< 1 Mbiri 28 >

1 Davide anayitana akuluakulu onse a Israeli kuti asonkhane ku Yerusalemu: akuluakulu a mafuko, olamulira magulu a ntchito ya mfumu, olamulira ankhondo 1,000, ndi olamulira ankhondo 100, ndiponso akuluakulu onse osunga katundu ndi ziweto za mfumu ndi ana ake, pamodzinso ndi akuluakulu a ku nyumba yaufumu, anthu amphamvu ndi asilikali onse olimba mtima.
Therfor Dauid clepide togidere alle the princes of Israel, the duykis of lynagis, and the souereyns of cumpenyes, that `mynystriden to the kyng, also the tribunes, and centuriouns, and hem that weren souereyns ouer the catel and possessiouns of the kyng, and hise sones, with `nurchis, and techeris, and alle the myyti and strongeste men in the oost of Jerusalem.
2 Mfumu Davide inayimirira ndipo inati: “Tamverani abale anga ndi anthu anga. Ine ndinali ndi maganizo omanga nyumba monga malo okhalamo Bokosi la Chipangano la Yehova, malo oyikapo mapazi a Mulungu wathu, ndipo ndinakonza ndondomeko yomangira nyumbayo.”
And whanne the kyng hadde rise, and `hadde stonde, he seide, My britheren and my puple, here ye me. Y thouyte for to bilde an hows, wherynne the arke of boond of pees of the Lord, and the stool of the feet of oure God schulde reste; and Y made redi alle thingis to bilde.
3 Koma Mulungu anati kwa ine, “Usandimangire nyumba chifukwa ndiwe munthu wankhondo ndipo wakhala ukukhetsa magazi.”
But God seide to me, Thou schalt not bilde an hows to my name, for thou art a man werriour, and hast sched blood.
4 “Komabe Yehova Mulungu wa Israeli anasankha ine pakati pa onse a banja langa kukhala mfumu ya Israeli kwamuyaya. Iye anasankha Yuda kukhala mtsogoleri, ndipo pa banja la Yuda anasankha banja langa. Pakati pa ana aamuna a abambo anga, kunamukomera Iye kundikhazika mfumu ya Aisraeli onse.
But the Lord God of Israel chees me of al the hows of my fadir, that Y schulde be kyng on Israel with outen ende; for of Juda he chees princes, sotheli of the hows of Juda he chees the hows of my fadir, and of the sones of my fadir it pleside hym to chese me kyng on al Israel.
5 Pa ana anga ambiri onse amene Yehova wandipatsa, Iye wasankha mwana wanga Solomoni kuti akhale pa mpando waufumu wa ufumu wa Yehova kuti alamulire Israeli.”
But also of my sones, for the Lord yaf to me many sones, he chees Salomon, my sone, that he schulde sitte in the troone of the rewme of the Lord on Israel.
6 Yehova anati kwa ine, “Solomoni mwana wako ndiye amene adzamanga nyumba yanga ndi mabwalo anga, pakuti Ine ndamusankha kuti akhale mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake.
And he seide to me, Salomon, thi sone, schal bilde myn hows, and myn auters; for Y haue chose hym to me in to a sone, and Y schal be to hym in to a fadir;
7 Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya ngati iye saleka kutsatira malamulo ndi malangizo anga, monga momwe zikuchitikira leromu.”
and Y schal make stidefast his rewme til in to with outen ende, if he schal contynue to do myn heestis and domes, as and to dai.
8 “Tsono lero ine ndikulamula inu pamaso pa Aisraeli onse ndi pa msonkhano wa Yehova, ndipo Mulungu wathu akumva: Mutsatire mosamala malamulo a Yehova Mulungu wathu, kuti dziko labwinoli likhale lanu ndi kuti mudzalipereke kwa zidzukulu zanu kukhala cholowa chawo kwamuyaya.”
Now therfor bifor al the cumpeny of Israel, `Y seie these thingis that suen in the heryng of God, kepe ye and seke ye alle the comaundementis of `youre Lord God, that ye haue in possessioun a good lond, and that ye leeue it to youre sones aftir you til in to with outen ende.
9 “Ndipo iwe mwana wanga Solomoni, umvere Mulungu wa abambo ako, umutumikire ndi mtima wodzipereka kwathunthu ndi mtima wako wonse, pakuti Yehova amasanthula mtima wa aliyense, ndipo amadziwa maganizo aliwonse a munthu. Ngati ufunafuna Yehova, Iye adzapezeka; koma ngati umutaya, Iye adzakukana kwamuyaya.
But thou, Salomon, my sone, knowe the God of thi fadir, and serue thou hym with perfit herte, and wilful soule; for the Lord serchith alle hertis, and vndirstondith alle thouytis of soulis; if thou sekist hym, thou schalt fynde hym; forsothe if thou forsakist hym, he schal caste thee awei with outen ende.
10 Tsopano ganizira bwino, pakuti Yehova wakusankha iwe kuti umange Nyumba ya Mulungu monga malo ake opatulika. Khala wamphamvu ndipo ugwire ntchito.”
Now therfor, for the Lord chees thee, for to bilde the hows of seyntuarie, be thou coumfortid, and parforme.
11 Kotero Davide anapatsa Solomoni mwana wake mapulani a khonde la Nyumba ya Mulungu, nyumba zake, mosungiramo katundu, zipinda zake zamʼmwamba, zipinda zamʼkati ndi malo a nsembe zopepesera machimo.
Forsothe Dauid yaf to Salomon, his sone, the discryuyng, `ether ensaumple, of the porche, and of the temple, and of celeris, and of the soler, and of closetis in pryuy places, and of the hows of propiciacioun, `that is, of mersi;
12 Iye anapatsa Solomoni mapulani a zonse zimene ankaziganizira za bwalo la Nyumba ya Yehova ndi zipinda zonse zozungulira, zipinda zosungiramo chuma cha Nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Yehova.
also and of alle thingis whiche he thouyte of the large places, and of chaumbris bi cumpas, in to the tresours of the hows of the Lord, and `in to the tresours of holi thingis,
13 Davide anamulangiza za magulu a ansembe ndi Alevi ndi ntchito yonse yotumikira mʼNyumba ya Yehova, komanso za zinthu zonse zogwirira ntchito potumikira.
and of the departyngis of preestis and of dekenes, in to alle the werkis of the hows of the Lord, and alle vessels of the seruyce of the temple of the Lord.
14 Iye anakonzeratu za kulemera kwa golide wopangira zida zonse zagolide zogwirira ntchito zosiyanasiyana, ndiponso kulemera kwa siliva wopangira zida zonse zasiliva zogwirira ntchito zosiyanasiyana:
Of gold in weiyte bi ech vessel of the seruyce, and of siluer, for dyuersitee of vessels, and of werkis;
15 kulemera kwa golide wopangira choyikapo nyale chagolide ndi nyale zake; ndiponso kulemera kwa siliva wa choyikapo nyale chilichonse ndi nyale zake, molingana ndi kagwiritsidwe ka choyikapo nyale chilichonse;
but also to goldun candilstikis, and to her lanternes, he yaf gold, for the mesure of ech candilstike and lanternes; also and in silueren candilstikis, and in her lanternes, he bitook the weiyte of siluer, for the dyuersite of mesure.
16 kulemera kwa golide wa tebulo iliyonse yoyikapo buledi wopatulika; kulemera kwa siliva wopangira matebulo asiliva;
Also and he yaf gold in to the bord of settyng forth, for the dyuersite of mesure, also and he yaf siluer in to othere siluerne boordis;
17 muyeso wa golide woyengeka bwino wopangira mafoloko, mbale ndi zotungira; muyeso wa golide wa beseni lililonse la siliva;
also to fleisch hookis, and viols, and censeris of pureste gold; and to litle goldun lyouns, for the maner of mesure, he departide a weiyte in to a litil lyoun and a litil lioun; also and in to siluerne liouns he departide dyuerse weiyte of siluer.
18 ndiponso muyeso wa golide wabwino wopangira guwa la zofukiza. Davide anamupatsanso ndondomeko ya mapangidwe a galeta, akerubi agolide atatambasula mapiko awo kuphimba Bokosi la Chipangano la Yehova.
Forsothe he yaf pureste gold to the auter, wherynne encense was brent, that a lickenesse of the cart of cherubyns, holdinge forth wyngis, and hilynge the arke of boond of pees of the Lord, schulde be maad therof.
19 Davide anati, “Zonsezi ndalemba kuchokera kwa Yehova, ndipo Iye wachita kuti ndimvetsetse zonse za mapulaniwa.”
Dauid seide, Alle thingis camen writun bi the hond of the Lord to me, that Y schulde vndirstonde alle the werkis of the saumpler.
20 Davide anatinso kwa mwana wake Solomoni, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima ndipo uchite ntchitoyi. Usachite mantha kapena kutaya mtima pakuti Yehova Mulungu wanga ali nawe. Iye sadzakukhumudwitsa kapena kukusiya mpaka ntchito yonse ya Nyumba ya Mulungu itatha.
And Dauid seide to Salomon, his sone, Do thou manli, and be thou coumfortid, and make; drede thou not `with outforth, nether drede thou `with ynne; for `my Lord God schal be with thee, and he schal not leeue thee, nether schal forsake thee, til thou performe al the werk of the seruyce of the hows of the Lord.
21 Magulu a ansembe ndi Alevi ndi okonzeka kugwira ntchito ya Nyumba ya Mulungu, ndipo munthu waluso aliyense wodzipereka adzakuthandiza pa ntchito yonse. Akuluakulu ndi anthu onse adzamvera chilichonse chomwe udzalamula.”
Lo! the departyngis of prestis and of dekenes, in to al the werk of the seruyce of the hows of the Lord, schulen stonde niy thee; and thei ben redi, and bothe the princes and the puple kunnen do alle thi comaundementis.

< 1 Mbiri 28 >