< 1 Mbiri 23 >

1 Davide atakalamba, ali ndi zaka zambiri, anayika Solomoni mwana wake kukhala mfumu ya Israeli.
Gdy więc Dawid był już stary i syty dni, ustanowił swego syna Salomona królem nad Izraelem.
2 Iye anasonkhanitsanso pamodzi atsogoleri onse a Israeli, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi.
I zgromadził wszystkich książąt Izraela oraz kapłanów i Lewitów.
3 Anawerenga Alevi kuyambira a zaka makumi atatu ndi kupitirirapo, ndipo chiwerengero cha amuna onse chinali 38,000.
Lewitów policzono od trzydziestu lat wzwyż, a ich liczba według głów wynosiła trzydzieści osiem tysięcy.
4 Davide anati, “Mwa amenewa, amuna 24,000 aziyangʼanira ntchito za mʼNyumba ya Mulungu ndipo 6,000 akhale akuluakulu ndi oweruza.
Spośród nich dwadzieścia cztery tysiące ustanowiono na służbę w domu PANA, a urzędników i sędziów było sześć tysięcy.
5 Amuna 4,000 akhale alonda a pa zipata ndipo 4,000 azitamanda Yehova ndi zipangizo zoyimbira zimene ndazipereka ndi cholinga chimenecho.”
Ponadto – cztery tysiące odźwiernych i cztery tysiące chwalących PANA na instrumentach, które sporządziłem – [powiedział Dawid] – ku uwielbieniu [Boga].
6 Davide anagawa Aleviwo mʼmagulumagulu motsatira ana a Levi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
Dawid podzielił ich na zmiany według synów Lewiego: Gerszona, Kehata i Merariego.
7 Ana a Geresoni: Ladani ndi Simei.
Z Gerszona [byli] Ladan i Szimei.
8 Ana a Ladani: Mtsogoleri Yehieli, Zetamu ndi Yoweli. Onse analipo atatu.
Synowie Ladana: pierwszy Jechiel, potem Zetam i Joel – [ci] trzej.
9 Ana a Simei: Selomoti, Haziyeli ndi Harani. Onse analipo atatu. Awa anali atsogoleri a mabanja a Ladani.
Synowie Szimejego: Szelomit, Chaziel i Haran – [ci] trzej [byli] naczelnikami rodów Ladana.
10 Ndipo ana a Simei anali: Yahati, Zina, Yeusi ndi Beriya. Awa anali ana a Semei. Onse analipo anayi.
A synowie Szimejego: Jachat, Zina, Jeusz i Beria. Ci czterej byli synami Szimejego.
11 Mtsogoleri anali Yahati, ndipo Ziza anali wachiwiri, koma Yeusi ndi Beriya analibe ana aamuna ambiri. Kotero iwo anawerengedwa ngati banja limodzi ndipo anapatsidwa ntchito imodzinso yofanana.
Jachat był pierwszy, a Ziza drugi. Ale Jeusz i Beria nie mieli wielu synów i dlatego zostali policzeni jako jeden ród.
12 Ana a Kohati: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Onse analipo anayi.
Synowie Kehata: Amram, Ishar, Chebron i Uzziel – czterej.
13 Ana a Amramu: Aaroni ndi Mose. Aaroni ndi zidzukulu zake anapatulidwa kwamuyaya kuti azipereka zinthu zopatulika kwambiri monga nsembe pamaso pa Yehova, komanso kuti azitumikira pamaso pake ndi kumadalitsa anthu mʼdzina lake kwamuyaya.
Synowie Amrama: Aaron i Mojżesz. Lecz Aaron został odłączony, aby poświęcić najświętsze rzeczy, on i jego synowie, aż na wieki – by spalać kadzidło przed PANEM, służyć mu i błogosławić w jego imieniu na wieki.
14 Ana a Mose munthu wa Mulungu anawerengedwa ngati gawo la fuko la Levi.
Ale synowie Mojżesza, męża Bożego, zostali zaliczeni do pokolenia Lewiego.
15 Ana a Mose: Geresomu ndi Eliezara.
Synowie Mojżesza: Gerszon i Eliezer.
16 Zidzukulu za Geresomu: Mtsogoleri anali Subaeli.
Synowie Gerszona: pierwszy Szebuel.
17 Zidzukulu za Eliezara: Mtsogoleri anali Rehabiya. Eliezara analibe ana ena aamuna, koma ana a Rehabiya anali ochuluka kwambiri.
Synowie Eliezera: pierwszy Rechabiasz. Eliezer nie miał innych synów, ale synowie Rechabiasza bardzo się rozmnożyli.
18 Ana a Izihari: Mtsogoleri anali Selomiti.
Synowie Ishara: pierwszy Szelomit.
19 Ana a Hebroni: Mtsogoleri anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, Yahazieli anali wachitatu ndipo Yekameamu anali wachinayi.
Synowie Chebrona: pierwszy Jeriasz, drugi Amariasz, trzeci Jachaziel, a czwarty Jekameam.
20 Ana a Uzieli: Mtsogoleri anali Mika ndipo wachiwiri anali Isiya.
Synowie Uzziela: pierwszy Mika i drugi Jeszijasz.
21 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Ana a Mahili: Eliezara ndi Kisi.
Synowie Merariego: Machli i Muszi. Synowie Machliego: Eleazar i Kisz.
22 Eliezara anamwalira wopanda ana aamuna. Iye anali ndi ana aakazi okhaokha. Abale awo, ana a Kisi, ndiwo amene anawakwatira.
I Eleazar umarł, nie mając synów, tylko córki. Pojęli je [za żony] synowie Kisza, ich bracia.
23 Ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yeremoti. Onse analipo atatu.
Synowie Musziego: Machli, Eder i Jeremot – trzej.
24 Izi zinali zidzukulu za Levi mwa mabanja awo, atsogoleri a mabanja monga momwe analembedwera mayina awo ndi monga momwenso anawerengedwera, banja lililonse pa lokha. Awa ndi anthu ogwira ntchito oyambira zaka makumi awiri zobadwa kapena kupitirirapo, amene amatumikira mʼNyumba ya Yehova.
To są synowie Lewiego według swych rodów, głów rodzin, policzeni według liczby imion, głowa po głowie, którzy pełnili służbę w domu PANA od lat dwudziestu wzwyż.
25 Popeza Davide anati, “Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli, wapereka mpumulo kwa anthu ake ndipo wabwera kudzakhala mu Yerusalemu kwamuyaya,
Dawid bowiem powiedział: PAN, Bóg Izraela, dał odpoczynek swemu ludowi i będzie mieszkał w Jerozolimie na wieki.
26 sikofunikiranso kuti Alevi azinyamula tenti kapena zipangizo za chipembedzo.”
A Lewici już nie będą nosić przybytku ani wszelkich jego naczyń do jego obsługi.
27 Potsata malangizo otsiriza a Davide, Alevi anawerengedwa kuyambira amuna a zaka makumi awiri zakubadwa kapena kupitirirapo.
Według ostatnich postanowień Dawida Lewici zostali policzeni od lat dwudziestu wzwyż;
28 Ntchito ya Alevi inali kuthandiza zidzukulu za Aaroni pa ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova monga kuyangʼanira mabwalo, zipinda zamʼmbali, kuyeretsa zinthu zonse zachipembedzo, ndiponso kuchita ntchito zina za mʼnyumba ya Mulungu.
Ich stanowisko bowiem polegało na posługiwaniu synom Aarona w służbie domu PANA: na dziedzińcach, w komnatach, przy oczyszczaniu wszelkich rzeczy poświęconych i przy pracy wokół służby domu Bożego;
29 Iwo amayangʼanira buledi amene amayikidwa pa tebulo, ufa wa nsembe yachakudya, timitanda ta buledi wopanda yisiti: kuphika ndi kusakaniza, ndiponso miyeso yonse ndi kukula kwake.
I przy chlebie pokładnym, przy mące na ofiarę z pokarmów, przy plackach niekwaszonych, przy tym, co pieczone, i tym, co smażone, i przy wszystkim, co ważone i mierzone.
30 Iwo amayimiriranso mmawa uliwonse kuthokoza ndi kutamanda Yehova. Amachitanso chomwecho madzulo,
Mieli stawać każdego poranka, by dziękować PANU i wychwalać go, i tak samo wieczorem;
31 ndiponso popereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa Sabata ndi pa chikondwerero cha Mwezi Watsopano, ndi pa nthawi yosankhidwa ya Chikondwerero. Iwo amatumikira pamaso pa Yehova nthawi zonse mwa chiwerengero chawo ndi momwe analangizidwira.
Ponadto, mieli składać PANU wszelkie całopalenia w każdy szabat, w czasie nowiu księżyca i w uroczyste święta, według liczby [wynikającej z] ustalonego porządku – ustawicznie przed PANEM.
32 Ndipo kotero Alevi anachita ntchito yawo ya ku tenti ya msonkhano ya ku Malo Opatulika ndiponso molamulidwa ndi abale awo, zidzukulu za Aaroni, pa ntchito ya mʼNyumba ya Yehova.
I mieli pełnić straż przy Namiocie Zgromadzenia, straż przy świątyni i straż przy synach Aarona, swych braci, w służbie domu PANA.

< 1 Mbiri 23 >