< 1 Mbiri 25 >

1 Davide ndi atsogoleri a asilikali anapatula ena mwa ana a Asafu, Hemani ndi Yedutuni ku utumiki wa uneneri pogwiritsa ntchito apangwe, azeze ndi ziwaya zamalipenga. Tsopano nawu mndandanda wa anthu amene ankagwira ntchito imeneyi:
David and the leaders of the army selected some of the sons of Asaph, Heman, and Jeduthun to prophesy with harps, with stringed instruments, and with cymbals. Here is the list of the men who performed this service:
2 Kuchokera kwa ana a Asafu: Zakuri, Yosefe, Netaniya ndi Asareli. Ana a Asafu amalamulidwa ndi Asafu ndipo amanenera moyangʼaniridwa ndi mfumu.
From the sons of Asaph: Zaccur, Joseph, Nethaniah, and Asharelah, the sons of Asaph, under the direction of Asaph, who prophesied under the king's supervision.
3 Kwa Yedutuni, kuchokera kwa ana ake: Gedaliya, Zeri, Yesaya, Simei, Hasabiya ndi Matitiya. Onse analipo 9 ndipo amayangʼaniridwa ndi Yedutuni abambo awo, amene amanenera pogwiritsa ntchito apangwe poyamika ndi kutamanda Yehova.
From the sons of Jeduthun: Gedaliah, Zeri, Jeshaiah, Shimei, Hashabiah, and Mattithiah, six in all, under the direction of their father Jeduthun, who played the harp for giving thanks and praising Yahweh.
4 Kwa Hemani, kuchokera kwa ana ake: Bukiya, Mataniya, Uzieli, Subaeli ndi Yerimoti; Hananiya, Hanani, Eliata, Gidaliti ndi Romamiti-Ezeri; Yosibakasa, Maloti, Hotiri ndi Mahazioti.
From the sons of Heman: Bukkiah, Mattaniah, Uzziel, Shubael, and Jerimoth, Hananiah, Hanani, Eliathah, Giddalti, Romamti-Ezer, Joshbekashah, Mallothi, Hothir, and Mahazioth.
5 Onsewa anali ana a Hemani mlosi wa mfumu. Iye anapatsidwa anawa potsata mawu a Mulungu akuti adzamukweza. Mulungu anapatsa Hemani ana aamuna 14 ndi ana aakazi atatu.
All these were the sons of Heman the king's prophet. God gave Heman fourteen sons and three daughters to lift up his horn.
6 Anthu onsewa ankayangʼaniridwa ndi makolo awo pa mayimbidwe a mʼNyumba ya Yehova. Iwowatu ankayimba ndi ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe potumikira mʼNyumba ya Mulungu. Koma Asafu, Yedutuni ndi Hemani amayangʼaniridwa ndi mfumu.
All these were under the direction of their fathers. They were musicians in Yahweh's house, with cymbals and stringed instruments as they served in God's house. Asaph, Jeduthun, and Heman were under the king's supervision.
7 Iwo pamodzi ndi abale awo onse ophunzitsidwa ndi aluso loyimbira Yehova chiwerengero chawo chinali 288.
They and their brothers who were skilled and trained to make music to Yahweh numbered 288.
8 Angʼonoangʼono ndi akulu omwe, mphunzitsi ndi wophunzira yemwe anachita maere pa ntchito zawo.
They cast lots for their duties, all alike, the same for the young as well as the old, the teacher as well as the student.
9 Maere woyamba amene anali a Asafu, anagwera Yosefe, ana ndi abale ake. 12 Maere achiwiri anagwera Gedaliya, ndi abale ake ndi ana ake. 12
Now regarding Asaph's sons: The first lot fell to Joseph's family; the second fell to Gedaliah's family, twelve persons in number;
10 Maere achitatu anagwera Zakuri, ana ake ndi abale ake. 12
the third fell to Zaccur, his sons and his relatives, twelve persons in number;
11 Maere achinayi anagwera Iziri, ana ake ndi abale ake. 12
the fourth fell to Izri, his sons and his relatives, twelve persons in number;
12 Maere achisanu anagwera Netaniya, ana ake ndi abale ake. 12
the fifth fell to Nethaniah, his sons and his relatives, twelve persons in number;
13 Maere achisanu ndi chimodzi anagwera Bukiya, ana ake ndi abale ake. 12
the sixth fell to Bukkiah, his sons and his relatives, twelve persons in number;
14 Maere achisanu ndi chiwiri anagwera Yesarela, ana ake ndi abale ake. 12
the seventh fell to Jesarelah, his sons and his relatives, twelve persons in number;
15 Maere achisanu ndi chitatu anagwera Yeshaya, ana ake ndi abale ake. 12
the eighth fell to Jeshaiah, his sons and his relatives, twelve persons in number;
16 Maere achisanu ndi chinayi anagwera Mataniya, ana ake ndi abale ake. 12
the ninth fell to Mattaniah, his sons and his relatives, twelve persons in number;
17 Maere a khumi anagwera Simei, ana ake ndi abale ake. 12
the tenth fell to Shimei, his sons and his relatives, twelve persons in number;
18 Maere a 11 anagwera Azareli, ana ake ndi abale ake. 12
the eleventh fell to Azarel, his sons and his relatives, twelve persons in number;
19 Maere a 12 anagwera Hasabiya, ana ake ndi abale ake. 12
the twelfth fell to Hashabiah, his sons and his relatives, twelve persons in number;
20 Maere a 13 anagwera Subaeli, ana ake ndi abale ake. 12
the thirteenth fell to Shubael, his sons and his relatives, twelve persons in number;
21 Maere a 14 anagwera Matitiya, ana ake ndi abale ake. 12
the fourteenth fell to Mattithiah, his sons and his relatives, twelve persons in number;
22 Maere a 15 anagwera Yeremoti, ana ake ndi abale ake. 12
the fifteenth fell to Jerimoth, his sons and his relatives, twelve persons in number;
23 Maere a 16 anagwera Hananiya, ana ake ndi abale ake. 12
the sixteenth fell to Hananiah, his sons and his relatives, twelve persons in number;
24 Maere a 17 anagwera Yosibakasa, ana ake ndi abale ake. 12
the seventeenth fell to Joshbekashah, his sons and his relatives, twelve persons in number;
25 Maere a 18 anagwera Hanani, ana ake ndi abale ake. 12
the eighteenth fell to Hanani, his sons and his relatives, twelve persons in number;
26 Maere a 19 anagwera Maloti, ana ake ndi abale ake. 12
the nineteenth fell to Mallothi, his sons and his relatives, twelve persons in number;
27 Maere a 20 anagwera Eliyata, ana ake ndi abale ake. 12
the twentieth fell to Eliathah, his sons and his relatives, twelve persons in number;
28 Maere a 21 anagwera Hotiri, ana ake ndi abale ake. 12
the twenty-first fell to Hothir, his sons and his relatives, twelve persons in number;
29 Maere a 22 anagwera Gidaliti, ana ake ndi abale ake. 12
the twenty-second fell to Giddalti, his sons and his relatives, twelve persons in number;
30 Maere a 23 anagwera Mahazioti, ana ake ndi abale ake. 12
the twenty-third fell to Mahazioth, his sons and his relatives, twelve persons in number;
31 Maere a 24 anagwera Romamiti-Ezeri, ana ake ndi abale ake 12.
the twenty-fourth fell to Romamti-Ezer, his sons and his relatives, twelve persons in number.

< 1 Mbiri 25 >