< 1 Mafumu 1 >

1 Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
Gdy król Dawid zestarzał się [i] posunął w latach, to choć okrywano go szatami, nie mógł się rozgrzać.
2 Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
Jego słudzy powiedzieli mu więc: Niech poszukają dla naszego pana, króla, młodej dziewicy, która stawałaby przed królem i pielęgnowała go. Niech kładzie się na twoim łonie, żeby nasz pan, król, mógł się rozgrzać.
3 Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
Szukali więc pięknej dziewczyny po wszystkich obszarach Izraela i znaleźli Abiszag Szunamitkę, i przyprowadzili ją do króla.
4 Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
Dziewczyna ta [była] bardzo piękna; pielęgnowała króla i służyła mu, ale król z nią nie obcował.
5 Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
Lecz Adoniasz, syn Chaggity, wywyższał się, mówiąc: Ja zostanę królem. Zaopatrzył się w rydwany i jeźdźców oraz pięćdziesięciu mężczyzn, którzy biegali przed nim.
6 (Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
Jego ojciec nigdy go nie upominał, mówiąc: Czemu to uczyniłeś? Był on też bardzo przystojny, [jego matka] urodziła go po Absalomie.
7 Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
Porozumiał się z Joabem, synem Serui, i z kapłanem Abiatarem, a oni przystali z Adoniaszem i pomogli [mu].
8 Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
Lecz kapłan Sadok, Benajasz, syn Jehojady, prorok Natan, Szimei, Rei oraz dzielni wojownicy Dawida nie sprzyjali Adoniaszowi.
9 Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
Potem Adoniasz zabił owce, woły i tuczne bydło przy kamieniu Zochelet, blisko źródła Rogel, i zaprosił wszystkich swych braci, synów króla, oraz wszystkich mężczyzn Judy, sługi króla.
10 koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
Lecz nie zaprosił proroka Natana, Benajasza i dzielnych wojowników oraz swego brata Salomona.
11 Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
Wtedy Natan zapytał Batszebę, matkę Salomona: Czy nie słyszałaś, że Adoniasz, syn Chaggity, króluje, a nasz pan, Dawid, [o tym] nie wie?
12 Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
Chodź więc teraz, proszę, dam ci radę, abyś ocaliła swoje życie i życie swego syna, Salomona.
13 Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
Idź i wejdź do króla Dawida, i powiedz mu: Czyż ty, mój panie, królu, nie przysiągłeś swojej służącej: Twój syn Salomon będzie królował po mnie i on zasiądzie na moim tronie? Dlaczego więc króluje Adoniasz?
14 Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
A oto gdy ty będziesz tam jeszcze rozmawiała z królem, ja wejdę za tobą i potwierdzę twoje słowa.
15 Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
Batszeba weszła więc do króla do komnaty. Król już się bardzo zestarzał, a Abiszag Szunamitka usługiwała królowi.
16 Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
Wtedy Batszeba uklękła i oddała pokłon królowi, a król zapytał: Czego chcesz?
17 Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
A [ona] mu odpowiedziała: Mój panie, ty przysiągłeś swojej służącej na PANA, swego Boga: Twój syn, Salomon, będzie królował po mnie i on zasiądzie na moim tronie.
18 Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
A oto teraz Adoniasz króluje, a ty, mój panie, królu, [o tym] nie wiesz.
19 Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
Zabił bowiem woły, tuczne bydło i bardzo dużo owiec i zaprosił wszystkich synów króla, kapłana Abiatara oraz dowódcę wojska, Joaba, ale twego sługi Salomona nie zaprosił.
20 Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
Lecz ty, mój panie, królu, [wiesz], że oczy całego Izraela są zwrócone na ciebie, abyś im oznajmił, kto zasiądzie na tronie mego pana, króla, po nim.
21 Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
W przeciwnym razie, gdy mój pan, król, zaśnie ze swymi ojcami, ja i mój syn Salomon będziemy uważani za przestępców.
22 Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
A gdy jeszcze rozmawiała z królem, przyszedł prorok Natan.
23 Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
I oznajmiono królowi: Oto prorok Natan. I gdy wszedł przed oblicze króla, pokłonił się królowi twarzą do ziemi.
24 Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
Potem Natan powiedział: Mój panie, królu, czy ty powiedziałeś: Adoniasz będzie królował po mnie i on zasiądzie na moim tronie?
25 Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
Dziś bowiem zstąpił i zabił woły, tuczne bydło oraz bardzo dużo owiec, i zaprosił wszystkich synów króla, dowódców wojsk oraz kapłana Abiatara, a oto oni jedzą z nim i piją, i mówią: Niech żyje król Adoniasz!
26 Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
Lecz mnie, twego sługi, i kapłana Sadoka, i Benajasza, syna Jehojady, oraz twego sługi Salomona nie zaprosił.
27 Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
Czy wyszło to od mego pana, króla, a nie oznajmiłeś swemu słudze, kto zasiądzie po nim na tronie mego pana, króla?
28 Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
Król Dawid odpowiedział: Zawołajcie mi Batszebę. Ta weszła przed oblicze króla i stanęła przed nim.
29 Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
Wtedy król przysiągł: Jak żyje PAN, który wybawił moją duszę z wszelkiego ucisku;
30 ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
Jak przysiągłem ci na PANA, Boga Izraela: Twój syn Salomon będzie królować po mnie i on zasiądzie na moim tronie zamiast mnie, tak dziś uczynię.
31 Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
Batszeba schyliła się twarzą ku ziemi i pokłoniła się królowi, i powiedziała: Niech żyje mój pan, król Dawid, na wieki!
32 Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
Potem król Dawid rozkazał: Zawołajcie mi kapłana Sadoka, proroka Natana i Benajasza, syna Jehojady. I [tamci] weszli przed oblicze króla.
33 mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
A król powiedział im: Weźcie ze sobą sługi waszego pana, wsadźcie mego syna Salomona na moją mulicę i sprowadźcie go do Gichonu.
34 Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
A tam niech kapłan Sadok i prorok Natan namaszczą go na króla nad Izraelem. Następnie zadmijcie w trąbę i powiedzcie: Niech żyje król Salomon!
35 Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
Potem pójdziecie za nim, a on przyjdzie i zasiądzie na moim tronie, i będzie królował na moje miejsce. Jego bowiem ustanowiłem wodzem nad Izraelem i nad Judą.
36 Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
Benajasz, syn Jehojady, odpowiedział królowi: Amen. Niech to stwierdzi PAN, Bóg mego pana, króla.
37 Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
Jak PAN był z moim panem, królem, tak niech będzie z Salomonem i niech wywyższy jego tron nad tron mego pana, króla Dawida.
38 Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
Poszli więc kapłan Sadok, prorok Natan i Benajasz, syn Jehojady, oraz Keretyci i Peletyci i wsadzili Salomona na mulicę króla Dawida, i zaprowadzili go do Gichonu.
39 Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
Wtedy kapłan Sadok wziął róg olejku z namiotu i namaścił Salomona. Potem zadęto w trąbę, a cały lud powiedział: Niech żyje król Salomon!
40 Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
I cały lud szedł za nim. Lud także grał na fletach i tak bardzo się radował, że ziemia drżała od jego głosu.
41 Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
I usłyszeli to Adoniasz oraz wszyscy zaproszeni, którzy z nim byli, a właśnie skończyli ucztę. A gdy Joab usłyszał głos trąby, zapytał: Cóż to za krzyk poruszonego miasta?
42 Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
A gdy on jeszcze mówił, przyszedł Jonatan, syn kapłana Abiatara. Adoniasz powiedział mu: Wejdź, jesteś bowiem dzielnym człowiekiem i przynosisz dobrą nowinę.
43 Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
Wtedy Jonatan odpowiedział Adoniaszowi: Nasz pan, król Dawid, ustanowił królem Salomona.
44 Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
Król bowiem posłał z nim kapłana Sadoka i proroka Natana oraz Benajasza, syna Jehojady, do tego Keretytów i Peletytów, którzy wsadzili go na mulicę króla;
45 ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
Następnie kapłan Sadok i prorok Natan namaścili go na króla w Gichonie. I wyruszyli stamtąd, tak się radując, że miasto zadrżało. Stąd ten krzyk, który usłyszeliście.
46 Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
A Salomon zasiadł już na tronie królestwa.
47 Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
Ponadto przyszli słudzy króla, aby błogosławić naszemu panu, królowi Dawidowi, mówiąc: Niech Bóg sławniejszym uczyni imię Salomona niż twoje imię i niech wywyższy jego tron ponad twój tron. A król skłonił się na [swym] łożu.
48 inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
Również sam król powiedział: Błogosławiony [niech będzie] PAN, Bóg Izraela, który dał dziś zasiadającego na moim tronie, a moje oczy to widzą.
49 Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
Wtedy zlękli się wszyscy zaproszeni, którzy byli z Adoniaszem, i wstali, i poszli każdy swoją drogą.
50 Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
Adoniasz także, bojąc się Salomona, wstał, poszedł i uchwycił się rogów ołtarza.
51 Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
I doniesiono o tym Salomonowi: Oto Adoniasz boi się króla Salomona i uchwycił się rogów ołtarza, mówiąc: Niech mi dziś przysięgnie król Salomon, że nie zabije swego sługi mieczem.
52 Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
Wtedy Salomon odpowiedział: Jeśli okaże się godziwym człowiekiem, nie spadnie mu nawet włos na ziemię, ale jeśli znajdzie się w nim zło, poniesie śmierć.
53 Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”
Król Salomon posłał więc, aby go sprowadzono od ołtarza. Kiedy przyszedł, pokłonił się królowi Salomonowi. A powiedział mu Salomon: Idź do swego domu.

< 1 Mafumu 1 >