< 1 Akorinto 16 >

1 Tsopano za zopereka zothandiza anthu a Ambuye a ku Yerusalemu. Muchite zomwe ndinawuza mipingo ya ku Galatiya kuti ichite.
Now concerning the offering for the saints, you also are to do as I directed the church of Galatia.
2 Pa tsiku loyamba la sabata lililonse, aliyense wa inu azipatula ndalama molingana ndi zomwe wapezera. Asunge, kuti ndikabwera pasadzakhalenso msonkhamsonkha.
On the first day of each week let each of you put aside something, keeping it in store as he may prosper, so that when I come there may be no collections going on.
3 Pamenepo, ndikadzafika, ndidzawapatsa makalata a umboni anthu amene mudzawasankhe ndi kuwatuma kuti akapereka mphatso zanu ku Yerusalemu.
On my arrival I will send those whom you may accredit by letter to carry your bounty to Jerusalem.
4 Ngati kutaoneka kuti nʼkoyenera kuti ndipite nawo, adzapita nane limodzi.
And if it is worth while for me to go too, they will accompany me.
5 Ndidzafika kwanuko nditadutsa ku Makedoniya pakuti ndikuyembekezera kudzera ku Makedoniyako.
Now I shall come to you after I have gone through Macedonia.
6 Mwina ndidzakhala nanu kanthawi kochepa kapenanso nyengo yonse yozizira, kuti mudzandithandize kupitiriza ulendo wanga kulikonse kumene ndingapite.
I shall remain some time with you; possibly spending the winter, in order that you may help me forward in whatever journey I take.
7 Sindikufuna kuti ndikuoneni tsopano mongodutsa chabe, koma ndikuyembekezera kudzakhala nanu kwa kanthawi, ngati Ambuye alola.
For I do not wish at this present time to see you merely in passing; but if the Lord permits, I hope to remain some time with you.
8 Koma ndikhala ndili ku Efeso mpaka nthawi ya Pentekosite,
I am staying for the present in Ephesus, until Pentecost;
9 pakuti mwayi waukulu wapezeka woti nʼkugwira ntchito yaphindu, koma pali ambiri amene akutsutsana nane.
for a door has opened to me, great and effectual, and the opponents are many.
10 Ngati Timoteyo afike kwanuko, onetsetsani kuti pasakhale zina zomuchititsa mantha pamene ali pakati panu, pakuti iye akugwira ntchito ya Ambuye monga ine.
If Timothy come, see to it that he is among you without trepidation; for he is doing the Lord’s work, as I am, so let no one disparage him.
11 Wina aliyense asamunyoze. Muthandizeni kupitiriza ulendo wake mwamtendere kubwereranso kuli ine. Ndikumuyembekeza pamodzi ndi abale ena.
Whenever he comes to me, send him on his way in peace, for I am expecting him with the other brothers.
12 Tsono kunena za mʼbale wathu, Apolo, ndinamuwumiriza kwambiri kuti abwere kwa inu abale, ndipo iye sanafune kupita tsopano. Koma akadzapeza mpata wabwino adzabwera.
As for our Apollos, I have many times urged him to go to you with the others, but he was always unwilling to go to you at this time. He will come, however, whenever he has a good opportunity.
13 Khalani tcheru; khazikikani mʼchikhulupiriro chanu; limbani mtima; khalani amphamvu.
Be watchful, stand firm in the faith, be manly, be strong.
14 Chitani zonse mwachikondi.
Let all that you do be done in love.
15 Mukudziwa kuti a mʼbanja la Stefano ndiye anali oyamba kutembenuka mtima ku Akaya, ndipo akhala akudzipereka kutumikira oyera mtima. Choncho ndikukudandaulirani, inu abale,
I beg you this, my brothers - you know the household of Stephanus, that they were the first-fruits of Achaia, and that they devoted themselves to the service of the saints -
16 kuti muziwamvera anthu oterewa, ndiponso aliyense wogwira nawo ntchitoyi modzipereka.
so I want you also to show deference to such, and to every fellow worker, and laborer.
17 Ndikondwera kuti Stefano, Fortunato ndi Akayiko afika, chifukwa akhala akundithandiza pakuti inu simuli nane.
I am glad that Stephanus and Fortunatus and Achaicus have arrived, for they have made up for your absence.
18 Pakuti anatsitsimutsa mzimu wanga ndi wanu womwe. Anthu a mtundu oterewa ngofunika kuwalemekeza.
They refresh my spirit as they do yours. So cultivate the acquaintance of such men.
19 Mpingo wa mʼchigawo cha ku Asiya ukupereka moni. Akula ndi Prisila akuperekanso moni wachisangalalo, mwa Ambuye, ndiponso mpingo umene umakumana mʼnyumba mwawo ukupereka moni.
The churches of Asia greet you. Aquila and Priscilla (Prisca), with the church that meets in their house, greet you heartily in the Lord.
20 Abale onse kuno akupereka moni wawo. Patsanani moni wachikondi chenicheni.
All the brothers send greetings. Greet one another with a holy kiss.
21 Ineyo Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa mawu awa akuti moni.
The greeting of me, Paul, with my own hand.
22 Ngati wina sakonda Ambuye akhale wotembereredwa. Maranatha! (Ambuye athu bwerani)!
If any one does not love the Lord, let him be accursed. Our Lord is coming.
23 Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi inu.
The grace of our Lord Jesus be with you.
24 Chikondi changa chikhale ndi nonsenu mwa Khristu Yesu.
My love be with you all in Christ Jesus.

< 1 Akorinto 16 >