< 1 Mafumu 11 >

1 Komatu Mfumu Solomoni anakonda akazi ambiri achilendo ndipo kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, analinso ndi akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni, ndi Ahiti.
Ali car Solomun ljubljaše mnoge žene tuðinke osim kæeri Faraonove, Moavke, Amonke, Edomke, Sidonke i Hetejke,
2 Akazi amenewa anali ochokera ku mitundu ija imene Yehova anawuza Aisraeli kuti, “Simuyenera kudzakwatirana nawo amenewa, chifukwa ndithu, amenewa adzatembenuza mitima yanu kuti mutsatire milungu yawo.” Komabe Solomoni anawakonda kwambiri akazi amenewa.
Od onijeh naroda za koje bješe rekao Gospod sinovima Izrailjevijem: ne idite k njima i oni da ne dolaze k vama, jer æe zanijeti srce vaše za svojim bogovima. Za njih prionu Solomun ljubeæi ih.
3 Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa.
Te imaše žena carica sedam stotina, i tri stotine inoèa; i žene njegove zanesoše srce njegovo.
4 Solomoni atakalamba, akazi akewo anakopa mtima wake kuti atsatire milungu ina, ndipo sanatsatire Yehova Mulungu wake ndi mtima wodzipereka, monga unalili mtima wa Davide abambo ake.
I kad ostarje Solomun, žene zanesoše srce njegovo za tuðim bogovima; i srce njegovo ne bi cijelo prema Gospodu Bogu njegovu kao što je bilo srce Davida oca njegova.
5 Pakuti iye ankapembedza Asitoreti, mulungu wamkazi wa Asidoni, ndiponso Moleki mulungu wonyansa wa Aamoni.
I Solomun hoðaše za Astarotom, boginjom Sidonskom, i za Melhomom, gadom Amonskim.
6 Kotero Solomoni anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanatsatire Yehova kwathunthu monga anachitira Davide abambo ake.
I èinjaše Solomun što bješe zlo pred Gospodom, i ne hoðaše sasvijem za Gospodom kao David otac njegov.
7 Pa phiri la kummawa kwa Yerusalemu, anamanga malo opembedzerapo Kemosi, mulungu wonyansa wa Mowabu, ndiponso malo a Moleki, mulungu wonyansa wa Aamoni.
Tada sagradi Solomun visinu Hemosu, gadu Moavskom, na gori prema Jerusalimu, i Molohu gadu Amonskom.
8 Iye anamangiranso malo oterewa akazi ake onse achilendo, amene amafukiza lubani ndi kumapereka nsembe kwa milungu yawo.
Tako uèini svijem ženama tuðinkama, te kaðahu i prinošahu žrtve svojim bogovima.
9 Choncho Yehova anakwiyira Solomoni chifukwa mtima wake unatembenuka kuchoka kwa Yehova Mulungu wa Israeli, amene anamuonekera kawiri konse.
A Gospod se razgnjevi na Solomuna što se odvrati srce njegovo od Gospoda Boga Izrailjeva, koji mu se bješe javio dva puta.
10 Ngakhale kuti Yehova anamuletsa Solomoni kutsatira milungu ina, iyeyo sanamvere lamulo la Yehova.
I bješe mu zapovjedio da ne ide za drugim bogovima, a on ne održa što mu Gospod zapovjedi.
11 Pamenepo Yehova anati kwa Solomoni, “Popeza mtima wako ndi wotere ndipo sunasunge pangano langa ndi malamulo anga amene ndinakuwuza, ndithudi, Ine ndidzawugawa ufumuwu kuwuchotsa kwa iwe ndi kuwupereka kwa mmodzi mwa atumiki ako.
I reèe Gospod Solomunu: što se to naðe na tebi, i nijesi držao zavjeta mojega ni uredaba mojih, koje sam ti zapovjedio, zato æu otrgnuti od tebe carstvo i daæu ga sluzi tvojemu.
12 Koma chifukwa cha Davide abambo ako, sindidzachita zimenezi iwe uli moyo. Ndidzawugawa mʼdzanja la mwana wako.
Ali za tvojega vijeka neæu to uèiniti radi Davida oca tvojega; nego æu ga otrgnuti iz ruku sina tvojega,
13 Komabe sindidzamulanda ufumu wonse, koma ndidzamusiyira fuko limodzi chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso chifukwa cha Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha.”
Ali neæu otrgnuti svega carstva; jedno æu pleme dati sinu tvojemu radi Davida sluge svojega i radi Jerusalima, koji izabrah.
14 Ndipo Yehova anamuutsira Solomoni mdani, Hadadi Mwedomu, wochokera ku banja laufumu ku Edomu.
I podiže Gospod protivnika Solomunu, Adada Idumejca, koji bijaše od carskoga roda u Idumeji.
15 Kale pamene Davide ankachita nkhondo ndi Aedomu, Yowabu mkulu wa ankhondo, amene anapita kukakwirira Aisraeli akufa, anakantha amuna onse ku Edomu.
Jer kad David bijaše u Idumeji i Joav vojvoda doðe da pokopa pobijene, pobi sve muškinje u Idumeji.
16 Yowabu ndi Aisraeli onse anakhala kumeneko miyezi isanu ndi umodzi mpaka anawononga amuna onse a ku Edomu.
Jer Joav osta ondje šest mjeseca sa svijem Izrailjem dokle ne pobi sve muškinje u Idumeji.
17 Koma Hadadi akanali mwana anathawira ku Igupto pamodzi ndi akuluakulu ena a ku Edomu amene ankatumikira abambo ake.
Tada uteèe Adad s nekoliko Idumejaca sluga oca svojega, i otide u Misir; a Adad bješe tada dijete.
18 Iwo ananyamuka ku Midiya ndi kupita ku Parani. Ndipo anatenga amuna ena ku Paraniko, napita nawo ku Igupto, kwa Farao mfumu ya Igupto, amene anamupatsa nyumba, malo ndiponso chakudya.
I otišavši iz Madijama doðoše u Faran; i uzevši sa sobom ljudi iz Farana doðoše u Misir k Faraonu caru Misirskom, koji mu dade kuæu i odredi mu hranu, a dade mu i zemlje.
19 Farao anamukomera mtima Hadadi ndipo anamupatsa mkazi amene anali mngʼono wake wa Mfumukazi Tahipenesi.
I Adad naðe veliku milost u Faraona, te ga oženi sestrom žene svoje, sestrom carice Tahpenese.
20 Mngʼono wake wa Tahipenesi anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Genubati, amene analeredwa mʼnyumba yaufumu ndi Tahipenesi. Genubatiyo ankakhala limodzi ndi ana a Farao.
I sestra Tahpenesina rodi mu sina Genuvata, kojega othrani Tahpenesa u dvoru Faraonovu, i bješe Genuvat u dvoru Faraonovu meðu sinovima Faraonovijem.
21 Ali ku Iguptoko, Hadadi anamva kuti Davide ndi Yowabu anamwalira. Pamenepo Hadadi anati kwa Farao, “Loleni ndichoke kuti ndibwerere ku dziko la kwathu.”
A kad Adad èu u Misiru da je David poèinuo kod otaca svojih i da je umro Joav vojvoda, reèe Adad Faraonu: pusti me da idem u svoju zemlju.
22 Farao anafunsa kuti, “Kodi ukusowa chiyani kuno kuti ufune kubwerera ku dziko la kwanu?” Hadadi anayankha kuti, “Palibe chimene ndikusowa, koma loleni kuti ndichoke!”
A Faraon mu reèe: a šta ti je malo kod mene, te hoæeš da ideš u svoju zemlju? A on reèe: ništa; ali me pusti.
23 Ndipo Mulungu anawutsira Solomoni mdani wina, Rezoni mwana wa Eliada, amene anali atathawa mbuye wake, Hadadezeri mfumu ya ku Zoba.
Podiže mu Bog još jednoga protivnika, Rezona sina Elijadina, koji bješe pobjegao od gospodara svojega Adadezera cara Sovskoga.
24 Iye anasonkhanitsa anthu ndipo anali mtsogoleri wa anthu owukira pamene Davide anapha ankhondo a ku Zoba. Anthu owukirawa anapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko ndi kuyamba kulamulira.
I skupiv k sebi ljude posta starješina od èete kad ih David ubijaše; potom otišavši u Damask ostaše ondje i obladaše Damaskom.
25 Rezoni anali mdani wa Israeli pa masiku onse a Solomoni, kuwonjezera pa mavuto amene ankabweretsa Hadadi. Kotero Rezoni ankalamulira ku Aramu ndipo ankadana ndi Israeli.
I bješe protivnik Izrailjev svega vijeka Solomunova, i to osim zla koje èinjaše Adad; i mržaše na Izrailja carujuæi u Siriji.
26 Yeroboamu, mwana wa Nebati anawukiranso mfumu. Iye anali mmodzi mwa akuluakulu a Solomoni wa fuko la Efereimu, wa ku Zeredi, ndipo amayi ake anali Zeruya, mkazi wamasiye.
I Jerovoam sin Navatov Efraæanin iz Saride, èija mati bješe po imenu Seruja žena udovica, sluga Solomunov, podiže se na cara.
27 Nkhani ya kuwukira kwa Yeroboamu inali yotere: Solomoni anamanga malo a chitetezo a Milo ndipo anakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide, abambo ake.
A ovo bi uzrok zašto se podiže na cara: Solomun graðaše Milon i zaziðivaše prolom grada Davida oca svojega;
28 Tsono Yeroboamu anali munthu wamphamvu kwambiri ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo amadziwa kugwira ntchito bwino, anamuyika kukhala woyangʼanira anthu a ntchito onse a nyumba ya Yosefe.
A Jerovoam bijaše krjepak i hrabar; zato videæi Solomun mladiæa da nastaje za poslom postavi ga nad svijem dancima doma Josifova.
29 Tsiku lina Yeroboamu ali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, anakumana ndi mneneri Ahiya pa msewu, ndipo Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano. Awiriwo anali okha kuthengoko,
Pa u to vrijeme kad Jerovoam otide iz Jerusalima, naðe ga na putu Ahija Silomljanin prorok imajuæi na sebi novu haljinu, i bijahu njih dvojica sami u polju.
30 ndipo Ahiya anagwira mwinjiro watsopano umene anavala ndi kuwungʼamba zidutswa 12.
I Ahija uze novu haljinu koja bješe na njemu, i razdrije je na dvanaest komada.
31 Tsono iye anati kwa Yeroboamu, “Tenga zidutswa khumi, pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taona, Ine ndidzachotsa ufumu mʼdzanja la Solomoni ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
I reèe Jerovoamu: uzmi deset komada; jer ovako veli Gospod Bog Izrailjev: evo istrgnuæu carstvo iz ruke Solomunove, i daæu tebi deset plemena.
32 Koma chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso mzinda wa Yerusalemu, umene ndinawusankha pakati pa mafuko a Israeli, iye adzakhala ndi fuko limodzi lokha.
Samo æe jedno pleme ostati njemu radi sluge mojega Davida i radi grada Jerusalima, koji izabrah izmeðu svijeh plemena Izrailjevih.
33 Ndidzachita zimenezi chifukwa wandisiya Ine ndi kupembedza Asitoreti mulungu wamkazi wa Asidoni, Kemosi mulungu wa Amowabu ndiponso Moleki mulungu wa Aamoni, ndipo sanayende mʼnjira yanga, kapena kusunga mawu anga ndi malamulo anga monga anachitira Davide abambo ake.
Jer ostaviše mene i pokloniše se Astaroti boginji Sidonskoj i Hemosu bogu Moavskom i Melhomu bogu sinova Amonovijeh, i ne hodiše putovima mojim èineæi što je pravo preda mnom, uredbe moje i zakone moje, kao David otac njegov.
34 “‘Koma sindidzalanda ufumu wonse mʼdzanja la Solomoni. Ine ndamuyika kukhala wolamulira masiku onse a moyo wake chifukwa cha mtumiki wanga Davide, amene ndinamusankha ndiponso amene anamvera malamulo anga ndi mawu anga.
Ali neæu uzeti carstva iz ruku njegovijeh, nego æu ga ostaviti neka vlada dokle je god živ Davida radi sluge svojega, kojega izabrah, koji je držao zapovijesti moje i uredbe moje.
35 Ndidzalanda ufumu mʼdzanja la mwana wake ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
Nego æu uzeti carstvo iz ruku sina njegova, i daæu tebi od njega deset plemena.
36 Ndidzapereka fuko limodzi kwa mwana wake ndi cholinga choti Davide mtumiki wanga adzakhale nyale nthawi zonse pamaso panga mu Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha kuyikamo Dzina langa.
A sinu æu njegovu dati jedno pleme da bude vidjelo Davidu sluzi mojemu vazda preda mnom u gradu Jerusalimu, koji izabrah da u njemu namjestim ime svoje.
37 Koma kunena za iwe, ndidzakutenga ndipo udzalamulira chilichonse chimene mtima wako ukukhumba; udzakhala mfumu ya Israeli.
Tebe æu dakle uzeti da caruješ nad svijem što ti duša želi, i biæeš car nad Izrailjem.
38 Ngati udzamvera zonse zimene ndidzakulamula ndi kuyenda mʼnjira yanga ndi kuchita zabwino pamaso panga, posunga malamulo anga ndi mawu anga monga anachitira Davide mtumiki wanga, Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakupatsa ufumu umene udzakhala wokhazikika monga ndinamupatsira Davide, ndipo Ine ndidzakupatsa Israeli.
I ako uzaslušaš sve što ti zapovjedim, i uzideš mojim putovima i ušèiniš što je pravo preda mnom, držeæi uredbe moje i zapovijesti moje, kao što je èinio David sluga moj, biæu s tobom i sazidaæu ti tvrd dom, kao što sam sazidao Davidu, i daæu ti Izrailja.
39 Ine ndidzalanga zidzukulu za Davide chifukwa cha zimenezi, koma osati kwamuyaya.’”
I muèiæu sjeme Davidovo za to, ali ne svagda.
40 Solomoni anafunitsitsa kupha Yeroboamu, koma Yeroboamu anathawira ku Igupto, kwa Sisaki mfumu ya Igupto ndipo anakhala kumeneko mpaka Solomoni atamwalira.
Zato tražaše Solomun da ubije Jerovoama; ali se Jerovoam podiže i pobježe u Misir k Sisaku caru Misirskom, i bi u Misiru dok ne umrije Solomun.
41 Ntchito zina za Solomoni, zonse zomwe anachita komanso za nzeru zake, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya Solomoni?
A ostala djela Solomunova i što je god èinio, i mudrost njegova, nije li to zapisano u knjizi djela Solomunovijeh?
42 Solomoni analamulira Aisraeli onse mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi.
A carova Solomun u Jerusalimu nad svijem Izrailjem èetrdeset godina.
43 Ndipo anagona ndi makolo ake nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo ake.
I poèinu Solomun kod otaca svojih, i bi pogreben u gradu Davida oca svojega; a Rovoam sin njegov zacari se na njegovo mjesto.

< 1 Mafumu 11 >