< 1 Akorinto 15 >

1 Tsono abale, ndikufuna ndikukumbutseni za Uthenga Wabwino umene ndinakulalikirani. Munawulandira ndipo munawukhulupirira kolimba.
Nambeambe nendakuwakombosha, ainja na alombo, nnani ya injili yaihubiriwa, ambayo mwaipokile ni yema nakwe.
2 Inu munapulumutsidwa ndi Uthenga Wabwinowu, ngati mwasunga mawu amene ndinakulalikirani. Kupanda kutero, mwangokhulupirira pachabe.
Ni katika injili yee mwatilopolelwa, kati mwalikamwa imara neno lyaniwahubirie mwenga, ila muaminiya bure.
3 Pakuti chimene ndinalandira ndinapereka kwa inu monga chofunika kuposa zonse, kuti Khristu anafera zoyipa zathu monga mwa Malemba,
Kati kwanza yaniipokii kwa umuhimu niiletike kwinu kati ya ibile: panga bokana na maandiko, Kristo awile kwa ajili ya sambi yitu,
4 kuti anayikidwa mʼmanda, kuti anaukitsidwa tsiku lachitatu monga mwa Malemba;
bokana na maandiko atisikwa, ni panga atifufuka lisoba lya tatu.
5 ndipo kuti anaonekera kwa Petro, ndipo kenaka kwa Atumwi khumi ndi awiriwo.
Ni panga ywamtokii Kefa, boka po kwa balo komi ni ibele.
6 Pambuyo pake, Iye anaonekera kwa anthu oposa 500 mwa abale pa nthawi imodzi, ndipo ambiri mwa iwo akanali ndi moyo ngakhale kuti ena anagona tulo.
Boka po atikwatokiya kwa muda umo ba'ainja na alombo zaidi ya mia tano. Baingi babe babile bado akoto, lakini baadhi yabe bagonjike lugono.
7 Kenaka anaonekeranso kwa Yakobo, kenaka kwa atumwi onse.
Boka po atikumtokya Yakobo, boka po mitume yote.
8 Potsiriza pa onse anaonekeranso kwa ine, monga mwana wobadwa nthawi isanakwane.
Mwisho wa bote, atikunitokya nenga, kati yee kwa mwana ywabile belekwa katika wakati ubile kwaa sahihi.
9 Pakuti ine ndine wamngʼono kwa atumwi ndipo sindiyenera nʼkomwe kutchedwa mtumwi chifukwa ndinazunza mpingo wa Mulungu.
Kwa kuwa nenga na nchunu kati ya mitume. Nastahili kwaa kemelwa mtume, kwa sababu natilitesa likanisa lya Nnongo.
10 Koma mwachisomo cha Mulungu, ndili mmene ndililimu, ndipo chisomo chake kwa ine sichinali chopanda ntchito. Ndinagwira ntchito kuposa ena onse a iwo. Choncho sindine koma chisomo cha Mulungu chimene chinali ndi ine.
Lakini kwa neema ya Nnongo nibile kati yanibile, na neema yake kwango yaibile kwaa bure. Badala yake, nipangite bidii kuliko wote. Lakini ibile kwaa nenga, ila neema ya Nnongo ibile nkati yango.
11 Tsono kaya ndi ineyo kapena iwowo, izi ndi zomwe timalalikira, ndipo izi ndi zimene munakhulupirira.
Kwa eyo kati ni nenga au bembe, twati lihubiri nyoo na tutiaminiya nyoo.
12 Koma ngati timalalikira kuti Khristu anaukitsidwa kwa akufa, zikutheka bwanji kuti ena mwa inu azinena kuti kulibe kuuka kwa akufa?
Nambeambe kati Kristo atihubiriwa kati ywafufuka kwa bandu babile mu'kiwo, ibe namani baadhi yinu mubaye ntopo ufufuo wa bandu babile mu'kiwo?
13 Ngati kulibe kuuka kwa akufa, ndiye kuti ngakhale Khristu sanaukenso.
Lakini mana ntopo Ufufuo wa bandu babile mu'kiwo, bai hata Kristo afufuka kwaa kae.
14 Ndipo ngati Khristu sanaukitsidwe, ndiye kuti kulalikira kwathu nʼkopanda ntchito, ndipo chikhulupiriro chanu nʼchopandanso ntchito.
Ni mana Kristo afufuka kwaa, nga nyoo mahubiri yitu ni bure, na imani yitu ni bure.
15 Kuwonjezera pamenepa, ndiye kuti ndife mboni zabodza pa za Mulungu, pakuti tikuchita umboni kuti Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa. Ngati nʼzoona kuti akufa saukitsidwa, ndiye kuti Mulungu sanaukitsenso Khristu.
Ni twapatikana kuwa mashahidi ba ubocho kumhusu Nnongo, kwa sababu twatimshuhudia Nnongo kinchogo, baya atimfufua Kristo, wakati atikumfufua kwaa.
16 Pakuti ngati akufa saukitsidwa, ndiye kuti nayenso Khristu sanaukitsidwe.
Kati mana itei bandu bakiwo bafufuliwa kwaa, Yesu kae afufuliwa kwaa.
17 Ndipo ngati Khristu sanaukitsidwe, chikhulupiriro chanu nʼchopanda ntchito; mukanali mu machimo anu.
Ni kati Kristo afufuliwa kwaa, imani yinu nga ya bure na bado mubile katika sambi yinu.
18 Ndiye kuti nawonso amene agona tulo mwa Ambuye ndi otayika.
Nga nyoo hata balo babile batiwaa katika Kristo kae batiangamia.
19 Ngati kukanakhala kuti tili ndi chiyembekezo mwa Khristu mʼmoyo uno wokha, tikanakhala omvetsa chisoni kuposa anthu ena onse.
Mana itei kwa maisha aga kichake tubile ni ujasiri kwa wakati woisa nkati ya Kristo, bandu bote, twenga niwakuhurumilwa zaidi ya bandu bote.
20 Koma nʼzoonadi kuti Khristu anaukitsidwa kwa kufa, chipatso choyamba cha onse ogona tulo.
Lakini nambeambe Kristo atifufuka boka mu'kiwo, matunda ya kwanza ya balo babile mu'kiwo.
21 Pakuti monga imfa inadza kudzera mwa munthu, kuuka kwa akufa kwabweranso kudzera mwa munthu.
Kwa mana kiwo kiisile pitya bandu, pitya kae bandu ni ufufuo wa bandu.
22 Pakuti monga mwa Adamu onse amafa, chomwechonso mwa Khristu onse adzakhala ndi amoyo.
Kwa mana kati katika Adamu bote batiwaa, nga nyoo kae katika Kristo bote balowa pangika akoto.
23 Koma aliyense adzauka pa nthawi yake. Khristu ndiye woyambirira, pambuyo pake, pamene Khristu adzabwera, iwo amene ali ake adzauka.
Lakini kila yumo kayika mpango wake: Kristo, matunda ga kwanza, ni boka po balo babile ba Kristo bapangite ukoto wakati woisa kwake.
24 Pamenepo chimaliziro chidzafika, pamene Iye adzapereka ufumu kwa Mulungu Atate, atathetsa ufumu wonse, ulamuliro wonse ndi mphamvu zonse.
Nga po walowa pangika mwisho, palyo Kristo paakabidhi upwalume kwa Nnongo Tate. Ayee nga palyo palowa komesha utawala wote ni mamlaka yote ni ngupu.
25 Pakuti Iye ayenera kulamulira mpaka Mulungu atayika pansi pa mapazi ake adani ake onse.
Kwa kuwa lazima atawale mpaka paalowa beka maadui bake bote pae ya nyayo yake.
26 Mdani wotsiriza kuwonongedwa ndi imfa.
Adui wa mwisho uharibiwa ni kiwo.
27 Pakuti Mulungu “wayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake.” Ponena kuti wayika “zinthu zonse pansi pa mapazi ake,” nʼchodziwikiratu kuti sakuphatikizapo ndi Mulungu yemwe, amene anayika zinthu zonse pansi pa Khristu.
Kwa mana “abekite kila kilebe pae ya nyayo yabe.” Lakini paibaya “abekite kila kilebe,” ni wazi panga yee iusishe kwaa balo babekite kila kilebe pae yake mwene.
28 Pamene adzatsiriza kuchita zimenezi, Mwana weniweniyo adzakhala pansi pa ulamuliro wa Iye amene anayika zinthu zonse pansi pake, kuti Mulungu akhale zonse mu zonse.
Wakati ilebe yote ibekilwe pae yake, boka po mwana mwene alowa bekwa pae kwake ywembe ywabile atikuibeka ilebe yote pae yake. Ayee nga ipangike ili panga Nnongo Tate abe yote nkati ya gote.
29 Tsono ngati kulibe kuuka kwa akufa, kodi iwo amene akubatizidwa chifukwa cha akufa, adzatani? Ngati akufa saukitsidwa nʼkomwe, bwanji nanga anthu akubatizidwa mʼmalo mwawo?
Au kae bapanga namani balo baabatizwile kwa ajili ya bandu ba kiwo? Kati bandu ba kiwo bafufuliwa kwaa kabisa, kwa namani kae batibatizwa kwa ajili yabe?
30 Ndipo kwa ife, tikuyikiranji moyo wathu pachiswe nthawi ndi nthawi?
na kwa namani tubile katika hatari kila saa?
31 Abale, ndimafa tsiku ndi tsiku, ndikunenetsa zimenezi, mongotsimikizira monga ndimakunyadirani mwa Khristu Yesu Ambuye athu.
Ainja ni alombo bango, petya kuisifu kwango katika mwenga, ambayo nibile nayo katika Kristo Yesu Ngwana witu, natangaza nyoo: nawaa kila lisoba.
32 Ngati ndinalimbana ndi zirombo za kuthengo ku Efeso pa zifukwa za umunthu chabe, ndapindulanji? Ngati akufa sadzaukitsidwa, “Tiyeni tidye ndi kumwa, pakuti mawa tifa.”
Ifaika namani, katika mtazamo wa bandu, kati bandu ba'kiwo bafufuliwa kwaa? “Leka bai tulyee ni nywaa, kwa mana malabo twalowa waa.”
33 Musasocheretsedwe, “Kukhala mʼmagulu oyipa kumawononga makhalidwe abwino.”
Kana mulongele ubocho: “Makundi ganoite kwaa uharibia tabia inoyite.
34 Ganizani bwino monga kuyenerera, ndiye lekani kuchimwa; pakuti pali ena amene sadziwa Mulungu. Ndikunena izi kuti muchite manyazi.
“Mube na kiasi! mutame katika haki! kana muyendelee panga sambi. Kwa mana baadhi yinu mubile kwaa ni maarifa ya Nnongo. Nabaya nyoo kwa oni yinu.
35 Koma wina akhoza kufunsa kuti, “Kodi akufa amaukitsidwa motani? Adzauka ndi thupi la mtundu wanji?”
Lakini mundu ywenge abaya,”Jinsi gani bandu ba kiwo balowa fufuliwa? Na bembe balowa isa na aina gani ya yega?”
36 Wopusa iwe! Chimene mudzala sichikhala ndi moyo pokhapokha chitayamba chafa.
Wenga wa nlalo muno! Chelo chaukipandile kiweza kwaa kuanza kukua ila kiwile.
37 Mukadzala, simudzala thupi limene lidzamere, koma mbewu chabe, mwina ya tirigu kapena ya china chake.
Na chelo cha ukipandike ni yega kwaa ambao walowa kua, ila mbeyu yaichipua. Iweza kuwa ngano au kilebe chenge.
38 Koma Mulungu amayipatsa thupi monga Iye wafunira, ku mbewu ya mtundu uliwonse amapereka thupi lakelake.
Lakini Nnongo aipeya yega kati yaapendile, na katika kila mbeyu yega yake mwene.
39 Mnofu siwofanana. Anthu ali ndi mnofu wa mtundu wina, nyama zili ndi wina, mbalame zili ndi wina, nsomba zili ndi winanso.
Yega yote ilandana kwaa, ila, kwabile na yega imo wa bandu, ni yega yenge ya anyama, na yega yenge ya iyuni, ni yenge kwa ajili ya omba.
40 Palinso matupi akumwamba ndipo palinso matupi a dziko lapansi; koma ulemerero wa matupi akumwamba ndi wina, ndi wa matupi a dziko lapansi ndi winanso.
Pabile na yega ya kumaunde kae ni yega ya mu'dunia. Lakini utukufu wa yega ya kumaunde ni aina yimo na utukufu wa mu'dunia ni wenge.
41 Dzuwa lili ndi ulemerero wake, ndipo pali ulemerero wina wa mwezi, palinso ulemerero winanso wa nyenyezi. Ulemerero wa nyenyezi ndi wosiyanasiyana.
Kwabile ni utukufu umo wa lilumu, ni utukufu wenge wa mwei, ni utukufu wenge wa tondwa. Kwa mana tondwa yimo itofautiana ni tondwa yenge katika utukufu.
42 Zidzaterenso pamene akufa adzauka. Thupi loyikidwa mʼnthaka ngati mbewu limavunda, koma likadzauka lidzakhala losavunda.
Nga nyoo ubile kae ni ufufuo wa bandu ba kiwo. Chelo chakipandwile, na chakiotile kiaribika kwaa.
43 Limayikidwa mʼmanda mopanda ulemu, koma likadzaukitsidwa lidzakhala ndi ulemerero. Limayikidwa mʼmanda lili lofowoka, koma likadzaukitsidwa lidzakhala ndi mphamvu.
Kipandilwe katika matumizi ya kawaida, kioteshwa katika utukufu. Kipandilwe katika udhaifu, kioteshwa katika ngufu.
44 Limayikidwa mʼmanda thupi la mnofu chabe, koma likadzaukitsidwa lidzakhala lauzimu. Ngati pali thupi la mnofu, palinso thupi lauzimu.
Kipandilwe katika yega wa asili, kioteshwa katika yega wa kiroho. Kati kwabile ni yega wa asili, kubile ni yega ya kiroho kae.
45 Kwalembedwa kuti, “Munthu woyamba Adamu anakhala wamoyo,” Adamu wotsiriza anakhala wopatsa moyo.
Nga nyoo iandikilwe kae,”Mundu wa kwanza Adamu atipangika roho yaatama.” Adamu wa mwisho atipangika roho yaitoa ukoto.
46 Zauzimu sizinabwere koyambirira, koma zachilengedwe, pambuyo pake zauzimu.
Lakini wa kiroho aisa kwaa kwanza ila wa asili, ni boka po wa kiroho.
47 Munthu woyamba anali wa dziko lapansi, wochokera mʼnthaka koma munthu wachiwiri anali wochokera kumwamba.
Mundu wa kwanza ni wa dunia, atitengenezwa kwa mavumbi. Mundu wanaibele aboka kumaunde.
48 Monga analili munthu wa dziko lapansi, momwemonso anthu onse amene ndi a dziko lapansi. Ndipo monga alili munthu wakumwamba, momwemonso anthu onse amene ndi akumwamba.
Kati ya yolo ywapangilwe kwa mavumbi, nga nyoo pia balo bapangilwe kwa mavumbi. Kati ya mundu wa kumaunde abile, nga nyoo kae balo ba kumaunde.
49 Ndipo monga momwe tinabadwa ofanana ndi munthu wa dziko lapansi uja, momwemonso tidzakhala ofanana ndi munthu wakumwamba.
Kati ambavyo tupapike mfano wa mundu wa mavumbi, tupapike kae mfano wa mundu wa kumaunde.
50 Ndikunenetsa, abale, kuti thupi ndi magazi sizingathe kulowa mu ufumu wa Mulungu, ndipo zimene zimavunda sizingathe kulowa kumene zinthu sizivunda.
Nambeambe naabakiya, ainja na alombo bango, panga yega na mwai iweza kwaa kuurithi upwalume wa Nnongo. Wala wakuharibika kurithi wauharibika kwaa.
51 Tamverani, ndikuwuzeni chinsinsi. Tonse sitidzagona tulo, koma tonse tidzasandulika.
Linga! Naabakiya mwenga siri ya kweli: Twawile kwaa bote, ila bote twalowa badilishwa.
52 Zidzachitika mwadzidzidzi, mʼkamphindi kochepa, monga ngati kuphethira kwa diso, pa lipenga lotsiriza. Pakuti lipenga lidzalira, akufa adzaukitsidwa opanda chovunda, ndipo ife tidzasandulika.
Twalowa badilishwa katika muda, katika kufumba ni kufumbua kwa liyo, katika tarumbeta lya mwisho. Kwa kuwa tarumbeta yalowa lela, ni banda babile mu'kiwo balowa fufuliwa na hali ya haribika kwaa, na twalowa badilishwa.
53 Pakuti chovunda chiyenera kuvala chosavunda, ndi thupi ili lakufa liyenera kuvala losafa.
Kwani awoo waharibika ni lazima uwale wa haribika kwaa, ni wolo wa waa lazima uwale wa waa kwaa.
54 Pamene thupi lovundali likadzasanduka losavunda, ndipo thupi lotha kufali likadzasanduka losatha kufa, pamenepo zidzakwaniritsidwa zimene zinalembedwa zakuti, “Imfa yogonjetsedwa kwathunthu.”
Lakini muda woo wa haribika walowa walikwa wa haribika kwaa, ni wolo wa kiwo walowa jingya mu'kiwo, nga waisa msema ambao uandikilwe,”Kiwo chamezwile katika ushindi.”
55 “Iwe imfa, kupambana kwako kuli kuti? Iwe imfa, ululu wako uli kuti?” (Hadēs g86)
Kiwo, ushindi wako ubile kwaako? Kiwo, ubile kwaako ni uchungu wako?” (Hadēs g86)
56 Ululu wa imfa ndi tchimo, ndipo mphamvu ya tchimo ndi lamulo.
Uchungu wa kiwo ni sambi, ni nguvu ya sambi ni saliya.
57 Koma tiyamike Mulungu amene amatipambanitsa mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
Lakini shukrani kwa Nnongo, ywatupeile twenga ushindi pitya Ngwana witu Yesu Kristo!
58 Choncho, abale anga okondedwa imani njii. Musasunthike ndi chilichonse. Nthawi zonse mudzipereke kwathunthu ku ntchito ya Ambuye, chifukwa mukudziwa kuti ntchito zanu mwa Ambuye sizili zopanda phindu.
Kwa eyo, apendwa ainja na alombo bango, mube imara na kana mlendeme. Daima muipange kazi ya Ngwana, kwa sababu mutangite kuwa kazi yinu katika Ngwana ni yabure kwaa.

< 1 Akorinto 15 >