgórzu i pod każdym zielonym drzewem.
24 Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
Byli też w tej ziemi sodomici. Postępowali oni według wszystkich obrzydliwości pogan, których PAN wypędził sprzed synów Izraela.
25 Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
A w piątym roku króla Roboama, przeciw Jerozolimie nadciągnął Sziszak, król Egiptu.
26 Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
I zabrał skarby domu PANA oraz skarby domu królewskiego, zabrał wszystko. Zabrał też wszystkie złote tarcze, które wykonał Salomon.
27 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
Zamiast nich król Roboam wykonał spiżowe tarcze i powierzył je dowódcy straży przybocznej, która strzegła drzwi domu królewskiego.
28 Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
Ilekroć król wchodził do domu PANA, straż je nosiła, a potem odnosiła do wartowni.
29 Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
A pozostałe dzieje Roboama i wszystko, co czynił, czyż nie są zapisane w kronikach królów Judy?
30 Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
I trwała wojna między Roboamem a Jeroboamem po wszystkie dni.
31 Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
Potem Roboam zasnął ze swoimi ojcami i został pogrzebany z nimi w mieście Dawida. A jego matka miała na imię Naama, [była] Ammonitką. I jego syn Abijam królował w jego miejsce.

< 1 Mafumu 14 >