< 1 Mbiri 20 >

1 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Yowabu anatsogolera gulu la ankhondo. Iye anawononga Aamoni, kenaka anapita ku mzinda wa Raba ndipo anawuzungulira, koma Davide anatsala ku Yerusalemu. Yowabu anathira nkhondo mzinda wa Raba ndipo anawuwononga.
A kad proðe godina, u vrijeme kad carevi idu na vojsku, Joav izvede vojsku, te potiraše zemlju sinova Amonovijeh, i došavši opkoli Ravu; a David bješe ostao u Jerusalimu. I Joav osvoji Ravu i raskopa je.
2 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Ndipo Davide anavala chipewacho. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
I David uze caru njihovu s glave krunu, i naðe da poteže talanat zlata, i drago kamenje bješe u njoj; i metnuše je na glavu Davidu, i odnese iz grada plijen vrlo velik.
3 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka Davide pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
A narod što bijaše u njemu izvede i isijeèe ih pilama i gvozdenijem branama i sjekirama. I tako uèini David svijem gradovima sinova Amonovijeh. Potom se vrati David sa svijem narodom u Jerusalim.
4 Patapita nthawi, nkhondo inayambika pakati pa Aisraeli ndi Afilisti ku Gezeri. Nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Sipai, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai, ndipo Afilisti anagonja.
A poslije toga nasta rat u Gezeru s Filistejima; tada Sivehaj Husaæanin ubi Sifaja koji bijaše roda divovskoga, i biše pokoreni.
5 Pa nkhondo inanso ndi Afilisti, Elihanani mwana wa Yairi anapha Lahimi mʼbale wake wa Goliati Mgiti, amene mkondo wake unali ngati ndodo yowombera nsalu.
Nasta opet rat s Filistejima, u kom Elhanan sin Jairov ubi Lamiju brata Golijata Getejina, kojemu kopljaèa bijaše kao vratilo.
6 Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati, panali munthu wina wamtali kwambiri, wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
I opet nasta rat u Gatu, gdje bijaše jedan èovjek vrlo visok, koji imaše po šest prsta, skupa dvadeset i èetiri; i on bijaše roda divovskoga.
7 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
I ružaše Izrailja, te ga ubi Jonatan sin Samaje brata Davidova.
8 Anthu amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.
Ti bijahu sinovi istoga diva iz Gata, i pogiboše od ruke Davidove i od ruke sluga njegovijeh.

< 1 Mbiri 20 >